< Zachariáš 7 >

1 Potom stalo se léta čtvrtého Daria krále, stalo se slovo Hospodinovo k Zachariášovi, čtvrtého dne měsíce devátého, kterýž jest Kislef,
Pa chaka chachinayi cha Mfumu Dariyo, pa tsiku lachinayi la Kisilevi, mwezi wachisanu ndi chinayi, Yehova anayankhula ndi Zekariya.
2 Když poslal do domu Božího Sarezer a Regemmelech, i muži jeho, aby se kořili tváři Hospodinově,
Anthu a ku Beteli anali atatuma Sarezeri ndi Regemu-Meleki pamodzi ndi anthu awo, kuti akapemphe chifundo kwa Yehova
3 A aby mluvili k kněžím, kteříž byli v domě Hospodina zástupů, i k prorokům, řkouce: Budeme-li plakati měsíce pátého, oddělujíce se, jako jsme činili již po mnoho let?
pokafunsa kwa ansembe a ku Nyumba ya Yehova Wamphamvuzonse ndi aneneri kuti, “Kodi ine ndizilira ndi kusala zakudya pa mwezi wachisanu, monga mmene ndakhala ndikuchitira pa zaka zambiri?”
4 I stalo se slovo Hospodina zástupů ke mně, řkoucí:
Pamenepo Yehova Wamphamvuzonse anayankhula nane kuti,
5 Rci všemu lidu této země i kněžím takto: Když jste se postívali a kvílili, pátého a sedmého měsíce, a to po sedmdesáte let, zdaliž jste se opravdu mně, mně, pravím, postili?
“Funsa anthu onse a mʼdziko ndi ansembe kuti, ‘Pamene munkasala zakudya pa mwezi wachisanu ndi wachisanu ndi chiwiri pa zaka 70 zapitazi, kodi munkasala chifukwa cha Ine?
6 A když jíte aneb pijete, zdaliž ne pro sebe jíte a ne pro sebe pijete?
Ndipo pamene munkadya ndi kumwa, kodi simunkachita zimenezi podzisangalatsa nokha?
7 Zdaliž tato nejsou slova, kteráž prohlásil Hospodin skrze proroky předešlé, když ještě Jeruzalém seděl bezpečně a užíval pokoje, i města jeho vůkol něho, a lid v straně polední i na rovinách bydlil?
Kodi awa si mawu amene Yehova ankanena kudzera mwa aneneri oyamba aja pamene Yerusalemu ndi mizinda yake yozungulira anali pa mtendere ndi pa ulemerero, ndi pamene Negevi ndi ku madera akumadzulo a mʼmbali mwa phiri munali anthu?’”
8 I stalo se slovo Hospodinovo k Zachariášovi, řkoucí:
Ndipo Yehova anayankhulanso ndi Zekariya kuti,
9 Takto mluvíval Hospodin zástupů, řka: Soud pravý vynášejte, a milosrdenství a lítosti dokazujte jeden každý k bližnímu svému.
“Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Muziweruza molungama; muzichitirana chifundo ndi kumverana chisoni.
10 A vdovy ani sirotka, příchozího ani chudého neutiskejte, a zlého žádný bližnímu svému neobmýšlejte v srdci svém.
Musamazunze akazi amasiye kapena ana amasiye, alendo kapena osauka. Musamaganizirane zoyipa mʼmitima mwanu.’
11 Ale nechtěli pozorovati, a nastavili ramene urputného, a uši své obtížili, aby neslyšeli.
“Koma makolo anu anakana kumvera uthenga umenewu; anawumitsa mtima nandifulatira, natseka makutu awo kuti asamve.
12 A srdce své učinili kámen přetvrdý, aby neslyšeli zákona toho a slov těch, kteráž posílal Hospodin zástupů Duchem svým skrze proroky předešlé. Pročež přišel hněv veliký od Hospodina zástupů.
Anawumitsa mitima yawo ngati mwala wa sangalabwi ndipo sanamvere lamulo kapena mawu amene Yehova Wamphamvuzonse anawatumiza mwa Mzimu wake kudzera mwa aneneri oyamba aja. Kotero Yehova Wamphamvuzonse anakwiya kwambiri.
13 Nebo stalo se, že jakož volajícího neslyšeli, tak když volali, neslyšel jsem, praví Hospodin zástupů.
“‘Pamene ndinawayitana, iwo sanamvere; choncho pamene iwo anandiyitana, Ine sindinamverenso,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.
14 A vichřicí rozptýlil jsem je mezi všecky ty národy, kterýchž neznali, a země tato spustla po nich, tak že nebylo žádného, kdo by tudy chodil, a tak přivedli zemi žádoucí na spuštění.
‘Ndinawamwaza ndi kamvuluvulu pakati pa mitundu yonse ya anthu, kumene anali alendo. Dziko lawo linatsala litasakazidwa kwambiri kotero kuti palibe amene amabwera kapena kupitamo. Umu ndi mmene anasandutsira dziko labwino kukhala chipululu.’”

< Zachariáš 7 >