< Žalmy 92 >

1 Žalm a píseň, ke dni sobotnímu. Dobré jest oslavovati Hospodina, a žalmy zpívati jménu tvému, ó Nejvyšší,
Salimo. Nyimbo ya pa tsiku la Sabata. Nʼkwabwino kutamanda Yehova ndi kuyimbira nyimbo dzina lanu, Inu Wammwambamwamba,
2 Zvěstovati každé jitro milosrdenství tvé, a pravdu tvou každé noci,
Kulengeza chikondi chanu mmawa, ndi kukhulupirika kwanu nthawi ya usiku,
3 Při nástroji o desíti strunách, při loutně, a při harfě s písničkou.
kuyimbira nyimbo choyimbira cha zingwe khumi ndi mayimbidwe abwino a zeze.
4 Nebo jsi mne rozveselil, Hospodine, skutky svými, o skutcích rukou tvých zpívati budu.
Pakuti Inu mumandisangalatsa ndi ntchito zanu, Inu Yehova; Ine ndikuyimba mwachimwemwe pa ntchito ya manja anu.
5 Jak velicí jsou skutkové tvoji, Hospodine! Velmi hluboká jsou myšlení tvá.
Ndi yayikuludi ntchito yanu Yehova, maganizo anu ndi ozamadi!
6 Člověk hovadný nezná toho, aniž blázen rozumí tomu,
Munthu wopanda nzeru sadziwa, zitsiru sizizindikira,
7 Že vyrostají bezbožní jako bylina, a kvetou všickni činitelé nepravosti, aby vyhlazeni byli na věky.
kuti ngakhale anthu oyipa aphuka ngati udzu ndipo anthu onse ochita zoyipa apindula, adzawonongedwa kwamuyaya.
8 Ty pak, ó Nejvyšší, že na věky jsi Hospodin.
Koma Inu Yehova, ndinu wokwezedwa kwamuyaya.
9 Nebo aj, nepřátelé tvoji, Hospodine, nebo aj, nepřátelé tvoji zahynou; rozptýleni budou všickni činitelé nepravosti.
Zoonadi adani anu Yehova, zoonadi adani anu adzawonongeka; onse ochita zoyipa adzabalalitsidwa.
10 Můj pak roh vyzdvihneš jako jednorožcův, pokropen budu olejem novým.
Inu mwakweza nyanga yanga ngati nyanga ya njati; mafuta abwino akhuthulidwa pamutu wanga.
11 I podívá se oko mé na ty, jenž mne špehují, a o těch nešlechetnících, jenž proti mně povstávají, ušima svýma uslyším.
Maso anga aona kugonjetsedwa kwa olimbana nane, makutu anga amva za kugwa kwa amaliwongo anga oyipa.
12 Spravedlivý jako palma kvésti bude, a jako cedr na Libánu rozloží se.
Anthu olungama adzaphuka ngati mtengo wa mgwalangwa, adzakula ngati mkungudza wa ku Lebanoni;
13 Štípení v domě Hospodinově v síňcích Boha našeho kvésti budou.
odzalidwa mʼnyumba ya Yehova, adzakula bwino mʼmabwalo a Mulungu wathu.
14 Ještě i v šedinách ovoce ponesou, spanilí a zelení budou,
Iwo adzaberekabe zipatso mu ukalamba wawo, adzakhala anthete ndi obiriwira,
15 Aby to zvěstováno bylo, že přímý jest Hospodin, skála má, a že nepravosti žádné při něm není.
kulengeza kuti, “Yehova ndi wolungama; Iye ndiye Thanthwe langa, ndipo mwa Iye mulibe choyipa.”

< Žalmy 92 >