< Žalmy 74 >
1 Vyučující, Azafův. Proč, ó Bože, nás tak do konce zamítáš? Proč roznícena jest prchlivost tvá proti stádci pastvy tvé?
Ndakatulo ya Asafu. Nʼchifukwa chiyani mwatitaya ife kwamuyaya, Inu Mulungu? Chifukwa chiyani mkwiyo wanu ukutukutira pa nkhosa za busa lanu?
2 Rozpomeň se na shromáždění své, jehož jsi od starodávna dobyl a vykoupil, na proutek dědictví svého, na Sion horu tuto, na níž přebýváš.
Kumbukirani anthu amene munawagula kalekale, fuko la cholowa chanu, limene Inu munaliwombola, phiri la Ziyoni, kumene inuyo mumakhala.
3 Přispějž k hrozným pustinám. Jak všecko pohubil nepřítel v svatyni!
Tembenuzani mapazi kuloza ku mabwinja awa amuyaya chiwonongeko ichi chonse mdani wabweretsa pa malo opatulika.
4 Řvali nepřátelé tvoji u prostřed shromáždění tvých, a na znamení toho zanechali množství korouhví svých.
Adani anu anabangula pa malo pamene Inu munkakumana nafe; anayimika mbendera zawo monga zizindikiro zachigonjetso.
5 Za hrdinu jmín byl ten, kterýž co nejvýše zdvihl sekeru, roubaje vazbu dříví jeho.
Iwo anachita ngati anthu oti anyamula mbendera zawo kuti adule mitengo mʼnkhalango.
6 A nyní již řezby jeho napořád sekerami a palicemi otloukají.
Kenaka anaphwanya ndi nkhwangwa ndi akasemasema awo zonse zimene tinapachika.
7 Uvrhli oheň do svatyně tvé, na zem zřítivše, poškvrnili příbytku jména tvého.
Iwo anatentha malo anu opatulika mpaka kuwagwetsa pansi; anadetsa malo okhalamo dzina lanu.
8 Řekli v srdci svém: Vyhubme je napořád. Takž vypálili všecky stánky Boha silného v zemi.
Ndipo anati mʼmitima yawo, “Tawatha kwathunthu.” Anatentha malo aliwonse amene Mulungu amapembedzedwerako mʼdzikomo.
9 Znamení svých nevidíme, jižť není proroka, aniž jest mezi námi, kdo by věděl, dokud to stane.
Ife sitinapatsidwe chizindikiro chodabwitsa; palibe aneneri amene atsala ndipo palibe aliyense wa ife akudziwa kuti izi zidzatenga nthawi yayitali bwanji.
10 I dokudž, ó Bože, útržky činiti bude odpůrce? A nepřítel ustavičně-liž rouhati se bude jménu tvému?
Kodi mpaka liti, mdani adzanyoze Inu Mulungu? Kodi amaliwongowa adzapeputsa dzina lanu kwamuyaya?
11 Proč zdržuješ ruku svou, a pravice své z lůna svého nevzneseš?
Chifukwa chiyani mukubweza dzanja lanu lamanja? Litulutseni kuchoka pachifuwa chanu ndipo muwawononge!
12 Však jsi ty, Bože, král můj od starodávna, působíš hojné spasení u prostřed země.
Koma Inu Mulungu, ndinu Mfumu yanga kuyambira kalekale; Mumabweretsa chipulumutso pa dziko lapansi.
13 Ty silou svou rozdělil jsi moře, a potřels hlavy draků u vodách.
Ndinu amene munagawa nyanja ndi mphamvu yanu; munathyola mitu ya zirombo za mʼmadzi.
14 Ty jsi potřel hlavu Leviatanovi, dal jsi jej za pokrm lidu na poušti.
Ndinu amene munaphwanya mitu ya Leviyatani ndi kuyipereka ngati chakudya cha zirombo za mʼchipululu.
15 Ty jsi otevřel vrchoviště a potoky, ty jsi osušil i řeky prudké.
Ndinu amene munatsekula akasupe ndi mitsinje, munawumitsa mitsinje imene siphwa nthawi zonse.
16 Tvůjť jest den, tvá jest také i noc, světlo i slunce ty jsi učinil.
Masana ndi anu ndipo usiku ndi wanunso; Inuyo munakhazikitsa dzuwa ndi mwezi.
17 Ty jsi založil všecky končiny země, léto i zimy ty jsi sformoval.
Ndinu amene munakhazikitsa malire onse a dziko lapansi; munakhazikitsa chilimwe ndi dzinja.
18 Rozpomeniž se na to, že útržky činil ten odpůrce Hospodinu, a lid bláznivý jak se jménu tvému rouhal.
Kumbukirani momwe mdani wakunyozerani Inu Yehova, momwe anthu opusa apeputsira dzina lanu.
19 Nevydávejž té zběři duše hrdličky své, na stádce chudých svých nezapomínej se na věky.
Musapereke moyo wa nkhunda yanu ku zirombo zakuthengo; nthawi zonse musayiwale miyoyo ya anthu anu osautsidwa.
20 Ohlédni se na smlouvu; nebo plní jsou i nejtmavější koutové země peleší ukrutnosti.
Mukumbukire pangano lanu, pakuti malo obisika a mʼdziko asanduka mochitira zachiwawa zochuluka.
21 Nechažť bídní neodcházejí s hanbou, chudý a nuzný ať chválí jméno tvé.
Musalole kuti osautsidwa abwerere mwamanyazi; osauka ndi osowa atamande dzina lanu.
22 Povstaniž, ó Bože, a veď při svou, rozpomeň se na pohanění, kteréžť se děje od nesmyslných na každý den.
Dzukani Inu Mulungu ndipo dzitetezeni pa mlandu; kumbukirani momwe opusa akukunyozerani tsiku lonse.
23 Nezapomínej se na vykřikování svých nepřátel, a na hluk proti tobě povstávajících, kterýž se silí ustavičně.
Musalekerere phokoso la otsutsana nanu, chiwawa cha adani anu, chimene chikumveka kosalekeza.