< Žalmy 71 >

1 V tebeť, Hospodine, doufám, nechť nejsem zahanben na věky.
Mwa Inu Yehova ine ndathawiramo; musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
2 Vedlé spravedlnosti své vytrhni mne, a vyprosť mne; nakloň ke mně ucha svého, a spas mne.
Mundilanditse ndi kundipulumutsa mwa chilungamo chanu, mutchere khutu lanu ndi kundipulumutsa.
3 Budiž mi skalou obydlí, na niž bych ustavičně utíkal; přikázal jsi ostříhati mne, nebo skála má i pevnost má ty jsi.
Mukhale thanthwe langa lothawirapo, kumene ine nditha kupita nthawi zonse; lamulani kuti ndipulumuke, pakuti Inu ndinu thanthwe langa ndi linga langa.
4 Bože můj, vytrhni mne z ruky bezbožníka, z ruky převráceného a násilníka.
Landitseni Inu Mulungu wanga, kuchoka mʼdzanja la oyipa, kuchoka mʼdzanja la oyipa ndi anthu ankhanza.
5 Nebo ty jsi má naděje, Pane; Hospodine, v tebeť doufám od své mladosti.
Pakuti Inu mwakhala chiyembekezo changa, Inu Ambuye Wamphamvuzonse, chilimbikitso changa kuyambira ndili mwana.
6 Na tebe jsem zpolehl hned od života, z břicha matky mé ty jsi mne vyvedl, v tobě jest chvála má vždycky.
Kuyambira pamene ndinabadwa, ndakhala ndikudalira Inu; Inu munanditulutsa mʼmimba mwa amayi anga, ndipo ndidzakupembedzani nthawi zonse.
7 Jako zázrak byl jsem mnohým, a však ty jsi mé silné doufání.
Ine ndakhala chinthu chodabwitsa kwa anthu ambiri koma Inu ndinu wonditchinjiriza wamphamvu.
8 Ó ať jsou naplněna ústa má chválením tebe, přes celý den slavením tebe.
Pakamwa panga padzaza ndi matamando anu, kulengeza ulemerero wanu tsiku lonse.
9 Nezamítejž mne v věku starosti; když zhyne síla má, neopouštějž mne.
Musanditaye pamene ndakalamba; musandisiye pamene mphamvu zanga zatha.
10 Nebo mluvili nepřátelé moji proti mně, a ti, jenž střehou duše mé, radili se spolu,
Pakuti adani anga ayankhula motsutsana nane; iwo amene amadikira kuti andiphe amapangana pamodzi.
11 Pravíce: Bůh jej opustil, hoňte a popadněte jej, nebo kdo by ho vytrhl, není žádného.
Iwo amati, “Mulungu wamusiya; mutsatireni ndi kumugwira, pakuti palibe amene adzamupulumutse.”
12 Bože, nevzdalujž se ode mne, Bože můj, přispějž mi na pomoc.
Musakhale kutali ndi ine Inu Mulungu, bwerani msanga, Inu Mulungu wanga; thandizeni.
13 Nechť jsou zahanbeni, a zhynou protivníci duše mé; přikryti buďte lehkostí a hanbou, kteříž hledají pádu mého.
Ondineneza anga awonongeke mwa manyazi, iwo amene akufuna kundipweteka avale chitonzo ndi manyazi.
14 Já pak ustavičně čekati, a vždy víc a víc tě chváliti budu.
Koma ine ndidzakhala ndi chiyembekezo mwa Inu nthawi zonse, ndidzakutamandani mowirikizawirikiza.
15 Ústa má budou vypravovati spravedlnost tvou, každého dne spasení tvé, ačkoli mu počtu nevím.
Pakamwa panga padzafotokoza za chilungamo chanu, za chipulumutso chanu tsiku lonse, ngakhale sindikudziwa muyeso wake.
16 Přistoupě k všelijaké moci Panovníka Hospodina, připomínati budu tvou vlastní spravedlnost.
Ndidzabwera ndi kulengeza za machitidwe amphamvu zanu Inu Ambuye Wamphamvuzonse. Ndidzalengeza chilungamo chanu, chanu chokha.
17 Bože, učinil jsi mne od mladosti mé, a až po dnes vypravuji o divných činech tvých.
Kuyambira ubwana wanga, Inu Mulungu mwakhala mukundiphunzitsa, ndipo mpaka lero ine ndikulengeza za ntchito zanu zodabwitsa
18 Protož také i do starosti a šedin, Bože, neopouštěj mne, až v známost uvedu rámě tvé tomuto věku, a všechněm potomkům sílu tvou.
Ngakhale pamene ndakalamba ndipo imvi zili mbuu musanditaye Inu Mulungu, mpaka nditalengeza mphamvu zanu kwa mibado yonse yakutsogolo.
19 Nebo spravedlnost tvá, Bože, vyvýšená jest, provodíš zajisté věci veliké. Bože, kdo jest podobný tobě?
Mphamvu zanu ndi kulungama kwanu zimafika mpaka kumwambamwamba. Ndani wofanana nanu Inu Mulungu, amene mwachita zazikulu?
20 Kterýž ač jsi mi dal okusiti úzkostí velikých a hrozných, však zase k životu navrátíš mne, a z propastí země zase mne vyzdvihneš.
Ngakhale mwandionetsa mavuto ambiri owawa, mudzabwezeretsanso moyo wanga; kuchokera kunsi kwa dziko lapansi, mudzandiukitsanso.
21 Rozmnožíš důstojnost mou, a zase utěšíš mne.
Inu mudzachulukitsa ulemu wanga ndi kunditonthozanso.
22 I jáť také budu tě slaviti na nástroji hudebném, i pravdu tvou, Bože můj; žalmy tobě zpívati budu na harfě, ó svatý Izraelský.
Ndidzakutamandani ndi zeze chifukwa cha kukhulupirika kwanu Mulungu, ndidzayimba matamando kwa Inu ndi pangwe, Inu Woyera wa Israeli.
23 Plésati budou rtové moji, když žalmy zpívati budu tobě, i duše má, kterouž jsi vykoupil.
Milomo yanga idzafuwula ndi chimwemwe pamene ndidzayimba matamando kwa Inu amene mwandiwombola.
24 Nadto i jazyk můj každý den vypravovati bude spravedlnost tvou; nebo se zastyděti a zahanbiti musili ti, jenž mého pádu hledali.
Lilime langa lidzafotokoza za ntchito zanu zachilungamo tsiku lonse, pakuti iwo amene amafuna kundipweteka achititsidwa manyazi ndi kusokonezedwa.

< Žalmy 71 >