< Žalmy 68 >

1 Přednímu z kantorů, Davidův žalm k zpívání. Povstane Bůh, a rozprchnou se nepřátelé jeho, a utekou od tváři jeho ti, kteříž ho mají v nenávisti.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Adzuke Mulungu, adani ake amwazikane; adani ake athawe pamaso pake.
2 Jakož rozehnán bývá dým, tak je rozženeš; jakož se rozplývá vosk před ohněm, tak bezbožní zahynou před tváří Boží.
Monga momwe mphepo imachotsera utsi; Inu muwawulutsire kutali. Monga phula limasungunukira pa moto, oyipa awonongeke pamaso pa Mulungu.
3 Spravedliví pak veselíce se, poskakovati budou před Bohem, a plésati budou radostí.
Koma olungama asangalale ndi kukondwera pamaso pa Mulungu; iwo akondwere ndi kusangalala.
4 Prozpěvujte Bohu, žalmy zpívejte jménu jeho, vyrovnejte cestu tomu, kterýž se vznáší na oblacích. Hospodin jest jméno jeho, plésejtež před ním.
Imbirani Mulungu imbirani dzina lake matamando, mukwezeni Iye amene amakwera pa mitambo; dzina lake ndi Yehova ndipo sangalalani pamaso pake.
5 Otec jest sirotků a ochránce vdov, Bůh v příbytku svatém svém.
Atate wa ana amasiye, mtetezi wa akazi amasiye, ndiye Mulungu amene amakhala mʼmalo oyera.
6 Bůh samotné rozmnožuje v domy, vyvodí vězně z okovů, zpurní pak bydliti musejí v zemi vyprahlé.
Mulungu amakhazikitsa mtima pansi osungulumwa mʼmabanja, amatsogolera amʼndende ndi kuyimba; koma anthu osamvera amakhala ku malo owuma a dziko lapansi.
7 Bože, když jsi předcházel lid svůj, když jsi kráčel po poušti, (Sélah)
Pamene munatuluka kutsogolera anthu anu, Inu Mulungu, pamene munayenda kudutsa chipululu,
8 Země se třásla, též i nebesa rozplývala se před tváří Boží, i ta hora Sinai před přítomností Boží, Boha Izraelského.
dziko lapansi linagwedezeka, miyamba inakhuthula pansi mvula, pamaso pa Mulungu, Mmodzi uja wa ku Sinai. Pamaso pa Mulungu, Mulungu wa Israeli.
9 Deštěm štědrosti hojné skropoval jsi, Bože, dědictví své, a když zemdlívalo, ty jsi je zase očerstvoval.
Munapereka mivumbi yochuluka, Inu Mulungu; munatsitsimutsa cholowa chanu cholefuka.
10 Zástupové tvoji přebývají v něm, kteréžs ty nastrojil dobrotivostí svou pro chudého, ó Bože.
Anthu anu anakhala mʼmenemo ndipo munapatsa anthu osauka zimene zinkawasowa chifukwa cha ubwino wanu Mulungu.
11 Pán dal slovo své, i těch, kteréž potěšeně zvěstovaly, zástup veliký, řkoucích:
Ambuye analengeza mawu, ndipo gulu linali lalikulu la iwo amene anapita kukawafalitsa;
12 Králové s vojsky utíkali, utíkali, a doma hlídající dělily kořisti.
“Mafumu ndi ankhondo anathawa mwaliwiro; mʼmisasa anthu anagawana zolanda pa nkhondo.
13 Ačkoli jste mezi kotly ležeti musili, však jste jako holubice, mající křídla postříbřená, a brky z ryzího zlata.
Ngakhale mukugona pakati pa makola a ziweto, mapiko a nkhunda akutidwa ndi siliva, nthenga zake ndi golide wonyezimira.”
14 Když Všemohoucí rozptýlí krále v této zemi, zbělíš jako sníh na hoře Salmon.
Pamene Wamphamvuzonse anabalalitsa mafumu mʼdziko, zinali ngati matalala akugwa pa Zalimoni.
15 Hoře veliké, hoře v Bázan, hoře pahrbkovaté, hoře v Bázan.
Mapiri a Basani ndi mapiri aulemerero; mapiri a Basani, ndi mapiri a msonga zambiri.
16 Pročež vyskakujete, hory pahrbkovaté? Na tétoť hoře zalíbilo se Bohu přebývati, jistě žeť na ní Hospodin na věky přebývati bude.
Muyangʼaniranji mwansanje inu mapiri a msonga zambiri, pa phiri limene Mulungu analisankha kuti azilamulira, kumene Yehova mwini adzakhalako kwamuyaya?
17 Vozů Božích jest dvadceti tisíců, mnoho tisíců andělů, Pán pak mezi nimi jako na Sinai v svatyni přebývá.
Magaleta a Mulungu ndi osawerengeka, ndi miyandamiyanda; Ambuye wabwera kuchokera ku Sinai, walowa mʼmalo ake opatulika.
18 Vstoupil jsi na výsost, jaté jsi vedl vězně, vzal jsi dary pro lidi. I nejzpurnější k přebývání s námi, Hospodine Bože, přivozuješ.
Pamene Inu munakwera mmwamba, munatsogolera a mʼndende ambiri; munalandira mphatso kuchokera kwa anthu, ngakhale kuchokera kwa owukira, kuti Inu Mulungu, mukhale kumeneko.
19 Požehnaný Pán, každého dne nás osýpá dary svými, Bůh silný spasení našeho. (Sélah)
Matamando akhale kwa Ambuye, kwa Mulungu Mpulumutsi wathu amene tsiku ndi tsiku amasenza zolemetsa zathu.
20 Onť jest Bůh silný náš, Bůh silný k hojnému spasení. Hospodin Pán z smrti vyvodí.
Mulungu wathu ndi Mulungu amene amapulumutsa; Ambuye Wamphamvuzonse ndiye amene amatipulumutsa ku imfa.
21 Raní zajisté Bůh hlavu nepřátel svých, a vrch hlavy vlasatý chodícího v hříších svých.
Ndithu Mulungu adzaphwanya mitu ya adani ake, zipewa za ubweya za iwo amene amapitiriza kuchita machimo awo.
22 Řekltě Pán: Zaseť vyvedu své, jako z Bázan, zase vyvedu z hlubokosti mořské.
Ambuye akunena kuti, “Ndidzawabweretsa kuchokera ku Basani; ndidzawabweretsa kuchokera ku nyanja zozama.
23 A protož noha tvá zbrocena bude ve krvi, i jazyk psů tvých krví nepřátelskou.
Kuti muviyike mapazi anu mʼmagazi a adani anu, pamene malilime a agalu anu akudyapo gawo lawo.”
24 Spatřili slavné jití tvé, Bože, jití silného Boha mého a krále mého v svatyni.
Mayendedwe aulemu a anthu anu aonekera poyera, Inu Mulungu; mayendedwe olemekeza Mulungu wanga ndi Mfumu yanga yokalowa mʼmalo opatulika.
25 Napřed šli zpěváci, z zadu hrající na nástroje hudebné, u prostřed pak děvečky bubnující.
Patsogolo pali oyimba nyimbo pakamwa, pambuyo pawo oyimba nyimbo ndi zipangizo; pamodzi ndi iwo pali atsikana akuyimba matambolini.
26 V shromážděních dobrořečte Bohu Pánu, kteříž jste z národu Izraelského.
Tamandani Mulungu mu msonkhano waukulu; tamandani Yehova mu msonkhano wa Israeli.
27 Tu ať jest Beniamin maličký, kterýž je opanoval, tu knížata z Judy a houfové jejich, knížata z Zabulona, i knížata z Neftalíma.
Pali fuko lalingʼono la Benjamini, kuwatsogolera, pali gulu lalikulu la ana a mafumu a Yuda, ndiponso pali ana a mafumu a Zebuloni ndi Nafutali.
28 Obdařil tě Bůh tvůj silou. Potvrdiž, Bože, což jsi mezi námi vzdělal,
Kungani mphamvu zanu Mulungu; tionetseni nyonga zanu, Inu Mulungu, monga munachitira poyamba.
29 Z chrámu svého nad Jeruzalémem, do něhož tobě přinášeti budou králové dary.
Chifukwa cha Nyumba yanu ku Yerusalemu, mafumu adzabweretsa kwa Inu mphatso.
30 Zahub zástup kopidlníků, sebrání mocných vůdců i lidu bujného, pyšně vykračující s kusy stříbra; rozptyl lidi žádostivé válek.
Dzudzulani chirombo pakati pa mabango, gulu la ngʼombe zazimuna pakati pa ana angʼombe a mitundu ya anthu. Mochititsidwa manyazi, abweretse mitanda ya siliva. Balalitsani anthu a mitundu ina amene amasangalatsidwa ndi nkhondo.
31 Přijdouť nejvzácnější z Egypta, Mouřenínská země rychle vztáhne ruku svou k Bohu.
Nthumwi zidzachokera ku Igupto; Kusi adzadzipereka yekha kwa Mulungu.
32 Království země zpívejte Bohu, žalmy zpívejte Pánu, (Sélah)
Imbirani Mulungu Inu mafumu a dziko lapansi imbirani Ambuye matamando. (Sela)
33 Tomu, kterýž se vznáší nad nebem nebes starodávních; aj, vydává hlas svůj, hlas přemocný.
Kwa Iye amene amakwera pa mitambo yakalekale ya mmwamba amene amabangula ndi mawu amphamvu.
34 Dejte čest síly Bohu, jehož důstojnost nad Izraelem, a velikomocnost jeho na oblacích.
Lengezani za mphamvu za Mulungu, amene ulemerero wake uli pa Israeli amene mphamvu zake zili mʼmitambo.
35 Přehrozný jsi, ó Bože, z svatých příbytků svých. Bůh silný Izraelský, onť dává moc a sílu lidu svému, Bůh požehnaný.
Ndinu woopsa, Inu Mulungu mʼmalo anu opatulika; Mulungu wa Israeli amapereka mphamvu ndi nyonga kwa anthu ake. Matamando akhale kwa Mulungu!

< Žalmy 68 >