< Žalmy 64 >
1 Přednímu z kantorů, žalm Davidův. Slyš, ó Bože, hlas můj, když naříkám, před hrůzou nepřítele ostříhej života mého.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Ndimvereni Mulungu pomwe ndikunena madandawulo anga; tetezani moyo wanga ku chiopsezo cha mdani.
2 Skrej mne před úklady zlostníků, před zbouřením těch, kteříž páší nepravost,
Ndibiseni ku chiwembu cha anthu oyipa, ku gulu laphokoso la anthu ochita zoyipa.
3 Kteříž naostřili jako meč jazyk svůj, naměřili střelu svou, řeč přehořkou.
Iwo amanola malilime awo ngati malupanga, amaponya mawu awo olasa ngati mivi.
4 Aby stříleli z skrýší na upřímého; nenadále naň vystřelují, aniž se koho bojí.
Iwo amaponya mivi yawo ali pa malo wobisala kwa munthu wosalakwa; amamulasa modzidzimutsa ndi mopanda mantha.
5 Zatvrzují se ve zlém, smlouvají se, jak by poléci mohli osídla, a říkají: Kdo je spatří?
Iwo amalimbikitsana wina ndi mnzake pa chikonzero chawo choyipa, amayankhula zobisa misampha yawo; ndipo amati, “Adzayiona ndani?”
6 Vyhledávají snažně nešlechetnosti, hyneme od ran přelstivých; takť vnitřnost a srdce člověka hluboké jest.
Iwo amakonzekera zosalungama ndipo amati, “Takonza ndondomeko yabwino kwambiri!” Ndithu maganizo ndi mtima wa munthu ndi zachinyengo.
7 Ale jakž Bůh vystřelí na ně prudkou střelu, poraženi budou.
Koma Mulungu adzawalasa ndi mivi; mwadzidzidzi adzakanthidwa.
8 A ku pádu je přivede vlastní jazyk jejich; vzdálí se jich každý, kdož by je viděl.
Iye adzatembenuza milomo yawoyo kuwatsutsa ndi kuwasandutsa bwinja; onse amene adzawaona adzagwedeza mitu yawo mowanyoza.
9 I budou se báti všickni lidé, a ohlašovati skutek Boží, a k srozumívání dílu jeho příčinu dadí.
Anthu onse adzachita mantha; adzalengeza ntchito za Mulungu ndi kulingalira mozama zomwe Iye wazichita.
10 Spravedlivý pak veseliti se bude v Hospodinu, a v něm doufati, anobrž chlubiti se budou všickni, kteříž jsou upřímého srdce.
Lolani wolungama akondwere mwa Yehova ndi kubisala mwa Iye, owongoka mtima onse atamande Iye!