< Žalmy 15 >
1 Žalm Davidův. Hospodine, kdo bude přebývati v stánku tvém? Kdo bydliti bude na hoře svaté tvé?
Salimo la Davide. Yehova, ndani angathe kukhala mʼmalo anu opatulika? Kodi ndani angathe kukhala mʼphiri lanu loyera?
2 Ten, kdož chodí v upřímnosti, a činí spravedlnost, a mluví pravdu z srdce svého.
Munthu wa makhalidwe abwino, amene amachita zolungama, woyankhula choonadi chochokera mu mtima mwake,
3 Kdož neutrhá jazykem svým, bližnímu svému nečiní zlého, a potupy neuvodí na bližního svého.
ndipo mʼkamwa mwake simutuluka mawu osinjirira, amene sachitira choyipa mnansi wake kapena kufalitsa mbiri yoyipa ya munthu mnzake,
4 Ten, před jehož očima v nevážnosti jest zavržený, v poctivosti pak bojící se Hospodina; a přisáhl-li by i se škodou, však toho nemění.
amene sapereka ulemu kwa munthu woyipa. Koma amalemekeza amene amaopa Yehova, amene amakwaniritsa zomwe walonjeza ngakhale pamene zikumupweteka,
5 Kdož peněz svých nedává na lichvu, a daru proti nevinnému nebéře. Kdož tyto věci činí, nepohneť se na věky.
amene amakongoletsa ndalama zake popanda chiwongoladzanja ndipo salandira chiphuphu pofuna kutsutsa anthu osalakwa. Iye amene amachita zinthu zimenezi sadzagwedezeka konse.