< Žalmy 145 >
1 Chvalitebná píseň Davidova. Vyvyšovati tě budu, Bože můj králi, a dobrořečiti jménu tvému na věky věků.
Salimo la matamando la Davide. Ndidzakukwezani Mulungu wanga, Mfumu yanga; ndidzatamanda dzina lanu ku nthawi za nthawi.
2 Na každý den dobrořečiti budu tobě, a chváliti jméno tvé na věky věků.
Ndidzakutamandani tsiku ndi tsiku ndi kulemekeza dzina lanu ku nthawi za nthawi.
3 Hospodin veliký jest, a vší chvály hodný, a velikost jeho nemůž vystižena býti.
Yehova ndi wamkulu ndi woyenera matamando onse; ukulu wake palibe angawumvetsetse.
4 Rodina rodině vychvalovati bude skutky tvé, a předivnou moc tvou zvěstovati.
Mʼbado wina udzayamikira ntchito yanu kwa mʼbado wina; Iwo adzafotokoza za machitidwe anu amphamvu.
5 O slávě a kráse velebnosti tvé, i o věcech tvých předivných mluviti budu.
Adzayankhula ulemerero wokongola waufumu wanu, ndipo ine ndidzalingalira za ntchito zanu zodabwitsa.
6 A moc přehrozných skutků tvých rozhlašovati budou; i já důstojnost tvou budu vypravovati.
Iwo adzafotokoza za mphamvu ya ntchito zanu zoopsa kwambiri, ndipo ine ndidzalengeza za ntchito zanu zazikulu.
7 Pamět mnohé dobroty tvé hlásati budou, a o spravedlnosti tvé zpívati, řkouce:
Adzakondwerera kuchuluka kwa ubwino wanu, ndi kuyimba mwachimwemwe za chilungamo chanu.
8 Milostivý a lítostivý jest Hospodin, dlouhoshovívající a velikého milosrdenství.
Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo, wosakwiya msanga ndi wodzaza ndi chikondi chosasinthika.
9 Dobrotivý Hospodin všechněm, a slitování jeho nade všecky skutky jeho.
Yehova ndi wabwino kwa onse; amachitira chifundo zonse zimene anazipanga.
10 Oslavujtež tebe, Hospodine, všickni skutkové tvoji, a svatí tvoji tobě dobrořečte.
Zonse zimene munazipanga zidzakutamandani, Inu Yehova; oyera mtima adzakulemekezani.
11 Slávu království tvého ať vypravují, a o síle tvé mluví,
Iwo adzafotokoza za ulemerero wa ufumu wanu ndi kuyankhula za mphamvu yanu,
12 Aby v známost uvedli synům lidským moci jeho, a slávu i ozdobu království jeho.
kuti anthu onse adziwe za machitidwe anu amphamvu ndi ulemerero wokongola wa ufumu wanu.
13 Království tvé jest království všech věků, a panování tvé nad jedním každým pokolením.
Ufumu wanu ndi ufumu wamuyaya, ndipo ulamuliro wanu ndi wosatha pa mibado yonse. Yehova ndi wokhulupirika pa malonjezo ake onse ndi wokonda zonse zimene Iye anazipanga.
14 Zdržujeť Hospodin všecky padající, a pozdvihuje všechněch sklíčených.
Yehova amagwiriziza onse amene akugwa ndipo amakweza onse otsitsidwa.
15 Oči všechněch v tebe doufají, a ty dáváš jim pokrm jejich v čas příhodný.
Maso a onse amayangʼana kwa Inu, ndipo Inu mumawapatsa chakudya chawo pa nthawi yoyenera.
16 Otvíráš ruku svou, a nasycuješ každý živočich podlé dobře líbezné vůle své.
Mumatsekula dzanja lanu ndi kukwaniritsa zokhumba za chamoyo chilichonse.
17 Spravedlivý jest Hospodin ve všech cestách svých, a milosrdný ve všech skutcích svých.
Yehova ndi wolungama mʼnjira zake zonse, ndi wokonda zonse zimene anazipanga.
18 Blízký jest Hospodin všechněm, kteříž ho vzývají, všechněm, kteříž ho vzývají v pravdě.
Yehova ali pafupi ndi onse amene amamuyitana, onse amene amamuyitana Iye mʼchoonadi.
19 Vůli těch, kteříž se ho bojí, činí, a křik jejich slyší, a spomáhá jim.
Iye amakwaniritsa zokhumba za iwo amene amamuopa; amamva kulira kwawo ndi kuwapulumutsa.
20 Ostříhá Hospodin všech, kdož jej milují, ale všecky bezbožné zatratí.
Yehova amayangʼana onse amene amamukonda koma adzawononga anthu onse oyipa.
21 Chválu Hospodinovu vypravovati budou ústa má, a dobrořečiti bude všeliké tělo jménu svatému jeho od věků až na věky.
Pakamwa panga padzayankhula zotamanda Yehova. Cholengedwa chilichonse chitamande dzina lake loyera ku nthawi za nthawi.