< Žalmy 13 >

1 Přednímu zpěváku, žalm Davidův. Až dokud, Hospodine? Což se na věky zapomeneš na mne? Dokudž tvář svou skrývati budeš přede mnou?
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Mpaka liti Yehova? Kodi mudzandiyiwala mpaka kalekale? Mpaka liti mudzandibisira nkhope yanu?
2 Dokud rady vyhledávati budu v mysli své, a den ode dne svírati se v srdci svém? Až dokud se zpínati bude nepřítel můj nade mnou?
Ndidzalimbana ndi maganizo anga ndi kukhala ndi chisoni mu mtima mwanga tsiku lililonse mpaka liti? Mpaka liti adani anga adzandipambana?
3 Vzhlédni, vyslyš mne, Hospodine Bože můj, osvěť oči mé, abych neusnul snem smrti,
Ndiyangʼaneni ndi kundiyankha, Inu Yehova Mulungu wanga. Walitsani maso anga kuti ndingafe;
4 A aby neřekl nepřítel můj: Svítězil jsem nad ním, a nepřátelé moji aby neplésali, jestliže bych se poklesl.
mdani wanga adzati, “Ndamugonjetsa,” ndipo adani anga adzakondwera pamene ine ndagwa.
5 Jáť zajisté v milosrdenství tvém doufám, plésati bude srdce mé v spasení tvém;
Koma ndikudalira chikondi chanu chosasinthika; mtima wanga umakondwera ndi chipulumutso chanu.
6 zpívati budu Hospodinu, že jest mi tak dobře učinil.
Ine ndidzayimbira Yehova pakuti wandichitira zokoma.

< Žalmy 13 >