< Príslovia 15 >

1 Odpověd měkká odvracuje hněv, ale řeč zpurná vzbuzuje prchlivost.
Kuyankha kofatsa kumathetsa mkwiyo, koma mawu ozaza amautsa ukali.
2 Jazyk moudrých ozdobuje umění, ale ústa bláznů vylévají bláznovství.
Munthu wanzeru amayankhula zinthu za nzeru, koma pakamwa pa zitsiru pamatulutsa za uchitsiru.
3 Na všelikém místě oči Hospodinovy spatřují zlé i dobré.
Maso a Yehova ali ponseponse, amayangʼana pa oyipa ndi abwino omwe.
4 Zdravý jazyk jest strom života, převrácenost pak z něho ztroskotání od větru.
Kuyankhula kodekha kuli ngati mtengo wopatsa moyo, koma kuyankhula kopotoka kumapweteka mtima.
5 Blázen pohrdá cvičením otce svého, ale kdož ostříhá naučení, opatrnosti nabude.
Chitsiru chimanyoza mwambo wa abambo ake, koma wochenjera amasamala chidzudzulo.
6 V domě spravedlivého jest hojnost veliká, ale v úrodě bezbožného zmatek.
Munthu wolungama amakhala ndi chuma chambiri, zimene woyipa amapindula nazo zimamugwetsa mʼmavuto.
7 Rtové moudrých rozsívají umění, srdce pak bláznů ne tak.
Pakamwa pa anthu anzeru pamafalitsa nzeru; koma mitima ya zitsiru sitero.
8 Obět bezbožných ohavností jest Hospodinu, ale modlitba upřímých líbí se jemu.
Nsembe za anthu oyipa zimamunyansa Yehova, koma amakondwera ndi pemphero la anthu owona mtima.
9 Ohavností jest Hospodinu cesta bezbožného, toho pak, kdož následuje spravedlnosti, miluje.
Ntchito za anthu oyipa zimamunyansa Yehova koma amakonda amene amafunafuna chilungamo.
10 Trestání přísné opouštějícímu cestu, a kdož nenávidí domlouvání, umře.
Amene amasiya njira yabwino adzalangidwa koopsa. Odana ndi chidzudzulo adzafa.
11 Peklo i zatracení jest před Hospodinem, čím více srdce synů lidských? (Sheol h7585)
Manda ndi chiwonongeko ndi zosabisika pamaso pa Yehova, nanji mitima ya anthu! (Sheol h7585)
12 Nemiluje posměvač toho, kterýž ho tresce, aniž k moudrým přistoupí.
Wonyoza sakonda kudzudzulidwa; iye sapita kwa anthu anzeru.
13 Srdce veselé obveseluje tvář, ale pro žalost srdce duch zkormoucen bývá.
Mtima wokondwa umachititsa nkhope kukhala yachimwemwe, koma mtima wosweka umawawitsa moyo.
14 Srdce rozumného hledá umění, ale ústa bláznů pasou se bláznovstvím.
Mtima wa munthu wozindikira zinthu umafunafuna nzeru, koma pakamwa pa zitsiru pamadya uchitsiru wawo.
15 Všickni dnové chudého zlí jsou, ale dobromyslného hody ustavičné.
Munthu woponderezedwa masiku ake onse amakhala oyipa, koma mtima wachimwemwe umakhala pa chisangalalo nthawi zonse.
16 Lepší jest maličko s bázní Hospodinovou než poklad veliký s nepokojem.
Kuli bwino kukhala ndi zinthu pangʼono nʼkumaopa Yehova, kusiyana ndi kukhala ndi chuma chambiri uli pamavuto.
17 Lepší jest krmě z zelí, kdež jest láska, nežli z krmného vola, kdež jest nenávist.
Kuli bwino kudyera ndiwo zamasamba pamene pali chikondi, kusiyana ndi kudyera nyama yangʼombe yonenepa pamene pali udani.
18 Muž hněvivý vzbuzuje sváry, ale zpozdilý k hněvu upokojuje svadu.
Munthu wopsa mtima msanga amayambitsa mikangano, koma munthu woleza mtima amathetsa ndewu.
19 Cesta lenivého jest jako plot z trní, ale stezka upřímých jest vydlážená.
Njira ya munthu waulesi ndi yowirira ndi mtengo waminga, koma njira ya munthu wolungama ili ngati msewu waukulu.
20 Syn moudrý obveseluje otce, bláznivý pak člověk pohrdá matkou svou.
Mwana wanzeru amakondweretsa abambo ake, koma mwana wopusa amanyoza amayi ake.
21 Bláznovství jest veselím bláznu, ale člověk rozumný upřímo kráčeti směřuje.
Uchitsiru umakondweretsa munthu wopanda nzeru, koma munthu womvetsa zinthu amayenda mowongoka.
22 Kdež není rady, zmařena bývají usilování, ale množství rádců ostojí.
Popanda uphungu zolinga zako munthu zimalephereka, koma pakakhala aphungu ambiri zolinga zimatheka.
23 Vesel bývá člověk z odpovědi úst svých; nebo slovo v čas příhodný ó jak jest dobré!
Munthu amakondwera ndi kuyankha koyenera, ndipo mawu onena pa nthawi yake ndi okoma.
24 Cesta života vysoko jest rozumnému proto, aby se uchýlil od pekla dole. (Sheol h7585)
Munthu wanzeru amatsata njira yopita ku moyo kuti apewe malo okhala anthu akufa. (Sheol h7585)
25 Dům pyšných vyvrací Hospodin, meze pak vdovy upevňuje.
Yehova amapasula nyumba ya munthu wonyada koma amasamalira malo a mkazi wamasiye.
26 Ohavností jsou Hospodinu myšlení zlého, ale čistých řeči vzácné.
Maganizo a anthu oyipa amamunyansa Yehova, koma mawu a anthu oyera mtima amamusangalatsa.
27 Kdož dychtí po lakomství, kormoutí dům svůj; ale kdož nenávidí darů, živ bude.
Munthu wofuna phindu mwachinyengo amavutitsa banja lake, koma wodana ndi ziphuphu adzakhala ndi moyo.
28 Srdce spravedlivého přemyšluje, co má mluviti, ale ústa bezbožných vylévají všelijakou zlost.
Munthu wolungama amaganizira za mmene ayankhire, koma pakamwa pa munthu woyipa pamatulutsa mawu oyipa.
29 Vzdálen jest Hospodin od bezbožných, ale modlitbu spravedlivých vyslýchá.
Yehova amakhala kutali ndi anthu oyipa, koma amamva pemphero la anthu olungama.
30 To, což se zraku naskýtá, obveseluje srdce; pověst dobrá tukem naplňuje kosti.
Kuwala kwa maso kumasangalatsa mtima ndipo uthenga wabwino umalimbitsa munthu.
31 Ucho, kteréž poslouchá trestání života, u prostřed moudrých bydliti bude.
Womvera mawu a chidzudzulo amene apatsa moyo adzakhala pakati pa anthu anzeru.
32 Kdo se vyhýbá cvičení, zanedbává duše své; ale kdož přijímá domlouvání, má rozum.
Amene amanyoza mwambo amadzinyoza yekha, koma womvera mawu a chidzudzulo amapeza nzeru zomvetsa zinthu.
33 Bázeň Hospodinova jest cvičení se moudrosti, a slávu předchází ponížení.
Kuopa Yehova kumaphunzitsa munthu nzeru, ndipo kudzichepetsa ndi ulemu chili patsogolo ndi kudzichepetsa.

< Príslovia 15 >