< Nehemiáš 11 >

1 I přebývala knížata lidu v Jeruzalémě. Jiný pak lid metali losy, aby vzali desátého člověka k bydlení v Jeruzalémě městě svatém, ale devět dílů v jiných městech,
Nthawi imeneyo atsogoleri a anthu ankakhala ku Yerusalemu. Tsono anthu ena onse anachita maere kuti apeze munthu mmodzi pa anthu khumi aliwonse kuti azikhala ku Yerusalemu, mzinda wopatulika. Anthu asanu ndi anayi otsalawo ankakhala mʼmidzi yawo.
2 Ačkoli dobrořečil lid všechněm mužům těm, kteříž se sami dobrovolně podali k bydlení v Jeruzalémě.
Anthu anayamikira onse amene anadzipereka kuti azikhala mu Yerusalemu.
3 A tito jsou přednější té krajiny, kteříž se osadili v Jeruzalémě. (V jiných pak městech Judských bydlili jeden každý v vládařství svém, po městech svých, lid Izraelský, kněží a Levítové, i Netinejští, též i synové služebníků Šalomounových.)
Aisraeli wamba, ansembe, Alevi, ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu ndiponso zidzukulu za antchito a Solomoni ankakhala mʼmidzi yawo, aliyense mu dera lake. Koma atsogoleri a chigawo cha Yuda anali atakhazikika mu Yerusalemu.
4 A tak v Jeruzalémě bydlili někteří z synů Judových i z synů Beniaminových. Z Judových: Ataiáš syn Uziáše, syna Zachariášova, syna Amariášova, syna Sefatiášova, syna Mahalaleelova z synů Fáresových.
Ku Yerusalemu kunkakhalanso anthu ena a mafuko a Yuda ndi Benjamini. Ena mwa zidzukulu za Yuda ndi awa: Ataya, mwana wa Uziya, mwana wa Zekariya, mwana wa Amariya mwana wa Sefatiya, mwana wa Mahalaleli. Onsewa anali ana a Perezi.
5 Též Maaseiáš syn Bárucha, syna Kolchozy, syna Chazaiášova, syna Adaiášova, syna Joiaribova, syna Zachariášova, syna Silonského.
Ena ndi awa: Maaseya mwana wa Baruki, mwana wa Koli-Hoze mwana wa Hazaya, mwana wa Adaya, mwana wa Yowaribu, Zekariya mwana wa Msiloni.
6 Všech synů Fáresových, bydlících v Jeruzalémě, čtyři sta šedesáte osm, mužů udatných.
Zidzukulu zonse za Perezi, anthu amphamvu zawo amene ankakhala ku Yerusalemu analipo anthu okwanira 468.
7 Synové Beniaminovi tito: Sallu syn Mesullama, syna Joedova, syna Pedaiášova, syna Kolaiášova, syna Maaseiášova, syna Itielova, syna Izaiášova.
Nazi zidzukulu za Benjamini: Salu mwana wa Mesulamu, mwana wa Yowedi, mwana wa Pedaya, mwana wa Kolaya, mwana wa Maaseiya, mwana wa Itieli, mwana wa Yesaiya.
8 A po něm Gabai, Sallai. Všech devět set dvadceti osm.
Abale ake anali Gabayi ndi Salaya. Onse pamodzi anali 928.
9 Joel pak syn Zichri byl jim představen, a Juda syn Senua nad městem druhý po něm.
Yoweli mwana wa Zikiri ndiye anali mtsogoleri wawo, ndipo Yuda mwana wa Hasenuya ndiye amayangʼanira chigawo cha chiwiri cha mzinda.
10 Z kněží: Jedaiáš syn Joiaribův a Jachin.
Ansembe anali awa: Yedaya mwana wa Yowaribu; Yakini;
11 Saraiáš syn Helkiáše, syna Mesullamova, syna Sádochova, syna Meraiotova, syna Achitobova, přední v domě Božím.
Seraya mwana wa Hilikiya mwana wa Mesulamu, mwana wa Zadoki, mwana wa Merayoti, mwana wa Ahitubi amene anali woyangʼanira Nyumba ya Mulungu,
12 Bratří pak jejich, přisluhujících v tom domě, osm set dvadceti dva. A Adaiáš syn Jerochama, syna Pelaliášova, syna Amzi, syna Zachariášova, syna Paschurova, syna Malkiášova,
ndi abale awo, amene ankagwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu. Onse pamodzi anali 822. Panalinso Adaya mwana wa Yerohamu, mwana wa Pelaliya, mwana wa Amizi, mwana wa Zekariya, mwana wa Pasi-Huri, mwana wa Malikiya,
13 A bratří jeho, knížat čeledí otcovských, dvě stě čtyřidceti dva. A Amassai syn Azarele, syna Achzai, syna Mesillemotova, syna Immerova.
ndi abale ake, amene anali atsogoleri a mabanja. Onse pamodzi anali 242. Kuphatikiza apo panalinso Amasisai mwana wa Azaireli, mwana wa Ahazayi, mwana wa Mesilemoti, mwana wa Imeri
14 Bratří pak jejich, mužů udatných, sto dvadceti osm, jimž představen byl Zabdiel syn Gedolimův.
ndi abale ake. Onse pamodzi anali 128 ndipo anali anthu olimba mtima kwambiri. Mtsogoleri wawo wamkulu anali Zabidieli mwana wa Hagedolimu.
15 Z Levítů tito: Semaiáš syn Chasuby, syna Azrikamova, syna Chasabiášova, syna Bunni.
Alevi anali awa: Semaya mwana wa Hasubu, mwana wa Azirikamu, mwana wa Hasabiya, mwana wa Buni.
16 A Sabbetai s Jozabadem byli nad dílem při domě Božím vně, z předních Levítů.
Sabetayi ndi Yozabadi anali atsogoleri amene ankayangʼanira ntchito ya kunja kwa Nyumba ya Mulungu.
17 A Mataniáš syn Míchy, syna Zabdi, syna Azafova, přední, začínal chvály a modlitbu. A Bakbukiáš druhý z bratří jeho, a Abda syn Sammua, syna Galalova, syna Jedutunova.
Mataniya mwana wa Mika, mwana wa Zabidi, mwana wa Asafu ndiye anali wotsogolera pa mapemphero achiyamiko. Panalinso Bakibukiya amene anali wachiwiri pakati pa abale ake. Kuwonjezera apo panalinso Abida mwana wa Samuwa, mwana wa Galali, mwana wa Yedutuni.
18 Všech Levítů v městě svatém dvě stě osmdesát a čtyři.
Alevi onse amene anali mu mzinda woyera analipo 284.
19 Z vrátných: Akkub, Talmon a bratří jejich, strážní u bran, sto sedmdesát a dva.
Alonda a ku Nyumba ya Mulungu anali awa: Akubu, Talimoni ndi abale awo. Onse pamodzi anali 172.
20 Ostatek pak lidu Izraelského, kněží a Levítů, bydlili ve všech městech Judských, jeden každý v dědictví svém.
Aisraeli ena onse pamodzi ndi ansembe ndi Alevi ankakhala mʼmizinda ya Yuda, ndipo aliyense ankakhala mʼdera la makolo ake.
21 Ale Netinejští bydlili v Ofel, Zicha pak a Gispa byli představeni Netinejským.
Koma antchito a ku Nyumba ya Mulungu ankakhala pa phiri la Ofeli, ndipo Ziha ndi Gisipa ndiwo anali kuwayangʼanira.
22 Představený pak Levítům v Jeruzalémě byl Uzi syn Báni, syna Chasabiášova, syna Mataniášova, syna Míchova z synů Azafových, jenž byli zpěváci při službě domu Božího.
Wamkulu wa Alevi mu Yerusalemu anali Uzi mwana wa Bani, mwana wa Hasabiya, mwana wa Mataniya, mwana wa Mika. Uzi anali mmodzi wa zidzukulu za Asafu, amene anali oyimba nyimbo pa nthawi zachipembedzo mʼNyumba ya Mulungu.
23 Nebo poručení královské bylo o nich, a stálé odměření pro zpěváky na každý den.
Pakuti mfumu inalamula kuti tsiku ndi tsiku pa nthawi zachipembedzo oyimba nyimbowo azikhalapo.
24 A Petachiáš syn Mesezabelův, z synů Záry syna Judova, místo královské držící v každém jednání k lidu.
Petahiya mwana wa Mesezabeli, mmodzi mwa zidzukulu za Zera mwana wa Yuda ndiye ankayimirira Aisraeli pa bwalo la mfumu ya Perisiya.
25 Ve vsech pak s poli jejich, z synů Judových bydlili v Kariatarbe a v vesnicích jeho, v Dibon a vesnicích jeho, v Jekabsael i ve vsech jeho,
Anthu ena a fuko la Yuda ankakhala ku Kiriyati-Ariba ndi midzi yake, ku Diboni ndi midzi yake, ku Yekabizeeli ndi midzi yake,
26 A v Jesua, v Molada, v Betfelet,
ku Yesuwa, Molada, Beti-Peleti,
27 A v Azarsual, v Bersabé i v vesnicích jeho.
Hazari-Suwali, Beeriseba ndi midzi yawo.
28 A v Sicelechu, v Mechona, i v vesnicích jeho,
Ku Zikilagi, Mekona ndi midzi yawo,
29 V Enremmon, v Zaraha, v Jarmut,
ku Eni-Rimoni, Zora, Yarimuti,
30 V Zanoe, v Adulam i ve vsech jeho, v Lachis s poli jeho, v Azeka a vesnicích jeho. A tak bydlili od Bersabé až do Gehinnom.
Zanowa, Adulamu ndi midzi yake, ku Lakisi ndi minda yake, ku Beeriseba mpaka ku chigwa cha Hinomu.
31 Synové pak Beniaminovi z Gabaa v Michmas, v Aia, v Bethel i v vesnicích jeho,
Nazonso zidzukulu za Benjamini zinkakhala mʼdera lawo kuyambira ku Geba mpaka ku Mikimasi, Ayiya, Beteli ndi midzi yake,
32 V Anatot, v Nobe, v Anania,
ku Anatoti, Nobu ndi Ananiya,
33 V Azor, v Ráma, v Gittaim,
ku Hazori, Rama ndi Gitaimu,
34 V Chadid, v Seboim, v Neballat,
ku Hadidi, Zeboimu ndi Nebalati,
35 V Lod, v Ono a v údolí řemeslníků.
ku Lodi, Ono ndi ku chigwa cha Amisiri.
36 Z Levítů pak někteří bydlili v dílích Judských a Beniaminských.
Magulu ena a Alevi a ku Yuda ankakhala ku Benjamini.

< Nehemiáš 11 >