< Jób 41 >

1 Vytáhneš-liž velryba udicí, aneb provazem pohříženým až k jazyku jeho?
“Kodi ungathe kukoka ngʼona ndi mbedza ya nsomba kapena kukanikiza lilime lake pansi ndi chingwe?
2 Zdali dáš kroužek na chřípě jeho, aneb hákem probodneš čelist jeho?
Kodi ungathe kumanga chingwe mʼmphuno mwake, kapena kubowola nsagwada zake ndi mbedza?
3 Zdaž se obrátí k tobě s prosbami, aneb mluviti bude tobě lahodně?
Kodi ngʼonayo idzakupempha kuti uyichitire chifundo? Kodi idzakuyankhula ndi mawu ofatsa?
4 Učiní-liž smlouvu s tebou? Přijmeš-liž jej za služebníka věčného?
Kodi idzachita nawe mgwirizano kuti uyisandutse kapolo wako mpaka muyaya?
5 Zdaž budeš s ním hráti jako s ptáčkem, aneb přivážeš jej dětem svým?
Kodi udzasewera nayo ngati mbalame, kapena kuyimangirira kuti atsikana ako asewere nayo?
6 Přistrojí-liž sobě hody z něho společníci, a rozdělí-liž jej mezi kupce?
Kodi anthu adzayitsatsa malonda? Nanga amalondawo nʼkugawanagawana nyama yake kuti akagulitse?
7 Zdaž naplníš háky kůži jeho, a vidlicemi rybářskými hlavu jeho?
Kodi chikopa chake ungathe kuchilasa ndi zisonga, kapena kubowola mutu wake ndi nthungo zophera nsomba?
8 Vztáhni jen na něj ruku svou, a neučiníš zmínky o boji.
Ukayiputa udziwe kuti pali nkhondo, ndipo iweyo sudzabwereranso.
9 Aj, naděje o polapení jeho mylná jest. Zdaž i k spatření jeho člověk nebývá poražen?
Chiyembekezo choti nʼkuyigonjetsa ndi chabodza; kungoyiona kokha, ndithu iwe kumangodzigwera wekha.
10 Není žádného tak smělého, kdo by jej zbudil, kdož tedy postaví se přede mnou?
Palibe wolimba mtima kuti ndi kuyiputa. Ndani angalimbe mtima kulimbana ndi Ine?
11 Kdo mne čím předšel, abych se jemu odplacel? Cožkoli jest pode vším nebem, mé jest.
Kodi ndani anandipatsa kanthu kuti ndimubwezere? Zonse za pansi pa thambo ndi zanga.
12 Nebudu mlčeti o údech jeho, a o síle výborného sformování jeho.
“Sindidzaleka kuyankhula za ziwalo zake za chirombocho, za mphamvu zake ndiponso za maonekedwe a thupi lake.
13 Kdo odkryl svrchek oděvu jeho? S dvojitými udidly svými kdo k němu přistoupí?
Ndani angasende chikopa chake? Ndani angayiyandikire kuti abowole chikopa chake cholimbacho?
14 Vrata úst jeho kdo otevře? Okolo zubů jeho jest hrůza.
Ndani angatsekule kukamwa kwake, pakamwa pamene pazunguliridwa ndi mano ochititsa mantha?
15 Šupiny jeho pevné jako štítové sevřené velmi tuze.
Kumsana kwake kuli mizere ya mamba onga zishango zolumikizanalumikizana;
16 Jedna druhé tak blízko jest, že ani vítr nevchází mezi ně.
Mambawo ndi olukanalukana kotero kuti mpweya sungathe kulowa pakati pake.
17 Jedna druhé se přídrží, a nedělí se.
Ndi olumikizanalumikizana; ndi omatirirana kwambiri kotero kuti sangathe kulekana.
18 Od kýchání jeho zažžehá se světlo, a oči jeho jsou jako záře svitání.
Kuyetsemula kwake kumatulutsa mbaliwali; maso ake amawala ngati kuwala kwa mʼbandakucha.
19 Z úst jeho jako pochodně vycházejí, a jiskry ohnivé vyskakují.
Mʼkamwa mwake mumatuluka nsakali zamoto ndipo mumathetheka mbaliwali zamoto.
20 Z chřípí jeho vychází dým, jako z kotla vroucího aneb hrnce.
Mʼmphuno mwake mumatuluka utsi ngati wa mʼnkhali yowira yomwe ili pa moto wa bango.
21 Dýchání jeho uhlí rozpaluje, a plamen z úst jeho vychází.
Mpweya wake umayatsa makala, ndipo malawi amoto amatuluka mʼkamwa mwake.
22 V šíji jeho přebývá síla, a před ním utíká žalost.
Mphamvu zake zili mʼkhosi mwake; aliyense wokumana nayo amangoti njenjenje ndi mantha.
23 Kusové masa jeho drží se spolu; celistvé jest v něm, aniž se rozdrobuje.
Minyewa ya thupi lake ndi yolumikizana ndipo ndi yokhwima kwambiri ndi yolimba.
24 Srdce jeho tuhé jest jako kámen, tak tuhé, jako úlomek zpodního žernovu.
Pachifuwa pake ndi powuma ngati mwala, ndi pa gwaa, ngati mwala wamphero.
25 Vyskýtání jeho bojí se nejsilnější, až se strachem i vyčišťují.
Ngʼonayo ikangovuwuka, ndi anthu amphamvu omwe amaopa; amabwerera mʼmbuyo, kuthawa.
26 Meč stihající jej neostojí, ani kopí, šíp neb i pancíř.
Ngakhale ikanthidwe ndi lupanga, lupangalo silichita kanthu, ngakhale mkondo, muvi ndi nthungo, zonse zimalephera.
27 Pokládá železo za plevy, ocel za dřevo shnilé.
Chitsulo imachiyesa ngati phesi chabe ndi mkuwa ngati chikuni chowola.
28 Nezahání ho střela, v stéblo obrací se jemu kamení prakové.
Muvi sungathe kuyithawitsa, miyala imene ayilasa nayo imangoyinyenyanyenya.
29 Za stéblo počítá střelbu, a posmívá se šermování kopím.
Zibonga zimakhala ngati ziputu; imangoseka pamene akuyibaya ndi nthungo.
30 Pod ním ostré střepiny, stele sobě na věci špičaté jako na blátě.
Mamba a ku mimba kwake ali ngati chopunthira chakunthwa ndipo imasiya mkukuluzi mʼmatope ngati galeta lopunthira tirigu.
31 Působí, aby vřelo v hlubině jako v kotle, a kormoutilo se moře jako v moždíři.
Imagadutsa madzi ozama ngati madzi a mʼnkhali, imachititsa nyanja kuti iwire ngati mbiya yoyengera mafuta.
32 Za sebou patrnou činí stezku, až sezdá, že propast má šediny.
Kumbuyo kwake imasiya nthubwitubwi zambee, kotero kuti munthu angaganize kuti nyanja yachita imvi.
33 Žádného není na zemi jemu podobného, aby tak učiněn byl bez strachu.
Pa dziko lapansi palibe china chofanana nacho, nʼcholengedwa chopanda mantha.
34 Cokoli vysokého jest, za nic pokládá, jest králem nade všemi šelmami.
Chimanyoza nyama zina zonse; icho chija ndi mfumu ya nyama zonse.”

< Jób 41 >