< Jób 36 >

1 Zatím přidal Elihu, a řekl:
Ndipo Elihu anapitirira kuyankhula nati:
2 Postrp mne maličko, a oznámímť šíře; neboť mám ještě, co bych za Boha mluvil.
“Mundilole pangʼono pokha ndipo ndikuonetsani kuti zilipo zambiri zoti ziyankhulidwe mʼmalo mwa Mulungu.
3 Vynesu smysl svůj zdaleka, a stvořiteli svému přivlastním spravedlnost.
Nzeru zanga ndimazitenga kutali; ndidzaonetsa kulungama kwa Mlengi wanga.
4 V pravdě, žeť ne budou lživé řeči mé; zdravě smýšlejícího máš mne s sebou.
Ndithudi mawu anga si abodza; wanzeru zangwiro ali ndi inu.
5 Aj, Bůh silný mocný jest, aniž svých zamítá; silný jest, a srdce udatného.
“Mulungu ndi wamphamvu, koma sanyoza anthu; Iye ndi wamphamvu, ndipo ndi wokhazikika pa cholinga chake.
6 Neobživuje bezbožného, chudým pak k soudu dopomáhá.
Salola oyipa kuti akhalebe ndi moyo koma amapereka ufulu kwa anthu osautsidwa.
7 Neodvrací od spravedlivého očí svých, nýbrž s králi na stolici sází je na věky, i bývají zvýšeni.
Iye saleka kuyangʼanira anthu olungama; amawayika kuti alamulire pamodzi ndi mafumu ndipo amawalemekeza mpaka muyaya.
8 Pakli by poutami sevříni byli, zapleteni jsouce provazy ssoužení:
Koma ngati anthu amangidwa ndi unyolo, ndipo akondwa ndi zingwe zamasautso,
9 Tudy jim v známost uvodí hřích jejich, a že přestoupení jejich se ssilila.
Iye amawafotokozera zomwe anachita, kuti iwo anachimwa modzikuza.
10 A tak otvírá sluch jejich, aby se napravili, anobrž mluví jim, aby se navrátili od nepravosti.
Mulungu amawatsekula makutu kuti amve malangizo ake ndipo amawalamula kuti alape zoyipa zawo.
11 Uposlechnou-li a budou-li jemu sloužiti, stráví dny své v dobrém, a léta svá v potěšení.
Ngati iwo amumvera ndi kumutumikira, adzatsiriza masiku a moyo wawo mwamtendere, adzatsiriza zaka zawo mosangalala.
12 Pakli neuposlechnou, od meče sejdou, a pozdychají bez umění.
Koma ngati samvera, adzaphedwa ndi lupanga ndipo adzafa osadziwa kanthu.
13 Nebo kteříž jsou nečistého srdce, přivětšují hněvu, aniž k němu volají, když by je ssoužil.
“Anthu osapembedza amasunga mkwiyo mu mtima mwawo; akawalanga, safuwulira kwa Iye kupempha thandizo.
14 Protož umírá v mladosti duše jejich, a život jejich s smilníky.
Amafa akanali achinyamata, pakati pa amuna achiwerewere a kumalo azipembedzo.
15 Vytrhuje, pravím, ssouženého z jeho ssoužení, a ty, jejichž sluch otvírá, v trápení.
Koma ovutika, Iye amawapulumutsa pa mavuto awo; Mulungu amawayankhula mʼmasautso awowo.
16 A tak by i tebe přenesl z prostředku úzkosti na širokost, kdež není stěsnění, a byl by pokojný stůl tvůj tukem oplývající.
“Iye akukukopani inu kuti muchoke mʼmasautso, kuti mupite ku malo aakulu kumene kulibe chokutchingani, kumalo a mpumulo kumene kuli chakudya chabwino kwambiri.
17 Ale ty zasloužils, abys jako bezbožný souzen byl; soud a právo na tě dochází.
Koma tsopano inu mwapezeka wopalamula chifukwa cha kuyipa kwanu; chiweruzo ndi chilungamo chakugwerani.
18 Jistě strach, aby tě neuvrhl Bůh u větší ránu, tak že by jakkoli veliká výplaty mzda, tebe nevyprostila.
Muchenjere kuti wina asakukopeni ndi chuma; musalole kuti chiphuphu chachikulu chikusocheretseni.
19 Zdaliž by sobě co vážil bohatství tvého? Jistě ani nejvýbornějšího zlata, ani jakékoli síly neb moci tvé.
Kodi chuma chanu kapena mphamvu zanu zonse zingakusungeni kotero kuti simungakhale pa masautso?
20 Nechvátejž tedy k noci, v kterouž odcházejí lidé na místo své.
Musalakalake kuti usiku ubwere, pakuti ndiyo nthawi imene anthu adzawonongeka.
21 Hleď, abys se neohlédal na marnost, zvoluje ji raději, nežli ssoužení.
Muchenjere kuti musatembenukire ku uchimo, chifukwa uchimowo ndiwo unabweretsa kuzunzika kwanu.
22 Aj, Bůh silný nejvyšší jest mocí svou. Kdo jemu podobný učitel?
“Taonani, Mulungu ndi wamkulu ndiponso ndi wamphamvu. Kodi ndi mphunzitsi uti amene angafanane naye?
23 Kdo jemu vyměřil cestu jeho? Kdo jemu smí říci: Činíš nepravost?
Kodi ndani amene anamuwuzapo Mulungu zoti achite, kapena kumuwuza kuti, ‘Inu mwachita chinthu cholakwa?’
24 Pamětliv buď raději, abys vyvyšoval dílo jeho, kteréž spatřují lidé,
Kumbukirani kutamanda ntchito zake zimene anthu amaziyamika mʼnyimbo.
25 Kteréž, pravím, všickni lidé vidí, na něž člověk patří zdaleka.
Anthu onse amaziona ntchitozo; anthuwo amaziona ali kutali.
26 Nebo Bůh silný tak jest veliký, že ho nemůžeme poznati, počet let jeho jest nevystižitelný.
Ndithudi, Mulungu ndi wamkulu, sitimudziwa nʼpangʼono pomwe! Chiwerengero cha zaka zake nʼchosadziwika.
27 On zajisté vyvodí krůpěje vod, kteréž vylévají déšť z oblaků jeho,
“Mulungu ndiye amakweza timadontho tamadzi kuthambo, timene timasungunuka nʼkukhala mvula;
28 Když se rozpouštějí oblakové, a kropí na mnohé lidi.
mitambo imagwetsa mvulayo ndipo mvulayo imavumbwa pa anthu mokwanira.
29 (Anobrž vyrozumí-li kdo roztažení oblaků, a zvuku stánku jeho,
Kodi ndani amene angadziwe momwe mitambo imayendera, momwe Iye amabangulira kuchokera kumalo ake?
30 Jak rozprostírá nad ním světlo své, aneb všecko moře přikrývá?
Taonani momwe amawalitsira zingʼaningʼani pa malo ake onse, zimafika ngakhale pansi pa nyanja.
31 Skrze ty věci zajisté tresce lidi, a též dává pokrmu hojnost.
Umu ndi mmene Iye amalamulira mitundu ya anthu ndi kuwapatsa chakudya chochuluka.
32 Oblaky zakrývá světlo, a přikazuje mu ukrývati se za to, co je potkává.)
Amadzaza manja ake ndi zingʼaningʼani, ndipo amazilamulira kuti zigwe pamalo pamene Iye akufuna.
33 Ohlašuje o něm zvuk jeho, též dobytek, a to hned, když pára zhůru vstupuje.
Mabingu ake amalengeza za kubwera kwa mvula yamkuntho; ngʼombe nazo zimalengeza za kubwera kwake.

< Jób 36 >