< Jób 31 >

1 Smlouvu jsem učinil s očima svýma, a proč bych hleděl na pannu?
“Ndinachita pangano ndi maso anga kuti sindidzapenya namwali momusirira.
2 Nebo jaký jest díl od Boha s hůry, aneb dědictví od Všemohoucího s výsosti?
Kodi Mulungu kumwambako wandisungira zotani? Kodi cholowa changa chochokera kwa Wamphamvuzonse kumwambako nʼchotani?
3 Zdaliž zahynutí nešlechetnému a pomsta zázračná činitelům nepravosti připravena není?
Kodi si chiwonongeko kwa anthu oyipa, tsoka kwa iwo amene amachita zolakwa?
4 Zdaliž on nevidí cest mých, a všech kroků mých nepočítá?
Kodi Mulungu saona zochita zanga, ndi kudziwa mayendedwe anga?
5 Obíral-li jsem se s neupřímostí, a chvátala-li ke lsti noha má:
“Ngati ndachita zinthu mwachiphamaso, kapena kufulumira kukachita zachinyengo,
6 Nechť mne zváží na váze spravedlnosti, a přezví Bůh upřímost mou.
Mulungu andiyeze ndi muyeso wake wolungama ndipo Iye adzadziwa kuti ine ndine wosalakwa,
7 Uchýlil-li se krok můj s cesty, a za očima mýma odešlo-li srdce mé, a rukou mých chytila-li se jaká poškvrna:
ngati mayendedwe anga asempha njira, ngati mtima wanga wakhumbira zimene maso anga aona, kapena ngati ndachita choyipa chilichonse.
8 Tedy co naseji, nechť jiný sní, a výstřelkové moji ať jsou vykořeněni.
Pamenepo ena adye zimene ndinadzala, ndipo zomera zanga zizulidwe.
9 Jestliže se dalo přivábiti srdce mé k ženě, a u dveří bližního svého činil-li jsem úklady:
“Ngati mtima wanga unakopekapo ndi mkazi, ndipo ngati ndinalakalaka mkazi wa mnansi wanga,
10 Nechť mele jinému žena má, a nad ní ať se schylují jiní.
pamenepo mkazi wanga aphikire mwamuna wina chakudya, ndipo amuna ena azigona naye.
11 Neboť jest to nešlechetnost, a nepravost odsudku hodná.
Pakuti zimenezo zikanakhala zochititsa manyazi, tchimo loyenera kulangidwa nalo.
12 Oheň ten zajisté by až do zahynutí žral, a všecku úrodu mou vykořenil.
Ndi moto umene umayaka mpaka chiwonongeko; ukanapsereza zokolola zanga.
13 Nechtěl-li jsem státi k soudu s služebníkem svým aneb děvkou svou v rozepři jejich se mnou?
“Ngati ndinkapondereza mlandu wa akapolo anga aamuna kapena aakazi, pamene ankabwera kwa ine ndi milandu yawo,
14 Nebo co bych činil, kdyby povstal Bůh silný? A kdyby vyhledával, co bych odpověděl jemu?
ndidzatani pamene Mulungu adzanditsutsa? Nanga ndidzayankha chiyani akadzandifunsa?
15 Zdali ten, kterýž mne v břiše učinil, neučinil i jeho? A ne sformoval nás hned v životě jeden a týž?
Kodi amene anapanga ine mʼmimba mwa amayi anga si yemwe anapanganso iwo? Kodi si mmodzi yemweyo amene anatipanga tonsefe mʼmimba mwa amayi athu?
16 Odepřel-li jsem žádosti nuzných, a oči vdovy jestliže jsem kormoutil?
“Ngati ndinawamana aumphawi zinthu zimene ankazikhumba, kapena kuwagwiritsa fuwa lamoto akazi amasiye amene amafuna thandizo kwa ine,
17 A jedl-li jsem skyvu svou sám, a nejedl-li i sirotek z ní?
ngati chakudya changa ndinadya ndekha, wosagawirako mwana wamasiye,
18 Poněvadž od mladosti mé rostl se mnou jako u otce, a od života matky své býval jsem vdově za vůdce.
chonsechotu kuyambira unyamata wanga ndinamulera monga abambo ake, ndipo moyo wanga wonse ndakhala ndikusamalira akazi amasiye,
19 Díval-li jsem se na koho, že by hynul, nemaje šatů, a nuzný že by neměl oděvu?
ngati ndinaona wina aliyense akuzunzika ndi usiwa, kapena munthu wosauka alibe chofunda,
20 Nedobrořečila-li mi bedra jeho, že rounem beranů mých se zahřel?
ndipo ngati iyeyo sananditamandepo chifukwa chomufunditsa ndi nsalu ya ubweya wankhosa,
21 Opřáhl-li jsem na sirotka rukou svou, když jsem v bráně viděl pomoc svou:
ngati ndinaopsezapo mwana wamasiye, poganiza kuti ndinali ndi mphamvu mʼbwalo la milandu,
22 Lopatka má od svých plecí nechť odpadne, a ruka má z kloubu svého ať se vylomí.
pamenepo phewa langa lipokonyeke, mkono wanga ukonyoke polumikizira pake.
23 Nebo jsem se bál, aby mne Bůh nesetřel, jehož bych velebnosti nikoli neznikl.
Popeza ine ndinaopa kwambiri chiwonongeko chochokera kwa Mulungu, ndinachitanso mantha ndi ulemerero wake, sindikanatha kuchita zinthu zimenezi.
24 Skládal-li jsem v zlatě naději svou, aneb hrudě zlata říkal-li jsem: Doufání mé?
“Ngati ndinayika mtima wanga pa chuma kapena kunena kwa golide wabwino kwambiri kuti, ‘Iwe ndiye chitetezo changa,’
25 Veselil-li jsem se z toho, že bylo rozmnoženo zboží mé, a že ho množství nabyla ruka má?
ngati ndinakondwera chifukwa choti chuma changa chinali chambiri, zinthu zimene manja anga anazipeza,
26 Hleděl-li jsem na světlost slunce svítícího, a na měsíc spanile chodící,
ngati pamene ndinaona dzuwa likuwala, kapena mwezi ukuyenda mwa ulemerero wake,
27 Tak že by se tajně dalo svésti srdce mé, a že by líbala ústa má ruku mou?
ndipo kuti mtima wanga unakopeka nazo nʼkuyika dzanja langa pakamwa mozilemekeza,
28 I toť by byla nepravost odsudku hodná; neboť bych tím zapíral Boha silného nejvyššího.
pamenepo zimenezinso zikanakhala machimo oti ndilangidwe nawo, chifukwa ndikanakhala wosakhulupirika kwa Mulungu wakumwamba.
29 Radoval-li jsem se z neštěstí toho, kterýž mne nenáviděl, a plésal-li jsem, když se mu zle vedlo?
“Ngati ndinasangalala ndi kuwonongeka kwa mdani wanga, kapena kusekera mavuto pamene mavuto anamugwera,
30 Nedopustilť jsem zajisté hřešiti ani ústům svým, abych zlořečení žádal duši jeho.
ine sindinachimwe ndi pakamwa panga potulutsa matemberero a mdani wanga kuti awonongeke,
31 Jestliže neříkala čeládka má: Ó by nám dal někdo masa toho; nemůžeme se ani najísti?
ngati anthu amene ndimakhala nawo mʼnyumba mwanga sananenepo kuti, ‘Kodi ndani amene sakhuta ndi chakudya cha Yobu?’
32 Nebo vně nenocoval host, dvéře své pocestnému otvíral jsem.
Komatu mlendo sindinamusiye pa msewu usiku wonse, pakuti khomo langa linali lotsekuka nthawi zonse kwa alendo,
33 Přikrýval-li jsem jako jiní lidé přestoupení svá, skrývaje v skrýši své nepravost svou?
ngati ndinabisa tchimo langa monga amachitira anthu ena, kubisa kulakwa mu mtima mwanga
34 A ač bych byl mohl škoditi množství velikému, ale pohanění rodů děsilo mne; protož jsem mlčel, nevycházeje ani ze dveří.
chifukwa choopa gulu la anthu, ndi kuchita mantha ndi mnyozo wa mafuko kotero ndinakhala chete ndipo sindinatuluke panja.
35 Ó bych měl toho, kterýž by mne vyslyšel. Ale aj, totoť jest znamení mé: Všemohoucí sám bude odpovídati za mne, a kniha, kterouž sepsal odpůrce můj.
“Aa, pakanakhala wina wondimva! Tsopano ndikutsiriza mawu anga odzitetezera. Wamphamvuzonse andiyankhe; mdani wanga achite kulemba pa kalata mawu ake ondineneza.
36 Víť Bůh, nenosil-li bych ji na rameni svém, neotočil-li bych ji sobě místo koruny.
Ndithu ine ndikanakoleka kalatayo pa phewa langa, ndikanayivala kumutu ngati chipewa chaufumu.
37 Počet kroků svých oznámil bych jemu, jako kníže přiblížil bych se k němu.
Ndikanamufotokozera zonse zimene ndinachita; ndikanafika pamaso pake ngati kalonga.
38 Jestliže proti mně země má volala, tolikéž i záhonové její plakali,
“Ngati minda yanga ikulira monditsutsa ine ndipo malo ake onse osalimidwa anyowa ndi misozi,
39 Jídal-li jsem úrody její bez peněz, a duši držitelů jejich přivodil-li jsem k vzdychání:
ngati ndinadya za mʼminda mwake osapereka ndalama kapena kukhumudwitsa anthu olima mʼmindamo,
40 Místo pšenice nechť vzejde trní, a místo ječmene koukol. Skonávají se slova Jobova.
pamenepo mʼmindamo mumere namsongole mʼmalo mwa tirigu ndi udzu mʼmalo mwa barele.” Mawu a Yobu athera pano.

< Jób 31 >