< Jób 30 >
1 Nyní pak posmívají se mi mladší mne, jejichž bych otců nechtěl byl postaviti se psy stáda svého.
“Koma tsopano akundinyoza, ana angʼonoangʼono kwa ine, anthu amene makolo awo sindikanawalola kuti azithandizana ndi agalu anga kuweta nkhosa zanga.
2 Ač síla rukou jejich k čemu by mi byla? Zmařena jest při nich starost jejich.
Kodi mphamvu zawo ndi za phindu lanji kwa ine, pakuti mphamvu zawo zinatha kale?
3 Nebo chudobou a hladem znuzeni, utíkali na planá, tmavá, soukromná a pustá místa.
Anali atatheratu kuwonda ndi njala, ankayendayenda mʼdziko lopanda madzi, mʼchipululu usiku.
4 Kteříž trhali zeliny po chrastinách, ano i koření, a jalovec za pokrm byl jim.
Ankathyola therere ndi masamba owawa, ndipo chakudya chawo chinali mizu ya mitengo ya masache.
5 Z prostřed lidí vyháníni byli; povolávali za nimi, jako za zlodějem,
Anapirikitsidwa pakati pa anthu anzawo, akuwakuwiza ngati kuti anali akuba.
6 Tak že musili bydliti v výmolích potoků, v děrách země a skálí.
Anawumirizidwa kukhala ku zigwembe za mitsinje yowuma, pakati pa matanthwe ndi mʼmaenje a mʼnthaka.
7 V chrastinách řvali, pod trní se shromažďovali,
Ankalira ngati nyama kuthengo ndipo ankawunjikana pamodzi pa ziyangoyango.
8 Lidé nejnešlechetnější, nýbrž lidé bez poctivosti, menší váhy i než ta země.
Anali anthu achabechabe ndi wopanda dzina, anathamangitsidwa mʼdziko.
9 Nyní, pravím, jsem jejich písničkou, jsa jim učiněn za přísloví.
“Ndipo tsopano ana awo akundiyimba nyimbo zachipongwe; ineyo ndasanduka chisudzo chawo.
10 V ošklivosti mne mají, vzdalují se mne, a na tvář mou nestydí se plvati.
Iwo amanyansidwa nane ndipo amandithawa; akandiona salephera kundilavulira mʼmaso mwangamu.
11 Nebo Bůh mou vážnost odjal, a ssoužil mne; pročež uzdu před přítomností mou svrhli.
Tsopano pakuti Mulungu wakhwefula uta wanga ndipo wandisautsa, iwowo analekeratu kundiopa.
12 Po pravici mládež povstává, nohy mi podrážejí, tak že šlapáním protřeli ke mně stezky nešlechetnosti své.
Ku dzanja langa lamanja anthu akulimbana nane; andikumbira dzenje loti ndigweremo ndikamayenda, andipangira mitumbira ya nkhondo kuti alimbane nane.
13 Mou pak stezku zkazili, k bídě mé přidali, ač jim to nic nepomůže.
Iwo anditsekera njira; akufuna kundichititsa ngozi, popanda wina aliyense wowaletsa.
14 Jako širokou mezerou vskakují, a k vyplénění mému valí se.
Akundithamangitsa ngati madzi olowera pa mpanda wobowoka, iwo akubwererabwerera pakati pa chipasupasu.
15 Obrátily se na mne hrůzy, stihají jako vítr ochotnost mou, nebo jako oblak pomíjí zdraví mé.
Zoopsa zandithetsa mphamvu; ulemu wanga wachita ngati wauluzika ndi mphepo, chuma changa chija chazimirira ngati mtambo.
16 A již ve mně rozlila se duše má, pochytili mne dnové trápení mého,
“Ndipo tsopano mtima wanga wachokamo; ndili mʼmasiku amasautso.
17 Kteréž v noci vrtá kosti mé ve mně; pročež ani nervové moji neodpočívají.
Mafupa anga akuphwanya usiku pakuti zowawa zanga sizikuleka.
18 Oděv můj mění se pro násilnou moc bolesti, kteráž mne tak jako obojek sukně mé svírá.
Mʼmphamvu zake Mulungu wakhala ngati chovala changa; Iye wandigwira ngati chovala chondithina pa khosi.
19 Uvrhl mne do bláta, tak že jsem již podobný prachu a popelu.
Wandiponya mʼmatope, ndipo ndasanduka ngati fumbi ndi phulusa.
20 Volám k tobě, ó Bože, a neslyšíš mne; postavuji se, ale nehledíš na mne.
“Inu Mulungu, ine ndikulirira kwa Inu, koma simukundiyankha; ndikayimirira, Inu simundiyangʼana nʼkomwe.
21 Obrátils mi se v ukrutného nepřítele, silou ruky své mi odporuješ.
Inuyo mumandichitira zankhanza; mumandizunza ndi dzanja lanu lamphamvu.
22 Vznášíš mne u vítr, sázíš mne na něj, a k rozplynutí mi přivodíš zdravý soud.
Mwandinyamulira ku mphepo ndipo mwandiwulutsa ndi mphepoyo; mwandiponya mʼmphepo ya mkuntho.
23 Nebo vím, že mne k smrti odkážeš, a do domu, do něhož se shromažďuje všeliký živý.
Ndikudziwa kuti Inu mudzandifikitsa ku imfa, kumalo kumene amoyo onse adzapitako.
24 Jistě žeť nevztáhne Bůh do hrobu ruky, by pak, když je stírá, i volali.
“Ndithudi palibe munthu amene amalanga munthu wosweka mtima, amene akupempha thandizo mʼmasautso ake.
25 Zdaliž jsem neplakal nad tím, kdož okoušel zlých dnů? Duše má kormoutila se nad nuzným.
Kodi ine sindinalire nawo iwo amene anali pamavuto? Kodi mtima wanga sunamvere chisoni anthu osauka?
26 Když jsem dobrého čekal, přišlo mi zlé; nadál jsem se světla, ale přišla mrákota.
Koma pamene ndinkayembekezera zabwino, zoyipa ndiye zinandigwera; pamene ndinkafunafuna kuwala, mdima ndiye unandigwera.
27 Vnitřností mé zevřely, tak že se ještě neupokojily; předstihli mne dnové trápení.
Kuwawa kwa mʼkati mwanga sikukuleka; ndili mʼmasiku amasautso.
28 Chodím osmahlý, ne od slunce, povstávaje, i mezi mnohými křičím.
Ndikuyenda wothimbirira, komatu osati ndi dzuwa; ndimayimirira pa msonkhano ndi kupempha chithandizo molira.
29 Bratrem učiněn jsem draků, a tovaryšem mladých pstrosů.
Ndasanduka mʼbale wa nkhandwe, mnzawo wa akadzidzi.
30 Kůže má zčernala na mně, a kosti mé vyprahly od horkosti.
Khungu langa layamba kuda ndipo likufunduka; thupi langa likutentha chifukwa cha kuphwanya kwa thupi.
31 A protož v kvílení obrátila se harfa má, a píšťalka má v hlas plačících.
Pangwe wanga wasanduka woyimbira maliro, ndipo chitoliro changa chikuyimbira anthu olira.