< Jakubův 4 >

1 Odkud jdou bojové a svády mezi vámi? Zdali ne odtud, totiž z líbostí vašich, kteréž rytěřují v oudech vašich?
Nʼchiyani chimene chimayambitsa ndewu ndi mapokoso pakati panu? Kodi sizichokera ku zilakolako zimene zimalimbana mʼkati mwanu?
2 Žádáte, a nemáte; závidíte a dychtíte, a nemůžete dosáhnouti; bojujete a válčíte, a však neobdržíváte, proto že neprosíte.
Mumalakalaka zinthu koma simuzipeza, choncho mumapha. Mumasirira zinthu koma simutha kuzipeza zimene mukufuna, choncho mumakangana ndi kumenyana. Mulibe zinthuzo chifukwa simupempha kwa Mulungu.
3 Prosíte, a nebéřete, proto že zle prosíte, abyste na své líbosti vynakládali.
Koma ngakhale mumapempha simulandira, chifukwa mumapempha ndi zolinga zoyipa. Mumapempha kuti muzigwiritse ntchito pa zokusangalatsani nokha.
4 Cizoložníci a cizoložnice, což nevíte, že přízeň světa jest nepřítelkyně Boží? A protož kdo by koli chtěl býti přítelem tohoto světa, nepřítelem Božím učiněn bývá.
Inu anthu achigololo, kodi simukudziwa kuti kuchita ubwenzi ndi dziko lapansi ndi kudana ndi Mulungu? Choncho, aliyense wosankha kukhala bwenzi la dziko lapansi amasanduka mdani wa Mulungu.
5 Což mníte, že nadarmo dí písmo: Zdali k závisti nakloňuje duch ten, kterýž přebývá v nás?
Kapena mukuganiza kuti Malemba amanena popanda chifukwa kuti Mulungu amafunitsitsa mwansanje mzimu umene Iye anayika kuti uzikhala mwa ife?
6 Nýbrž hojnější dává milost. Nebo dí: Bůh se pyšným protiví, ale pokorným dává milost.
Koma amatipatsa chisomo chochuluka. Nʼchifukwa chake Malemba amati, “Mulungu amatsutsa odzikuza, koma apereka chisomo kwa odzichepetsa.”
7 Poddejtež se tedy Bohu, a zepřete se ďáblu, i utečeť od vás.
Dziperekeni nokha kwa Mulungu. Mukaneni Mdierekezi ndipo adzakuthawani.
8 Přibližte se k Bohu, a přiblížíť se k vám. Umejte ruce, hříšníci, a očisťte srdce vy, kteříž jste dvojité mysli.
Sendezani kufupi ndi Mulungu ndipo Iye adzasendeza kwa inu. Sambani mʼmanja mwanu, inu anthu ochimwa. Yeretsani mitima yanu, inu anthu okayikira.
9 Ssouženi buďte, a kvělte, a plačte; smích váš obratiž se v kvílení, a radost v zámutek.
Chitani chisoni chifukwa cha zimene mwachita, lirani misozi. Kuseka kwanu kusanduke kulira, ndipo chimwemwe chanu chisanduke chisoni.
10 Ponižte se před oblíčejem Páně, a povýšíť vás.
Dzichepetseni pamaso pa Ambuye ndipo Iye adzakukwezani.
11 Neutrhejtež jedni druhým, bratří. Kdož utrhá bratru, a potupuje bratra svého, utrhá zákonu, a potupuje zákon. Tupíš-li pak zákon, nejsi plnitel zákona, ale soudce.
Abale musamanenane. Aliyense wonenera zoyipa mʼbale wake kapena kumuweruza, akusinjirira ndi kuweruza Malamulo. Pamene muweruza malamulo, ndiye kuti simukusunga malamulowo, koma mukuwaweruza.
12 Jedenť jest vydavatel zákona, kterýž může spasiti i zatratiti. Ty kdo jsi, ješto tupíš jiného?
Pali mmodzi yekha Wopereka Malamulo ndi Woweruza. Ndiye amene akhoza kupulumutsa ndi kuwononga. Kodi ndiwe yani kuti uziweruza mnzako?
13 Ale nuže vy, kteříž říkáte: Dnes neb zítra vypravíme se do onoho města, a pobudeme tam přes celý rok, a budeme kupčiti, a něco zištěme;
Tsono tamverani, inu amene mumati, “Lero kapena mawa tipita ku mzinda wakutiwakuti, tikatha chaka chimodzi tikuchita malonda ndi kupanga ndalama.”
14 (Ješto nevíte, co zítra bude. Nebo jaký jest život váš? Pára zajisté jest, kteráž se na maličko ukáže, a potom zmizí.)
Chifukwa chiyani mukutero? Inu simukudziwa zimene ziti zichitike mawa. Kodi moyo wanu ndi wotani? Inu muli ngati nkhungu imene imangooneka kwa kanthawi kochepa ndipo kenaka ndikuzimirira.
15 Místo toho, co byste měli říci: Bude-li Pán chtíti, a budeme-li živi, učiníme toto neb onono.
Koma inuyo muyenera kunena kuti, “Ambuye akalola, tikadzakhala ndi moyo, tidzachita zakutizakuti.”
16 Vy pak chlubíte se v pýše své. Všeliká taková chlouba zlá jest.
Koma mmene zililimu mumangodzitama ndi kudzikuza. Kudzitama konse kotereku ndi koyipa.
17 A protož kdo umí dobře činiti, a nečiní, hřích má.
Aliyense amene amadziwa zabwino zimene amayenera kuchita koma osazichita, ndiye kuti wachimwa.

< Jakubův 4 >