< 1 Mojžišova 35 >

1 Potom mluvil Bůh k Jákobovi: Vstana, vstup do Bethel, a bydli tam; a udělej tam oltář Bohu silnému, kterýž se ukázal tobě, kdyžs utíkal před Ezau bratrem svým.
Tsono Mulungu anati kwa Yakobo, “Nyamuka uchoke kuno kupita ku Beteli. Kumeneko ukamange guwa lansembe la Mulungu amene anadza kwa iwe pamene umathawa Esau, mʼbale wako.”
2 Tedy řekl Jákob čeládce své, a všechněm, kteříž s ním byli: Odvrzte bohy cizí, kteréž máte mezi sebou, a očisťte se, a změňte roucha svá.
Choncho Yakobo anawuza a pa banja pake ndi onse amene anali naye kuti, “Chotsani milungu yachilendo imene muli nayo, ndipo mudziyeretse nokha ndi kusintha zovala zanu.
3 A vstanouce, vstupme do Bethel, a udělám tam oltář silnému Bohu, kterýž vyslyšel mne v den ssoužení mého, a byl se mnou na cestě, kterouž jsem šel.
Tiyeni tinyamuke kuchoka kuno kupita ku Beteli. Kumeneko ndikamumangira guwa lansembe Mulungu amene anandithandiza pa nthawi za masautso anga, komanso amene wakhala nane mʼmayendedwe anga onse.”
4 Tedy dali Jákobovi všecky bohy cizí, kteréž měli, i náušnice, kteréž byly na uších jejich; i zakopal je Jákob pod tím dubem, kterýž byl u Sichem.
Choncho anamupatsa Yakobo milungu yachilendo yonse imene anali nayo pamodzi ndi ndolo. Iye anazikwirira pansi pa mtengo wa thundu ku Sekemu.
5 I brali se odtud. (A byl strach Boží na městech, kteráž byla vůkol nich, a nehonili synů Jákobových.)
Pamenepo ananyamuka, ndipo mtima woopa Mulungu unagwera anthu onse a mʼmizinda yozungulira, kotero kuti palibe aliyense amene anatsatira banja la Yakobo.
6 Tedy přišel Jákob do Lůz, kteréž jest v zemi Kananejské, (to již slove Bethel, ) on i všecken lid, kterýž byl s ním.
Yakobo ndi anthu onse anali naye aja anafika ku Luzi (ku Beteli) mu dziko la Kanaani.
7 I vzdělal tu oltář, a nazval to místo Bůh silný Bethel; nebo tu se mu byl zjevil Bůh, když utíkal před bratrem svým.
Kumeneko anamanga guwa lansembe nalitcha Eli Beteli, chifukwa kunali kumeneko kumene Mulungu anadziwulula yekha kwa Yakobo pamene ankathawa mʼbale wake.
8 Tehdy umřela Debora, chovačka Rebeky, a pochována jest pod Bethel, pod dubem; i nazval jméno jeho Allon Bachuth.
Debora mlezi wa Rakele anamwalira komweko nayikidwa mʼmanda pansi pa mtengo wa thundu cha kumunsi kwa Beteli. Choncho panatchedwa Aloni-Bakuti (mtengo wamaliro).
9 Ukázal se pak opět Bůh Jákobovi, když se navracoval z Pádan Syrské, a požehnal mu.
Yakobo atabwera kuchokera ku Padanaramu, Mulungu anabweranso kwa iye namudalitsa.
10 I řekl jemu Bůh: Jméno tvé jest Jákob. Nebude více nazýváno jméno tvé toliko Jákob, ale Izrael také bude jméno tvé. Protož nazval jméno jeho Izrael.
Mulungu anati kwa iye, “Dzina lako ndiwe Yakobo, koma sudzatchedwanso Yakobo; koma udzatchedwa Israeli.” Choncho anamutcha iye Israeli.
11 Řekl ještě Bůh jemu: Já jsem Bůh silný všemohoucí; rostiž a množ se; národ, nýbrž množství národů bude z tebe, i králové z bedr tvých vyjdou.
Ndipo Mulungu anati kwa iye, “Ine ndine Mulungu Wamphamvuzonse; berekanani ndi kuchulukana. Mtundu wa anthu, inde, mitundu yambiri ya anthu idzatuluka mwa iwe, ndipo ena mwa zidzukulu zako adzakhala mafumu.
12 A zemi tu, kterouž jsem dal Abrahamovi a Izákovi, tobě ji dám; semeni také tvému po tobě dám tu zemi.
Dziko limene ndinapereka kwa Abrahamu ndi Isake ndiliperekanso kwa iwe. Lidzakhala lako ndi la zidzukulu zako.”
13 I vstoupil od něho Bůh z místa, na kterémž mluvil s ním.
Kenaka Mulungu anamusiya Yakobo.
14 Jákob pak vyzdvihl znamení pamětné na místě tom, na kterémž mluvil s ním, sloup kamenný; a pokropil ho skropením, a svrchu polil jej olejem.
Yakobo anayika mwala wachikumbutso pa malo pamene Mulungu anayankhula naye paja. Iye anathirapo nsembe yachakumwa ndi yamafuta.
15 A nazval Jákob jméno místa toho, na kterémž mluvil s ním Bůh, Bethel.
Yakobo anawatcha malo amene Mulungu anayankhula naye aja kuti Beteli.
16 I brali se z Bethel, a bylo již nedaleko do Efraty. I porodila Ráchel, a těžkosti trpěla roděci.
Kenaka anachoka ku Beteli. Koma ali pafupi kufika ku Efurata nthawi yakuti Rakele aone mwana inakwana. Iye anavutika pobereka.
17 A když s těžkostí rodila, řekla jí baba: Neboj se, nebo také tohoto syna míti budeš.
Akanali chivutikire choncho, mzamba anamulimbikitsa nati, “Usaope pakuti ubala mwana wina wamwamuna.”
18 I stalo se, když k smrti pracovala, (nebo umřela, ) nazvala jméno jeho Ben Oni; ale otec jeho nazval ho Beniaminem.
Tsono pamene Rakele ankapuma wefuwefu (popeza ankamwalira) iye anatcha mwana uja kuti Beni-Oni. Koma abambo ake anamutcha kuti Benjamini.
19 I umřela Ráchel, a pochována jest na cestě k Efratě, jenž jest Betlém.
Choncho Rakele anamwalira ndipo anayikidwa pa njira yopita ku Efurata (Kumeneko ndiye ku Betelehemu).
20 A postavil Jákob znamení pamětné nad hrobem jejím; toť jest znamení hrobu Ráchel až do dnešního dne.
Pa manda ake, Yakobo anayimika mwala wachikumbutso wa pa manda ndipo ulipobe mpaka lero.
21 I odebral se odtud Izrael, a rozbil stan svůj za věží Eder.
Israeli (Yakobo) anasunthanso nakamanga tenti yake kupitirira nsanja ya Ederi.
22 Stalo se pak také, když bydlil Izrael v té krajině, že Ruben šel, a spal s Bálou, ženinou otce svého; o čemž uslyšel Izrael. Bylo pak synů Jákobových dvanácte.
Israeli akanali mʼderali, Rubeni anapita nakagonana ndi Biliha, mdzakazi wa abambo ake. Yakobo uja anazimva zimenezi. Yakobo anali ndi ana aamuna khumi ndi awiri:
23 Synové pak Líe: Prvorozený Jákobův Ruben, potom Simeon, a Léví, a Juda, a Izachar, a Zabulon.
Ana a Leya ndi awa: Rubeni anali mwana woyamba wa Yakobo, Simeoni, Levi, Yuda, Isakara, ndi Zebuloni.
24 Synové Ráchel: Jozef a Beniamin.
Ana a Rakele ndi awa: Yosefe ndi Benjamini.
25 A synové Bály, děvky Ráchel: Dan a Neftalím.
Ana a Biliha, wantchito wa Rakele ndi awa: Dani ndi Nafutali.
26 A synové Zelfy, děvky Líe: Gád a Asser. Tiť jsou synové Jákobovi, kteříž mu zrozeni jsou v Pádan Syrské.
Ana a Zilipa wantchito wa Leya ndi awa: Gadi ndi Aseri. Awa ndiwo ana a Yakobo amene anabadwira ku Padanaramu.
27 Tedy přišel Jákob k Izákovi otci svému do Mamre, do města Arbe, jenž jest Hebron, kdežto bydlil pohostinu Abraham a Izák.
Yakobo anafika ku mudzi kwa abambo ake Isake ku Mamre, (kumene kunkatchedwa ku Kiriyati-Ariba kapenanso Hebroni) kumene Abrahamu ndi Isake anakhalako kale.
28 A bylo dnů Izákových sto osmdesáte let.
Isake anakhala ndi moyo zaka 180.
29 I dokonal Izák, a umřel, a připojen jest k lidu svému, stár jsa a plný dnů; i pochovali ho Ezau a Jákob, synové jeho.
Anamwalira ali wokalamba kwambiri ndipo anakakhala ndi anthu a mtundu wake. Ndipo ana ake Esau ndi Yakobo anamuyika mʼmanda.

< 1 Mojžišova 35 >