< 1 Mojžišova 29 >

1 Tedy Jákob vstav, odšel do země východní.
Yakobo anapitiriza ulendo wake kupita ku dziko la anthu a kummawa.
2 A pohleděv, uzřel studnici v poli a tři stáda ovcí, ana se složila při ní; nebo z té studnice napájeli stáda; a kámen veliký byl navrchu studnice.
Atafika kumeneko anaona chitsime ku busa ndipo panali magulu atatu a nkhosa zitagona pafupi ndi chitsimecho chifukwa nkhosazo zimamwetsedwa madzi ochokera mʼchitsimecho. Pamwamba pa chitsimecho panali mwala waukulu.
3 Shánívána pak tam bývala všecka stáda, a teprv odvalovali kámen ten od vrchu té studnice, a napájeli dobytky; potom zas přivalovali kámen na vrch studnice, na místo jeho.
Amati nkhosa zonse zikasonkhana, abusawo ankagudubuza mwalawo, kuwuchotsa ndi kumwetsa madzi nkhosazo. Kenaka ankawubwezera mwalawo pamalo pake, pakamwa pa chitsimepo.
4 Tedy řekl jim Jákob: Bratří moji, odkud jste? Kteřížto odpověděli: Jsme z Cháran.
Yakobo anafunsa abusawo kuti, “Abale anga, mwachokera kuti?” Iwo anayankha, “Tachokera ku Harani.”
5 I řekl jim: Znáte-li Lábana, syna Náchorova? A oni řekli: Známe.
Iye anawafunsanso kuti, “Kodi Labani, mdzukulu wa Nahori mukumudziwa?” Iwo anayankha, “Inde tikumudziwa?”
6 I dí opět k nim: Dobře-li se má? Odpověděli: Dobře, a aj, Ráchel dcera jeho tamto jde s dobytkem.
Ndipo Yakobo anawafunsanso, “Kodi ali bwino?” Iwo anati, “Inde ali bwino. Nayu Rakele mwana wake akubwera apoyu ndi nkhosa.”
7 Tedy řekl: Však ještě daleko do večera, aniž ještě čas, aby dobytek byl sehnán; napojte stáda, a jděte, paste.
Iye anati, “Taonani, dzuwa likanalipo ndipo nthawi yosonkhanitsa nkhosa sinakwane. Bwanji osazimwetsa madzi nkhosazi.”
8 A oni odpověděli: Nemůžeme, než až se všecka stáda seženou, a odvalen bude kámen od svrchku studnice, abychom napojili ovce.
Iwo anayankha, “Ayi sitingatero. Tidikira mpaka nkhosa zonse zisonkhane. Zikatero, tigubuduza mwalawu kuwuchotsa pamwamba pa chitsimepo, kenaka nʼkuzimwetsa madzi nkhosazo.”
9 Když on ještě mluvil s nimi, přišla k tomu Ráchel s stádem otce svého; neb ona pásla stádo.
Ali chiyankhulire nawo, Rakele anafika ndi nkhosa za abambo ake popeza ndiye amene ankaweta nkhosazo.
10 Tedy Jákob uzřev Ráchel, dceru Lábana ujce svého, a stádo jeho, přistoupil a odvalil ten kámen od vrchu studnice, a napojil stádo Lábana ujce svého.
Yakobo ataona Rakele mwana wa Labani, mlongo wa amayi ake, ali ndi nkhosa za Labani, anapita nawugudubuza mwala uja nazimwetsa madzi nkhosa za amalume akezo.
11 A políbil Jákob Ráchel, a povýšiv hlasu svého, plakal.
Kenaka Yakobo anapsompsona Rakele nayamba kulira mokweza.
12 Oznámil jí pak byl Jákob, že jest bratr otce jejího, a že jest syn Rebeky; a ona přiběhši, oznámila to otci svému.
Kenaka Yakobo anawuza Rakele kuti iye ndi mwana wa Rebeka, mlongo wa abambo a Rakele uja. Choncho Rakele anathamanga nakawuza abambo ake.
13 I stalo se, když Lában uslyšel pověst o Jákobovi, synu sestry své, že vyběhl proti němu, a objav ho, políbil, a uvedl do domu svého; on pak vypravoval Lábanovi o všech těch věcech.
Labani atamva za Yakobo, mwana wa mlongo wake, anafulumira kukakumana naye. Anamukupatira napsompsona, napita naye ku nyumba kwake. Yakobo anafotokozera Labani zonse zinachitika.
14 Jemužto odpověděl Lában: Jistě kost má a tělo mé jsi. I zůstal s ním přes celý měsíc.
Ndipo, Labani anati kwa iye, “Iwe ndiwe ndithu fupa ndi mnofu wanga.” Yakobo anakhala ndi Labani mwezi umodzi.
15 Tedy řekl Lában Jákobovi: Zdali proto, že jsi bratr můj, darmo mi sloužiti budeš? Pověz mi, jaká má býti mzda tvá?
Tsono Labani anawuza Yakobo kuti, “Zoona iwe ndi ife ndi abale. Koma suyenera kundigwirira ntchito popanda malipiro. Ndiwuze kuti malipiro ako azikhala wotani?”
16 (Měl pak Lában dvě dcery; jméno starší Lía, a jméno mladší Ráchel.
Tsono Labani anali ndi ana aakazi awiri; dzina la wamkulu linali Leya, ndipo dzina la wamngʼono linali Rakele.
17 Než Lía měla oči mdlé, ale Ráchel byla pěkné postavy a krásné tváři.
Leya anali ndi maonekedwe wofowoka koma Rakele anali wa maonekedwe wokongola kwambiri.
18 I miloval Jákob Ráchel.) Řekl tedy: Buduť sloužiti sedm let za Ráchel, dceru tvou mladší.
Yakobo anakonda Rakele ndipo anati, “Ndidzakugwirirani ntchito kwa zaka zisanu ndi ziwiri chifukwa cha mwana wanu wamngʼono, Rakele.”
19 Odpověděl Lában: Lépeť jest, abych ji tobě dal, nežli bych ji dal muži jinému; zůstaniž se mnou.
Labani anati, “Kuli bwino kuti ndimupereke kwa iwe ameneyu kusiyana ndi munthu wina. Khala ndi ine kuno.”
20 Takž Jákob sloužil za Ráchel sedm let; a bylo před očima jeho jako něco málo dnů, proto že laskav byl na ni.
Choncho Yakobo anagwira ntchito zaka zisanu ndi ziwiri chifukwa cha Rakele. Koma kwa iye zaka zonsezi zinakhala ngati masiku wochepa chifukwa anamukonda Rakele.
21 Potom řekl Jákob k Lábanovi: Dejž mi ženu mou; nebo vyplněni jsou dnové moji, abych všel k ní.
Kenaka Yakobo anati kwa Labani, “Nthawi yanga ndakwanitsa, ndipatseni mwana wanu kuti ndimukwatire.”
22 Tedy sezval Lában všecky muže místa toho, a učinil hody.
Pamenepo Labani anakonza phwando la ukwati, nayitana anthu onse a pamalopo.
23 U večer pak vzav Líu, dceru svou, uvedl ji k němu; a on všel k ní.
Koma pokwana usiku, Labani anatenga mwana wake wamkazi Leya namupatsa Yakobo, ndipo Yakobo anagona naye.
24 Dal také Lában Zelfu děvku svou Líe, dceři své, za služebnici.
Ndipo Labani anapereka wantchito wake wamkazi Zilipa kwa Leya kuti akhale wantchito wake.
25 A když bylo ráno, poznal, že jest Lía. I řekl k Lábanovi: Což jsi mi to učinil? Zdaliž jsem za Ráchel nesloužil u tebe? Pročežs mne tedy oklamal?
Pakucha mmawa, Yakobo anaona kuti anagona ndi Leya. Choncho Yakobo anafunsa Labani, “Nʼchiyani mwandichitirachi? Kodi ine sindinakugwirireni ntchito chifukwa cha Rakele? Bwanji mwandinyenga?”
26 Odpověděl Lában: Nebývá toho v kraji našem, aby vdávána byla mladší dříve, než prvorozená.
Labani anayankha, “Si mwambo wathu kuno kupereka wamngʼono ku banja, wamkulu asanakwatiwe.
27 Vyplň týden této; dámeť potom i tuto za službu, kterouž sloužiti budeš u mne ještě sedm let jiných.
Yamba watsiriza sabata ya chikondwerero cha ukwati wa Leya; kenaka ndidzakupatsanso Rakele. Koma udzayenera kundigwirira ntchito zaka zisanu ndi ziwiri.”
28 I udělal tak Jákob, a vyplnil týden její. Potom dal mu Ráchel dceru svou za manželku.
Yakobo anachitadi momwemo. Anamaliza sabata ya chikondwerero cha Leya, ndipo Labani anamupatsa Rakele kuti akhale mkazi wake.
29 Dal také Lában Ráchel, dceři své, Bálu, děvku svou za služebnici.
Labani anapereka wantchito wake wamkazi Biliha kwa Rakele kuti akhale wantchito wake.
30 Tedy všel také k Ráchel, a miloval ji více než Líu; i sloužil u něho ještě sedm let jiných.
Yakobo analowana ndi mkazi wake Rakele, ndipo Yakobo anakonda Rakele kuposa Leya. Ndipo anamugwirira ntchito Labani zaka zina zisanu ndi ziwiri chifukwa cha Rakele.
31 Vida pak Hospodin, že Lía nemá lásky, otevřel život její; a Ráchel nechal neplodné.
Pamene Mulungu anaona kuti Yakobo sankamukonda Leya kwambiri, Iye analola kuti Leya uja akhale ndi ana, ndi kuti Rakele akhale wosabala.
32 Tedy počala Lía a porodila syna, a nazvala jméno jeho Ruben; nebo řekla: Jistě viděl Hospodin trápení mé; jižť nyní milovati mne bude muž můj.
Leya anakhala ndi pathupi ndipo anabereka mwana wamwamuna. Anamutcha Rubeni pakuti anati, “Yehova waona kusauka kwanga. Zoonadi, mwamuna wanga adzandikonda tsopano.”
33 I počala opět a porodila syna, a řekla: Jistě uslyšel Hospodin, že jsem v nenávisti, protož dal mi i tohoto. A nazvala jméno jeho Simeon.
Anakhalanso ndi pathupi ndipo pamene anabereka mwana wamwamuna anati, “Yehova anamva kuti mwamuna wanga sakundikonda, choncho wandipatsanso mwana winayu.” Ndipo anamutcha dzina lake Simeoni.
34 A opět počala a porodila syna, a řekla: Již nyní připojí se ke mně muž můj, nebo jsem mu porodila tři syny. Z té příčiny nazváno jest jméno jeho Léví.
Anatenganso pathupi kachitatu, ndipo pamene anabereka mwana wamwamuna anati, “Pano pokha tidzaphatikana kwambiri ndi mwamuna wanga, chifukwa ndamubalira ana aamuna atatu.” Kotero anamutcha dzina lake Levi.
35 I počala ještě a porodila syna, a řekla: Již nyní chváliti budu Hospodina. Pročež nazvala jméno jeho Juda; i přestala roditi.
Anatenganso pathupi pena, ndipo pamene anabereka mwana wamwamuna, iye anati, “Nthawi ino ndidzalemekeza Yehova.” Choncho anamutcha Yuda. Kenaka analeka kubereka.

< 1 Mojžišova 29 >