< Ezechiel 12 >

1 I stalo se slovo Hospodinovo ke mně, řkoucí:
Yehova anayankhula nane kuti,
2 Synu člověčí, u prostřed domu zpurného ty bydlíš, kteříž mají oči, aby viděli, však nevidí; uši mají, aby slyšeli, však neslyší, proto že dům zpurný jsou.
“Iwe mwana wa munthu, ukukhala pakati pa anthu owukira, iwowo maso openyera ali nawo, koma sakuona ndipo makutu omvera ali nawo, koma sakumva chifukwa choti ndi anthu owukira.
3 Protož ty, synu člověčí, připrav sobě to, s čím bys se stěhoval, a stěhuj se ve dne před očima jejich. Přestěhuješ se pak z místa svého na místo jiné před očima jejich, zdaby aspoň viděli; nebo dům zpurný jsou.
“Choncho, iwe mwana wa munthu, longedza katundu wako wopita naye ku ukapolo. Unyamuke nthawi yamasana iwo akuona. Uchite ngati wanyamuka kuchoka kumene ukukhala kupita ku dziko lachilendo iwowo akuona. Mwina adzamvetsetsa, paja ndi anthu aupandu.
4 Vynesa pak své věci, jakožto ty, s nimiž se stěhovati máš ve dne před očima jejich, vyjdi u večer před očima jejich, jako ti, kteříž se stěhují.
Utulutse katundu wako wopita naye ku ukapolo nthawi ya masana iwo akuona. Ndipo nthawi ya madzulo, iwo akuona, uchoke monga ngati ukupita ku ukapolo.
5 Před očima jejich prokopej sobě zed, a vynes skrze ni.
Iwo akuona, ubowole pa khoma ndipo utulutsirepo katundu wako.
6 Před očima jejich na rameni nes, po tmě vynes, tvář svou přikrej, a nehleď na zemi; nebo za zázrak dal jsem tě domu Izraelskému.
Usenze katundu wako pa phewa iwo akuona, ndipo upite kunja ku mdima. Uphimbe nkhope yako kuti usaone pansi, pakuti ndakusandutsa iwe chizindikiro chochenjeza Aisraeli.”
7 I učinil jsem tak, jakž rozkázáno bylo. Věci své vynesl jsem, jakožto ty, s nimiž bych se stěhoval ve dne, u večer pak prokopal jsem sobě zed rukou; po tmě jsem je vynesl, na rameni nesa před očima jejich.
Choncho ine ndinachita monga momwe anandilamulira. Nthawi yamasana ndinatulutsa zinthu zanga nditazimanga ngati ndikupita ku ukapolo. Ndipo nthawi yamadzulo ndinabowola khoma ndi manja anga. Pamene chisisira chinkayamba, ndinasenza katundu wanga pa phewa kutuluka naye iwo akuona.
8 Opět stalo se slovo Hospodinovo ke mně ráno, řkoucí:
Mmawa mwake Yehova anandiyankhula nati:
9 Synu člověčí, zdaližť řekli dům Izraelský, dům ten zpurný: Co ty děláš?
“Iwe mwana wa munthu, kodi anthu aupandu a Israeli sanakufunse kuti ukuchita chiyani?
10 Rciž jim: Takto praví Panovník Hospodin: Na kníže v Jeruzalémě vztahuje se břímě toto a na všecken dům Izraelský, kteříž jsou u prostřed něho.
“Uwawuze kuti, ‘zimene ndikunena Ine Ambuye Wamphamvuzonse ndi izi: Uthengawu ndi wonena za kalonga wa ku Yerusalemu pamodzi ndi banja lonse la Israeli amene akukhala kumeneko.’
11 Rciž jim: Já jsem zázrakem vaším. Jakož jsem činil, tak se stane jim, postěhují se a v zajetí půjdou.
Uwawuze kuti, ‘Ndiwe chizindikiro chowachenjeza.’ “Zidzakuchitikirani monga momwe zakuchitikira iwemu. Iwo adzatengedwa kupita ku ukapolo.”
12 A kníže, kteréž jest u prostřed nich, na rameni ponese po tmě a vyjde. Zed prokopají, aby jej vyvedli skrze ni; tvář svou zakryje, tak že nebude viděti okem svým země.
“Kalonga wawo adzatenga katundu wake nʼchisisira nʼkunyamuka. Adzatulukira pa bowo limene anthu anabowola pa khoma. Adzaphimba nkhope yake kuti asaone kumene akupita.
13 Nebo roztáhnu sít svou na něj, a polapen bude do vrše mé, a zavedu jej do Babylona, země Kaldejské, kteréž neuzří, a tam umře.
Ndidzayala ukonde wanga pa iye ndi kumukola mu msampha wanga. Ndidzabwera naye ku Babuloni, dziko la Akaldeya, koma sadzaliona dzikolo, ndipo adzafera kumeneko.
14 Všecky také, kteříž jsou vůkol něho na pomoc jemu, i všecky houfy jeho rozptýlím na všecky strany, a mečem dobytým budu je stihati.
Ine ndidzabalalitsa kumbali zonse zinayi onse okhala naye pafupi, ndiwo omuthandiza ake pamodzi ndi ankhondo ake. Ndidzawalondola ndi lupanga losolola.
15 I zvědí, že já jsem Hospodin, když je rozptýlím mezi národy, a rozženu je po krajinách.
“Iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova, ndikadzawamwaza pakati pa anthu a mitundu ina ndi kuwabalalitsira ku mayiko ena.
16 Pozůstavím pak z nich muže nemnohé po meči, po hladu a po moru, aby vypravovali všecky ohavnosti své mezi národy, kamž se dostanou, i zvědí, že já jsem Hospodin.
Koma ndidzasiyako ena pangʼono amene adzapulumuke ku lupanga, njala ndi mliri, kuti akafotokoze ntchito zawo zonse zonyansa pakati pa anthu achilendo kumene akupitako. Pamenepo adzadziwa kuti ndine Yehova.”
17 Opět stalo se slovo Hospodinovo ke mně, řkoucí:
Pambuyo pake Yehova anandiyankhulanso nati,
18 Synu člověčí, chléb svůj s strachem jez, a vodu svou s třesením a s zámutkem pí,
“Iwe mwana wa munthu, uzinjenjemera ukamadya chakudya chako, ndipo uzinthunthumira ndi mantha ukamamwa madzi ako.
19 A rci lidu země této: Takto praví Panovník Hospodin o obyvatelích Jeruzalémských, o zemi Izraelské: Chléb svůj s zámutkem jísti budou, a vodu svou s předěšením píti, aby obloupena byla země jeho z hojnosti své, pro nátisk všech přebývajících v ní.
Uwawuze anthu a mʼdzikomo kuti izi ndi zimene Ambuye Wamphamvuzonse akunena za anthu okhala mu Yerusalemu ndi dziko la Israeli: Iwo adzadya chakudya chawo ndi mantha ndi kumwa madzi awo ndi nkhawa. Zonse za mʼdziko lawo zidzalandidwa chifukwa cha ziwawa za anthu onse okhala mʼmenemo.
20 Města také, v nichž bydlejí, zpustnou, a země pustá bude, a tak zvíte, že já jsem Hospodin.
Mizinda imene ili ndi anthu idzasakazika ndipo dziko lidzasanduka chipululu. Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”
21 Opět stalo se slovo Hospodinovo ke mně, řkoucí:
Yehova anayankhulanso nane kuti,
22 Synu člověčí, jaké to máte přísloví o zemi Izraelské, říkajíce: Prodlí se dnové, aneb zahyne všeliké vidění?
“Iwe mwana wa munthu, kodi mwambi umene ukunenedwa mu Israeli ndi wotani: ‘Masiku akupita koma masomphenya onse sakukwaniritsidwa?’
23 Protož rci jim: Takto praví Panovník Hospodin: Učiním, aby přestalo přísloví toto, aniž užívati budou přísloví toho více v Izraeli. Rci jim: Nýbrž přiblížili se dnové ti a splnění všelikého vidění.
Choncho uwawuze anthuwo kuti, ‘Ine Ambuye Yehova ndidzawuthetsa mwambi umenewu ndipo sadzawunenanso mu Israeli.’ Uwawuze kuti, ‘masiku ayandikira oti zonse zimene ndinanena mʼmasomphenya zichitikedi.
24 Nebo nebude více žádného vidění marného, a hádání pochlebníka u prostřed domu Izraelského,
Pakuti masiku amenewo sikudzakhalanso masomphenya abodza kapena kuwombeza kwa chinyengo pakati pa anthu a Israeli.
25 Proto že já Hospodin mluviti budu, a kterékoli slovo promluvím, stane se. Neprodlíť se dlouho, ale za dnů vašich, dome zpurný, mluviti budu slovo, a naplním je, praví Panovník Hospodin.
Koma Ine Ambuye ndidzayankhula chimene ndikufuna, ndipo chidzachitikadi, osachedwa ayi. Pakuti mʼmasiku anu omwe ano, inu anthu opanduka, ndidzakwaniritsa chilichonse chimene ndidzanena. Ndikutero Ine Yehova.’”
26 I stalo se slovo Hospodinovo ke mně, řkoucí:
Yehova anandiyankhula nati:
27 Synu člověčí, aj, dům Izraelský říkají: Vidění to, kteréž vidí tento, ke dnům mnohým patří, a na dlouhé časy tento prorokuje.
“Iwe mwana wa munthu, Aisraeli akunena kuti, ‘masomphenya amene ukuona sadzachitika kwa zaka zambiri. Iwo akuti ukulosa za zinthu zimene zidzachitika ku tsogolo kwambiri.’
28 Protož rci jim: Takto praví Panovník Hospodin: Neprodlíť se dlouho všeliké slovo mé, ale slovo, kteréž mluviti budu, stane se, praví Panovník Hospodin.
“Choncho uwawuze kuti, ‘zimene Ine Ambuye Yehova ndikunena ndi izi: Zonena zanga sizidzachedwanso; chilichonse chimene ndikunena chidzachitikadi. Ndikutero Ine Yehova.’”

< Ezechiel 12 >