< Ester 6 >
1 Té noci král nemoha spáti, rozkázal přinésti knihy pamětné, kroniky, kteréž čteny byly před králem.
Usiku umenewo mfumu inalephera kugona tulo; Choncho inayitanitsa buku limene amalembamo mbiri ya zamakedzana kuti amuwerengere.
2 I našli zapsáno, že pověděl Mardocheus na Bigtana a Teresa, dva komorníky královské z těch, jenž ostříhali prahu, že ukládali vztáhnouti ruku na krále Asvera.
Anapeza kuti mʼbukumo munalembedwa zoti Mordekai anawulula kuti Bigitana ndi Teresi, awiri mwa adindo ofulidwa a mfumu amene ankalondera pa khomo la chipinda cha mfumu ndiwo anakonza chiwembu chofuna kupha mfumu Ahasiwero.
3 Tedy řekl král: Čím jest poctěn, neb jak zveleben Mardocheus za to? Odpověděli služebníci královští, dvořané jeho: Není jemu nic dáno.
Mfumu inafunsa kuti, “Kodi Mordekai anamupatsa ulemu ndi ukulu wotani chifukwa cha chinthu chimene anachitachi?” Atumiki ake anamuyankha kuti, “Palibe chimene chinachitika kwa iye.”
4 I řekl král: Kdo jest v síni? (Aman pak byl přišel do síně domu královského zevnitřní, mluviti s králem, aby oběšen byl Mardocheus na šibenici, kterouž jemu připravil.)
Mfumu inati, “Kodi ndani ali mʼbwalomo?” Tsono Hamani anali atangolowa kumene mʼbwalo lakunja la nyumba yaufumu kuti akawuze mfumu zomukhomera Mordekai pa mtanda umene anamukonzera.
5 Odpověděli králi služebníci jeho: Aj, Aman stojí v síni. Řekl král: Nechť vejde sem.
Atumiki ake anamuyankha kuti, “Hamani ndiye wayima mu bwalo.” “Mulowetseni,” Mfumu inalamulira.
6 Takž všel Aman. Jemuž řekl král: Co sluší učiniti muži tomu, kteréhož by chtěl král ctíti? (Aman řekl sám v sobě: Kohož by jiného chtěl král více ctíti, nežli mne?)
Hamani atalowa, mfumu inamufunsa kuti, “Kodi timuchitire ulemu otani munthu amene mfumu ikondweretsedwa naye?” Tsono Hamani anaganiza mu mtima kuti, “Kodi palinso ndani amene mfumu ingamulemekeze kuposa ine?”
7 Odpověděl Aman králi: Muži tomu, jehož král ctíti chce,
Choncho Hamani anayankha mfumuyo kuti, “Munthu amene mfumu ifuna kumuchitira ulemu, imuchitire izi:
8 Ať přinesou roucho královské, do kteréhož se král obláčí, a přivedou koně, na kterémž jezdí král, a vstaví korunu královskou na hlavu jeho.
Anthu abwere ndi chovala cha ufumu ndi kavalo amene mfumu imakwerapo wokhala ndi chizindikiro chaufumu pamutu pake.
9 A dadouce roucho to i koně toho v ruku některého z nejznamenitějších knížat královských, ať oblekou muže toho, jehož král chce ctíti, a ať jej vodí na koni po ulici města, a volají před ním: Tak se má státi muži tomu, jehož král ctíti chce.
Ndipo mupereke chovala cha ufumucho ndi kavalo kwa mmodzi wa akalonga a mfumu a ulemu kwambiri. Ameneyu amuveke chovalacho munthu amene mfumu yakondweretsedwa naye. Akavekedwa chovalachi amuyendetse mʼmisewu yonse ya mzinda atakwera pa kavalo wa mfumu. Kalongayu azifuwula patsogolo pa munthuyu kuti ‘Ichi ndi chimene mfumu yachita kwa munthu amene yafuna kumuchitira ulemu!’”
10 Tedy řekl král Amanovi: Pospěš, vezmi to roucho a koně, jakž jsi řekl, a učiň to Mardocheovi Židu, kterýž sedí v bráně královské. Nepomíjejž ničeho ze všeho toho, což jsi mluvil.
Mfumu inalamulira Hamani kuti, “Pita msanga, katenge chovala cha ufumu ndi kavalo ndipo uchite monga wanenera kwa Mordekai Myuda, amene amakhala pa chipata cha mfumu. Usasiyeko china chilichonse chimene wanena.”
11 Protož vzav Aman roucho i koně, oblékl Mardochea, a vedl jej na koni po ulici města, volaje před ním: Tak se má státi muži tomu, jehož král ctíti chce.
Choncho Hamani anatenga chovala ndi kavalo. Anamuveka Mordekai chovalacho ndipo anamuyendetsa mʼmisewu yonse ya mu mzinda atakwera pa kavalo, akufuwula kuti, “Ichi ndi chimene mfumu yachita kwa munthu amene yafuna kumuchitira ulemu!”
12 Potom navrátil se Mardocheus k bráně královské. Aman pak rychle pospíšil do domu svého, smuten jsa, s zakrytou hlavou.
Pambuyo pake Mordekai anabwerera ku chipata cha mfumu. Koma Hamani anapita msanga ku nyumba kwake, akulira, atafundira mutu wake.
13 I vypravoval Aman Zeres ženě své a všechněm přátelům svým všecko, což se mu přihodilo. I řekli jemu mudrci jeho i Zeres žena jeho: Poněvadž z národu Židovského jest Mardocheus, před jehož oblíčejem počal jsi klesati, neodoláš jemu, ale jistě padneš před oblíčejem jeho.
Hamani anawuza Zeresi mkazi wake ndi abwenzi ake onse zonse zinamuchitikira. Anthu ake anzeru ndi mkazi wake Zeresi anamuwuza kuti, “Popeza kuti Mordekai ndi Myuda amene mwayamba kale kugonja pamaso pake, ndiye kuti palibe chimene mungachitepo. Mudzagwa ndithu pamaso pake.”
14 A když oni ještě mluvili s ním, komorníci královští přišli, a rychle vzali Amana na hody, kteréž připravila Ester.
Pamene anthuwa amayankhula nayebe, adindo a mfumu ofulidwa anabwera kudzamutenga Hamani mofulumira kupita naye ku phwando limene Estere anakonza.