< 5 Mojžišova 28 >

1 Jestliže pak opravdově poslušen budeš hlasu Hospodina Boha svého, ostříhaje a čině všecka přikázaní jeho, kteráž já dnes přikazuji tobě, vyvýší tě Hospodin Bůh tvůj nade všecky národy země.
Ngati mumvera Yehova Mulungu wanu ndi kutsatira mosamalitsa malamulo ake onse amene ndikukupatsani lero lino, Yehova Mulungu wanu adzakukwezani pamwamba pa mitundu yonse ya pa dziko lapansi.
2 A přijdou na tě všecka požehnání tato, a vyplní se při tobě, když jen poslušen budeš hlasu Hospodina Boha svého.
Madalitso awa adzabwera kwa inu ndi kuyenda nanu ngati mumvera Yehova Mulungu wanu:
3 Požehnaný budeš v městě, požehnaný i na poli.
Mudzadalitsika mʼmizinda yanu ndi kudalitsika mʼdzikolo.
4 Požehnaný plod života tvého, úrody země tvé, i plod dobytka tvého, prvorozené skotů tvých i stáda bravů tvých.
Yehova adzadalitsa ana anu, zokolola za mʼdziko lanu, ngʼombe zanu pamodzi ndi ziweto zanu zonse.
5 Požehnaný koš tvůj i díže tvá.
Dengu lanu ndi chiwaya chanu cha buledi zidzadalitsika.
6 Požehnaný budeš vcházeje, požehnaný i vycházeje.
Mudzadalitsika pa kulowa kwanu ndi pa kutuluka kwanu.
7 A učiní Hospodin, že nepřátelé tvoji, kteříž by povstali proti tobě, poraženi budou před tebou; jednou cestou vytáhnou proti tobě, a sedmi cestami před tebou utíkati budou.
Yehova adzaonetsetsa kuti adani anu amene adzakuwukirani agonjetsedwe pamaso panu. Iwo adzabwera kwa inu kuchokera mbali imodzi koma adzakuthawani ku mbali zisanu ndi ziwiri.
8 Přikáže Hospodin požehnání svému, aby s tebou bylo v špižírnách tvých a při všem, k čemu bys koli přičinil ruku svou, a požehná tobě v zemi, kterouž Hospodin Bůh tvůj dává tobě.
Yehova adzatumiza madalitso pa nkhokwe zanu ndi pa chilichonse chimene muchikhudza. Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani mʼdziko limene akukupatsani.
9 Vystaví tě sobě Hospodin za lid svatý, jakož zapřisáhl tobě, když ostříhati budeš přikázaní Hospodina Boha svého, a choditi po cestách jeho.
Yehova Mulungu wanu adzachititsa kuti mukhale anthu ake opatulika, monga momwe analonjezera pa malumbiro ake, ngati musunga malamulo ake ndi kuyenda mʼnjira zake.
10 I uzří všickni národové země, že jméno Hospodinovo vzýváno jest nad tebou, a budou se báti tebe.
Pamenepo anthu onse a dziko lapansi adzaona kuti mumadziwika ndi dzina la Yehova ndipo adzakuopani.
11 Učiní také Hospodin, že hojnost míti budeš všeho dobrého, plodu života svého, i plodu dobytků svých, i úrod zemských v zemi, kterouž s přísahou zaslíbil otcům tvým, že ji tobě dá.
Yehova adzakupambanitsani kwambiri ndipo adzakupatsani ana ambiri, ziweto zambiri, ndi zokolola zochuluka, mʼdziko limene Yehova analumbira kwa makolo anu kuti adzakupatsani.
12 Otevře Hospodin tobě poklad svůj výborný, nebe, aby vydalo déšť zemi tvé časem svým, a požehná všelikému dílu ruky tvé, tak že mnohým národům půjčovati budeš, sám pak nic nevypůjčíš.
Yehova adzatsekula kumwamba kumene amasungirako chuma chake, kutumiza mvula mʼdziko lanu pa nthawi yake ndi kudalitsa ntchito yonse ya manja anu. Mudzakongoza mitundu yambiri koma inu simudzakongola kwa aliyense.
13 I ustanoví tě Hospodin za hlavu a ne za ocas, a budeš vždycky vyšší, a nikdy nižší, když poslouchati budeš přikázaní Hospodina Boha svého, kteráž já dnes tobě přikazuji, abys ostříhal a činil je.
Yehova adzakuthandizani kukhala mutu osati mchira. Mukakhala ndi chidwi ndi malamulo a Yehova Mulungu wanu amene ndikukupatsani lero lino ndi kuwatsata mosamalitsa, inu mudzakhala apamwamba nthawi zonse osati apansi.
14 A neuchýlíš se od žádného slova, kteráž já dnes přikazuji tobě, ani na pravo ani na levo, odcházeje po bozích cizích, abys jim sloužil.
Musapatukire ku dzanja lamanja kapena lamanzere pa lamulo lina lililonse limene ndikukupatsani lero lino ndi kumatsatira kapena kuyitumikira milungu ina.
15 Jestliže pak hlasu Hospodina Boha svého poslouchati, a všech přikázaní a ustanovení jeho, kteráž já dnes přikazuji tobě, ostříhati a činiti nebudeš, přijdou na tě všecka zlořečenství tato a postihnou tě.
Koma ngati simumvera Yehova Mulungu wanu ndi kusatsata mosamalitsa malamulo ake ndi malangizo ake onse amene ndikukupatsani lero lino, matemberero awa adzabwera pa inu ndikukugonjetsani:
16 Zlořečený budeš v městě, zlořečený i na poli.
Mudzatembereredwa mu mzinda ndi kutembereredwa mʼmudzi.
17 Zlořečený koš tvůj, a zlořečená díže tvá.
Dengu lanu ndi chiwaya chanu cha buledi zidzatembereredwa.
18 Zlořečený plod života tvého i úrody země tvé, prvorozené skotů tvých i stáda bravů tvých.
Zipatso za mʼmimba mwanu zidzatembereredwa, ndiponso zomera za mʼdziko lanu, ana angʼombe zanu ndi ana ankhosa zanu zidzatembereredwa.
19 Zlořečený budeš vcházeje, zlořečený i vycházeje.
Mudzatembereredwa pa kulowa kwanu ndi pa kutuluka kwanu.
20 Pošle Hospodin na tě zlořečení, zkormoucení a bídu při všem, k čemuž bys koli přičinil ruky své a což bys koli dělal, dokudž nebudeš vyhlazen, a nezahyneš v náhle pro zlé skutky tvé, skrze něž jsi opustil mne.
Yehova adzakutumizirani matemberero, chisokonezo ndi minyozo pa chilichonse chimene mudzachichita mpaka mudzawonongedwa ndi kukhala bwinja mofulumira chifukwa cha zoyipa zimene mwazichita pa kumutaya Yehova.
21 Dopustí Hospodin, aby se přídržely tebe morní bolesti, až tě i vypléní z země, do níž se béřeš, abys ji dědičně opanoval.
Yehova adzakugwetserani mliri wa matenda mpaka atakuwonongani mʼdziko limene mukulowa kukalitengali.
22 Bíti tě bude Hospodin souchotinami, zimnicí, pálivostí, horkem, mečem, suchem a rudou, a budou tě stíhati, až tě i zkazí.
Yehova adzakukanthani ndi nthenda yowondetsa, ya malungo ndi ya zotupatupa, ndi kutentha kwakukulu ndi chilala, ndi chinsikwi ndi chiwawu zimene zidzakusautsani mpaka mutawonongeka.
23 I to nebe, kteréž jest nad hlavou tvou, bude měděné, a země, kteráž jest pod tebou, železná.
Mitambo ya pamutu panu idzawuma ngati mkuwa ndipo sidzagwetsa mvula mpaka nthaka yanu idzawuma gwaa ngati chitsulo.
24 Dá Hospodin zemi tvé místo deště prach a popel, a toť s nebe sstoupí na tě, dokudž bys nebyl vyhlazen.
Mʼmalo mwa mvula Yehova adzakupatsani fumbi ndi dothi ndipo lidzakugwerani kuchokera kumwamba mpaka mutawonongeka.
25 Učiní i to Hospodin, že poražen budeš od nepřátel svých; jednou cestou vytáhneš proti nim, a sedmi cestami utíkati budeš od tváři jejich, a musíš se smýkati po všech královstvích země.
Yehova adzalola kuti adani anu akugonjetseni. Mudzadzera njira imodzi pokalimbana ndi adani anu koma pothawa mudzabalalika mbali zisanu ndi ziwiri. Mudzakhala chinthu chochititsa mantha pakati pa maufumu onse a dziko lapansi.
26 I budou těla vaše mrtvá za pokrm všemu ptactvu nebeskému, a šelmám zemským, a nebude, kdo by je odehnal.
Mitembo yanu idzadyedwa ndi mbalame zamumlengalenga ndi nyama zakutchire, ndipo palibe amene adzaziyingitse.
27 Raní tě Hospodin vředem Egyptským, neduhy na zadku, prašivinami a svrabem nezhojitelným.
Yehova adzakusautsani ndi zithupsa za ku Igupto ndi zotupatupa, zipere, ndi mphere zimene simudzachiritsika nazo.
28 Raní tě Hospodin pominutím smyslu, slepotou a tupostí srdce,
Yehova adzakusautsani inu ndi misala, khungu ndi chisokonekero cha maganizo.
29 Tak že o poledni makati budeš, jako maká slepý ve tmě, a nebudeš míti prospěchu na cestách svých; k tomu také utiskán budeš, a loupen po všecky dny, a nebude, kdo by tě vysvobodil.
Masanasana mudzayenda ngati muli mu mdima, kumafufuzira njira ngati wosaona. Mudzakhala olephera pa chilichonse mungachite. Tsiku ndi tsiku mudzaponderezedwa ndi kuberedwa wopanda wokupulumutsani.
30 Manželku sobě zasnoubíš, a jiný s ní obývati bude; dům vystavíš, a nebudeš bydliti v něm; vinici štípíš, a sbírati na ní nebudeš.
Mudzachita chinkhoswe ndi mkazi, koma wina adzakulandani ndi kumukwatira. Mudzamanga nyumba koma simudzagonamo. Mudzalima munda wamphesa koma simudzadyako zipatso zake.
31 Vůl tvůj před tvýma očima zabit bude, a ty jeho jísti nebudeš; osel tvůj uchvácen bude před tváří tvou, anižť se zase navrátí; dobytek tvůj vydán bude nepřátelům tvým, a žádný ho nevysvobodí.
Ngʼombe yanu yamtheno idzaphedwa inu muli pomwepo koma simudzadyako. Bulu wanu adzalandidwa kwa inu mwamakani osabwera nayenso. Nkhosa zanu zidzapatsidwa kwa adani anu, ndipo palibe amene adzazipulumutsa.
32 Synové tvoji a dcery tvé cizímu národu vydáni budou, a oči tvé na to hledíce, umdlívati budou pro ně celého dne, a nebude síly v ruce tvé.
Ana anu aamuna ndi aakazi adzaperekedwa kwa anthu a mitundu ina ndipo inu mudzafika potopa ndi kulefuka nʼkudikirira tsiku ndi tsiku kuti mwina anawo abwerako.
33 Úrody země tvé i všecko úsilí tvé sžíře národ, kteréhož ty neznáš, a nebudeš než potlačený a potřený po všecky dny.
Anthu amene simukuwadziwa adzakudyerani zokolola zanu, ndipo mudzakhala mukuponderezedwa mwankhanza masiku onse.
34 A omámený budeš nad těmi věcmi, kteréž viděti budou oči tvé.
Zimene muzidzaziona zidzakusokonezani mitu.
35 Raní tě Hospodin vředem nejhorším na kolenou i na lýtkách, tak že se nebudeš moci zhojiti, od spodku nohy tvé až do vrchu hlavy.
Yehova adzakusautsani ndi zithupsa zaululu ndi zosachiritsika za mʼmawondo ndi mʼmiyendo ndipo zidzafalikira kuchoka kuphazi mpaka kumutu.
36 Zavede tě Hospodin i krále tvého, kteréhož ustanovíš nad sebou, do národu, kteréhož jsi ty neznal, ani předkové tvoji, a sloužiti tam budeš bohům cizím, dřevu a kameni.
Yehova adzakuthamangitsirani, inu ndi mafumu anu amene muwayika, ku dziko losadziwika kwa inu ndi kwa makolo anu. Kumeneko mudzakapembedza milungu ina, milungu ya mitengo ndi miyala.
37 A budeš k užasnutí a přísloví i v rozprávku všechněm národům, mezi kteréž zavede tě Hospodin.
Inu mudzakhala chinthu chochititsa mantha kuchisunga ndiponso chinthu chotukwanidwa ndi chonyozeka kwa anthu a mitundu yonse kumene Yehova adzakuthamangitsirani.
38 Mnoho semene vyneseš na pole k rozsívání, a málo shromáždíš, nebo sžerou to kobylky.
Mudzadzala mbewu zambiri ku munda koma mudzakolola pangʼono, chifukwa dzombe lidzaziwononga.
39 Vinice štípíš a dělati je budeš, ale vína píti ani sbírati nebudeš, nebo červ sžíře je.
Mudzadzala mpesa ndi kulimirira koma vinyo wake simudzamumwa kapena kukolola mphesazo, chifukwa mphutsi zidzadya mphesazo.
40 Olivoví hojnost míti budeš ve všech končinách svých, a však olejem se pomazovati nebudeš, nebo sprchne ovoce s olivy tvé.
Mudzakhala ndi mitengo ya olivi mʼdziko lanu lonse koma simudzagwiritsa ntchito mafuta ake, chifukwa zipatso zake zidzayoyoka.
41 Synů a dcer naplodíš, a nebudeš jich míti, nebo zajati budou.
Mudzabereka ana aamuna ndi aakazi koma sadzakhala anu, chifukwa adzapita ku ukapolo.
42 Všecko stromoví tvé i úrody země tvé kobylky zkazí.
Magulumagulu a dzombe adzawononga mitengo yanu ndi mbewu za mʼdziko lanu.
43 Cizozemec, kterýž s tebou přebývá, vzroste nad tebe, ty pak velice ponižovati se musíš.
Mlendo wokhala pakati panu adzatukuka kuposa inu, koma inuyo mudzaloweralowera pansi.
44 On půjčovati bude tobě, a ty nebudeš míti, co bys půjčil jemu; on bude přednější, a ty poslednější.
Iye adzakubwereketsani, koma inu simudzatha kubwereketsa. Iye adzakhala mutu ndipo inu mudzakhala mchira.
45 A přijdou na tebe všecka zlořečenství tato a stíhati tě budou, a obklíčí tě, až i zahyneš, jestliže bys neuposlechl hlasu Hospodina Boha svého, a neostříhal přikázaní a ustanovení jeho, kteráž přikázal tobě.
Matemberero onsewa adzabwera pa inu. Adzakulondolani ndi kukugonjetsani mpaka mutawonongeka, chifukwa simunamvere Yehova Mulungu wanu ndi kusunga malamulo ndi malangizo amene anakupatsani.
46 A budou rány tyto znamením a zázrakem na tobě i semeni tvém až na věky,
Matemberero amenewa adzakhala chizindikiro ndi chozizwitsa kwa inu ndi zidzukulu zanu mpaka kalekale.
47 Proto že jsi nesloužil Hospodinu Bohu svému s potěšením a veselím srdce, maje hojnost všech věcí.
Pakuti inu simunatumikire Yehova Mulungu wanu pa nthawi imene zinthu zinkakuyenderani bwino,
48 A protož nepříteli svému, kteréhož poslal na tebe Hospodin, sloužiti musíš v hladu, žízni, v nahotě a v nedostatku všech věcí; a vloží na šíji tvou jho železné, dokudž tě nesetře.
chomwecho pa nthawi ya njala ndi ludzu, ya maliseche ndi umphawi woopsa, mudzatumikira adani amene Yehova adzakutumizirani. Iye adzayika goli lachitsulo mʼkhosi mwanu kufikira atakuwonongani.
49 Přivede Hospodin na tebe národ z daleka, od nejdalších končin země, jako letí orlice, národ, jehož jazyku nerozumíš,
Yehova adzakutumizirani mtundu wa anthu kuchokera kutali kumapeto kwa dziko lapansi nudzachita ngati mphungu yowulukira pansi, mtundu wa anthu umene chiyankhulo chawo simudzachimva,
50 Národ nestydatý, kterýž ani starce nebude šanovati, a nad dítětem se neslituje.
mtundu wooneka wochititsa mantha, wopanda ulemu kwa okalamba kapena chisoni kwa ana.
51 A sžíře plod dobytků tvých i úrody země tvé, dokudž nebudeš vyhlazen; a nezanechá tobě obilí, vína mladého a oleje, prvorozeného z skotů tvých, ani stáda bravů tvých, až tě i vyhladí.
Iwo adzagwira ana a ziweto zanu, natenga zokolola za mʼdziko lanu kufikira mutawonongeka. Iwo sadzakusiyirani tirigu, vinyo watsopano kapena mafuta a olivi, kapena mwana wangʼombe aliyense kapena mwana wankhosa mpaka mutasanduka bwinja.
52 A oblehne tě ve všech městech tvých, dokudž by nepadly zdi tvé vysoké a pevné, v nichž ty doufáš po vší zemi své; obležen, pravím, budeš ve všech městech svých, po vší zemi své, kterouž Hospodin Bůh tvůj dal tobě,
Iwo adzathira nkhondo mizinda yonse mʼdziko lanu lonse mpaka malinga anu ataliatali omwe mumadalira aja atagwa. Adzathira nkhondo mizinda yonse ya mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani.
53 Tak že v obležení a ssoužení, jímž ssouží tě nepřítel tvůj, jísti budeš plod života svého, maso synů svých a dcer svých, kteréž by dal tobě Hospodin Bůh tvůj.
Chifukwa cha zosautsa zimene mdani wanu adzabweretsa pa nthawi yokuthirani nkhondo, inu mudzadya ana anu, mnofu wa ana anu aamuna ndi aakazi amene Yehova Mulungu wanu wakupatsani.
54 Člověk mezi vámi rozmazaný a v rozkoši schovaný záviděti bude bratru svému, i vlastní ženě své, i ostatním synům svým, kterýchž ještě zanechal,
Ngakhale munthu woleza mtima ndi wachifundo kwambiri pakati panu sadzakhala ndi chifundo pa mʼbale wake weniweni kapena mkazi wake amene iye amamukonda kapena ana ake otsalawo,
55 Tak že neudělí žádnému z nich masa synů svých, kteréž jísti bude, proto že nezůstalo jemu nic jiného v obležení a v ssoužení, jímž ssouží tě nepřítel tvůj ve všech městech tvých.
ndipo sadzagawirako aliyense wa iwo mnofu wa ana ake amene akudyawo. Kadzakhala kali komweko basi kamene kamutsalira chifukwa cha msautso umene mdani wanu adzagwetsa pa nthawi yothira nkhondo mizinda yanu yonse.
56 Rozmazaná mezi vámi a v rozkoši schovaná žena, kteráž rozmazaností a rozkoší velikou ledva nohou země se dotkla, vlastnímu muži svému a synu svému i dceři své,
Mayi woleza mtima ndi wachifundo kwambiri pakati panu, uja woti sangayerekeze kuponda pansi, adzabisira mwamuna wake amene amamukonda ndi ana ake omwe aamuna ndi aakazi
57 Také i lůžka svého, kteréž z ní vychází při porodu, ano i synů svých, kteréž zplodí, záviděti bude; nebo jísti je bude tajně pro nedostatek všech věcí v obležení a ssoužení, jímž ssouží tě nepřítel tvůj v městech tvých.
zotsalira za uchembere zochoka mʼmimba mwake ndi ana amene wabereka. Pakuti adzafuna kuti adye zimenezi yekha mobisa pa nthawi yothiridwa nkhondo chifukwa cha masautso amene mdani wanu adzagwetsa pa inu mʼmizinda yanu.
58 Nebudeš-li ostříhati a činiti všech slov zákona tohoto, kteráž psána jsou v knize této, abys se bál toho veleslavného a hrozného jména Hospodina Boha svého:
Ngati simutsata mosamalitsa mawu onse a malamulo awa amene alembedwa mʼbuku lino, komanso ngati simuopa dzina la ulemerero ndi loopsa, dzina la Yehova Mulungu wanu,
59 Rozmnoží ku podivení Hospodin rány tvé, a rány semene tvého, rány veliké a trvánlivé, i nemoci těžké a dlouhé.
Yehova adzatumiza pa inu ndi zidzukulu zanu miliri yoopsa, zosautsa zowawa ndi zokhalitsa, ndi matenda aakulu ndi ovuta kuchiritsika.
60 A obrátí na tebe všecky neduhy Egyptské, jichžs se strašil, a přichytí se tebe.
Adzakubweretserani matenda onse a ku Igupto aja mumawaopawa ndipo adzakukanirirani.
61 Všelijaký také neduh a všelikou ránu, kteráž není psána v knize zákona tohoto, uvede Hospodin na tebe, dokudž nebudeš vyhlazen.
Yehova adzakubweretseraninso mtundu uliwonse wa matenda ndi zosautsa zimene sizinalembedwe mʼbuku la malamulo lino, mpaka mutawonongeka.
62 A zůstane vás maličko, ješto vás prvé bylo mnoho, jako hvězd nebeských, proto že jsi neposlouchal hlasu Hospodina Boha svého.
Inu aja munali ochuluka ngati nyenyezi zakumwamba mudzatsala ochepa chabe chifukwa simunamvere Yehova Mulungu wanu.
63 I stane se, že jakož se veselil Hospodin nad vámi, dobře vám čině a rozmnožuje vás, tak veseliti se bude Hospodin nad vámi, když vás zkazí a vyhladí, a vypléněni budete z země, do kteréž jdete, abyste dědičně vládli jí.
Monga kunamukomera Yehova kukulemeretsani ndi kukuchulukitsani, momwemonso kudzamukondweretsa kukunthani ndi kukuwonongani. Inu mudzazulidwa kukuchotsani mʼdziko limene mukulowa kukalitengali.
64 A rozptýlí tě Hospodin mezi všecky národy, od jednoho konce země až do druhého, a budeš tam sloužiti bohům cizím, kterýchž ty neznáš, ani otcové tvoji, dřevu a kameni.
Kenaka Yehova adzakubalalitsani pakati pa anthu a mitundu yonse, kuchokera ku mapeto a dziko kufika ku mapeto ena. Kumeneko mudzapembedza milungu ina, milungu ya mitengo ndi ya miyala, imene inu eni kapena makolo anu sanayidziwepo.
65 A mezi národy těmi neoddechneš, aniž bude míti odpočinutí spodek nohy tvé; tam také dá Hospodin tobě srdce lekavé, a oči blíkavé, a truchlost mysli.
Pakati pa mitundu ya anthu imeneyi simudzapeza mpata, popanda malo woti nʼkuyikapo phazi. Kumeneko Yehova adzakupatsani moyo wa nkhawa, maso otopa ndi chiyembekezo, ndi mtima wosakhazikika.
66 I bude život tvůj nejistý před tebou, a strašiti se budeš v noci i ve dne, a nikdež nebudeš jist svým životem.
Inu mudzakhala osakhazikika mopitirira, odzazidwa ndi mantha usiku ndi usana womwe, osowa chitsimikizo cha pa moyo wanu.
67 Ráno díš: Ó by již byl večer! a večer díš: Ó by již bylo jitro! pro strach srdce svého, jímž se lekáš, a pro ty věci, na něž očima svýma hleděti musíš.
Mmawa muzidzati, “Chikhala anali madzulo!” ndipo madzulo mudzati, “Chikhala unali mmawa!” Mudzanena zimenezi chifukwa cha mantha amene adzakhale mu mtima mwanu ndi chifukwa cha zomwe muzidzaziona.
68 A zavede tě Hospodin do Egypta na lodech, cestou, o níž jsem řekl tobě: Nebudeš jí viděti více; a tam prodávati se budete nepřátelům svým za služebníky a děvky, a nebude, kdo by koupil.
Yehova adzakubwezani ku Igupto pa sitima zapamadzi paulendo umene Ine ndinati musawuyendenso. Kumeneko mudzadzitsatsa nokha kwa adani anu monga akapolo aamuna ndi aakazi, koma palibe amene adzakuguleni.

< 5 Mojžišova 28 >