< 5 Mojžišova 15 >
1 Každého léta sedmého odpouštěti budeš.
Kumapeto kwa zaka zisanu ndi ziwiri zilizonse, muzikhululukirana ngongole.
2 Tento pak bude způsob odpuštění, aby odpustil každý věřitel, kterýž rukou svou půjčil to, čehož půjčil bližnímu svému; nebude upomínati bližního svého aneb bratra svého, nebo vyhlášeno jest odpuštění Hospodinovo.
Zimenezi muzichita motere: wobwereketsa aliyense adzakhululukira ngongole imene anabwereketsa kwa Mwisraeli mnzake. Iye asadzafunenso kuti Mwisraeli mnzakeyo kapena mʼbale wake amubwezere chifukwa nthawi ya Ambuye yokhululukirana ngongole yalengezedwa.
3 Cizozemce upomínati budeš, ale to, což bys měl u bratra svého, propustí ruka tvá.
Mukhoza kulonjerera ngongole kwa mlendo, koma mukhululukire ngongole ina iliyonse imene mʼbale wanu ali nayo.
4 Toliko aby nuzným někdo nebyl příčinou tvou, poněvadž hojně požehná tobě Hospodin v zemi, kterouž Hospodin Bůh tvůj dá tobě v dědictví, abys jí dědičně vládl:
Komabe pasadzakhale wosauka pakati panu chifukwa Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani kwambiri mʼdziko limene adzakupatsani kuti likhale lanu ngati cholowa chanu.
5 Jestliže však pilně poslouchati budeš hlasu Hospodina Boha svého, tak abys hleděl činiti každé přikázaní toto, kteréž já tobě dnes přikazuji.
Adzakudalitsani pokhapokha ngati mudzamveradi Yehova Mulungu wanu posunga ndi kutsatira malamulo onse amene ndikukupatsani lero.
6 Hospodin zajisté Bůh tvůj požehná tobě, jakož mluvil tobě, tak že budeš moci půjčovati národům mnohým, tobě pak nebude potřeba vypůjčovati; i budeš panovati nad národy mnohými, ale oni nad tebou nebudou panovati.
Pakuti Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani monga analonjeza, ndipo inu mudzabwereketsa chuma kwa mitundu yambiri ya anthu koma inu simudzabwereka kwa aliyense. Mudzalamulira mitundu yambiri ya anthu koma inuyo palibe amene adzakulamulireni.
7 Byl-li by u tebe nuzný někdo z bratří tvých, v některém městě tvém, v zemi tvé, kterouž Hospodin Bůh tvůj dá tobě, nezatvrdíš srdce svého, a nezavřeš ruky své před nuzným bratrem svým:
Ngati pali mʼbale wanu wina wosauka mu mzinda wanu wina uliwonse mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani, musawumitse mitima yanu kapena kuchita kaligwiritsa kwa mʼbale wanu wosaukayo.
8 Ale štědře otevřeš jemu ruku svou, a ochotně půjčíš jemu, jakž by mnoho potřeboval toho, v čemž by nouzi měl.
Koma mukhale ofewa manja ndipo mumukongoze mʼbale wanu momasuka pa chilichonse chimene akufuna.
9 Vystříhej se, aby nebylo něco nepravého v srdci tvém, a řekl bys: Blíží se rok sedmý, jenž jest rok odpuštění, a bylo by nešlechetné oko tvé k bratru tvému nuznému, tak že bys neudělil jemu, pročež by volal proti tobě k Hospodinu, a byl by na tobě hřích:
Musayesere ndi pangʼono pomwe kusunga maganizo oyipa awa mu mtima mwanu: “Chaka chachisanu ndi chiwiri, chaka chokhululukirana ngongole, chayandikira,” kuti musaonetse mtima woyipa kwa mʼbale wanu wosauka nʼkusamupatsa chilichonse. Iye angadzakunenereni inu mlandu kwa Ambuye, ndipo mudzapezeka wochimwa.
10 Ale ochotně dáš jemu, a nebude srdce tvé neupřímé, když bys dával jemu; nebo tou příčinou požehná tobě Hospodin Bůh tvůj ve všech skutcích tvých a ve všem díle, k kterémuž bys vztáhl ruku svou.
Mumupatse iye mowolowamanja ndipo muchite zimenezi mosasungira kanthu kumtima. Tsono chifukwa cha zimenezi, Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani pa ntchito zanu zonse ndi pa chilichonse chimene mukhudza.
11 Nebo nebudete bez chudých v zemi vaší; protož přikazuji tobě, řka: Abys ochotně otvíral ruku svou bratru svému, chudému svému a nuznému svému v zemi své.
Anthu osauka sadzatha mʼdziko lanu. Chomwecho ndikukulamulani kuti mukhale ofewa manja kwa abale anu ndi kwa osauka, osowa mʼdziko mwanu.
12 Jestliže by prodán byl tobě bratr tvůj Žid aneb Židovka, a sloužil by tobě za šest let, sedmého léta propustíš jej od sebe svobodného.
Ngati mʼbale wanu wamwamuna kapena wamkazi adzigulitsa yekha kwa inu, nakugwirirani ntchito zaka zisanu ndi chimodzi, muzimumasula mʼchaka cha chisanu ndi chiwiri.
13 A když jej propustíš svobodného od sebe, nepustíš ho prázdného.
Ndipo pamene mumumasula, musangomulola apite chimanjamanja.
14 Štědře darovati jej budeš dary z dobytka svého, z stodoly a z vinice své; v čemž požehnal tobě Hospodin Bůh tvůj, z toho dáš jemu.
Mumupatse mowolowamanja zochokera pa ziweto zanu, kopunthira tirigu ndi kopsinyira vinyo. Inu mumupatse iye monga Yehova Mulungu wanu wakudalitsirani.
15 A pamatuj, že jsi služebníkem byl v zemi Egyptské, a že tě vykoupil Hospodin Bůh tvůj, protož já to dnes tobě přikazuji.
Kumbukirani kuti munali akapolo mʼdziko la Igupto ndipo Yehova Mulungu wanu anakupulumutsani. Nʼchifukwa chake ndikukupatsani lamulo ili lero lino.
16 Pakliť by řekl: Nepůjdu od tebe, proto že by tě miloval i dům tvůj, a že mu dobře u tebe,
Koma ngati kapoloyo akuwuzani kuti, “Ine sindikufuna kumasulidwa,” chifukwa choti wakukondani inuyo pamodzi ndi banja lanu ndiponso kuti kwamukomera iyeyo kuti azikhalabe nanu,
17 Tedy vezma špici, probodneš ucho jeho na dveřích, a bude u tebe služebníkem na věky. Takž podobně i děvce své učiníš.
pamenepo muzitenga chobowolera chachitsulo ndi kubowola khutu lake pa chitseko, ndipo mukatero adzakhala kapolo wanu moyo wake wonse. Mdzakazi wanu muzimuchitanso chimodzimodzi.
18 Nechť není za těžké před očima tvýma, když bys ho svobodného propustil od sebe, nebo dvojnásob více, než ze mzdy nájemník, sloužil tobě šest let; i požehná tobě Hospodin ve všech věcech, kteréž činiti budeš.
Musaone ngati chopweteka kumasula wantchito wanu, chifukwa ntchito imene wayigwira pa zaka zisanu ndi chimodzi zimenezi ndi yopindula kawiri pa ntchito imene akanagwira waganyu chabe. Ndipo Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani pa chilichonse chimene mukuchita.
19 Všeho prvorozeného, což se narodí z skotů tvých neb z bravů tvých, samce posvětíš Hospodinu Bohu svému. Nebudeš dělati prvorozeným volkem svým, a nebudeš holiti prvorozených ovec svých.
Mumupatulire Yehova Mulungu wanu choyamba kubadwa chachimuna chilichonse pa ngʼombe ndi nkhosa zanu. Musamazigwiritse ntchito ngʼombe zoyamba kubadwa kapena kumeta nkhosa zoyamba kubadwa.
20 Před Hospodinem Bohem svým budeš je jísti na každý rok na místě, kteréž by vyvolil Hospodin, ty i čeled tvá.
Inuyo ndi banja lanu, chaka chilichonse muzizidya zimenezi pamaso pa Yehova Mulungu wanu pa malo amene Iye adzasankhe.
21 Pakliť by na něm byla vada, že by kulhavé aneb slepé bylo, aneb mělo by jakoukoli škodlivou vadu, nebudeš ho obětovati Hospodinu Bohu svému.
Ngati chiweto chili ndi chilema monga kulumala kapena chosaona, kapena ngati chili ndi cholakwika chachikulu chilichonse, musachipereke nsembe kwa Yehova Mulungu wanu.
22 V branách svých budeš je jísti, buďto čistý neb nečistý, rovně jako srnu aneb jelena;
Muzichidya mʼmizinda yanuyanu. Onse odetsedwa monga mwa mwambo ndi oyeretsedwa omwe akhoza kuchidya monga akudya gwape kapena mbawala.
23 Toliko krve jeho nebudeš jísti, ale na zem vycedíš ji jako vodu.
Koma musadye magazi ake. Muwathire pansi ngati madzi.