< 2 Královská 14 >
1 Léta druhého Joasa syna Joachaza, krále Izraelského, kraloval Amaziáš syn Joasa, krále Judského.
Mʼchaka chachiwiri cha Yehowasi mwana wa Yowahazi mfumu ya Israeli, Amaziya mwana wa Yowasi mfumu ya Yuda anayamba kulamulira.
2 V pětmecítma letech byl, když počal kralovati, a kraloval dvadceti devět let v Jeruzalémě. Jméno matky jeho Joadan z Jeruzaléma.
Iye anali ndi zaka 25 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 29. Amayi ake anali Yehoyadini wa ku Yerusalemu.
3 Ten činil to, což dobrého jest před očima Hospodinovýma, ačkoli ne tak jako David otec jeho. Všecko, což činil Joas otec jeho, tak činil.
Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova, koma osafanana ndi zomwe anachita Davide kholo lake. Iye anatsatira zochita zonse za Yowasi abambo ake.
4 A však výsostí nezkazili, ještě lid obětoval a kadil na výsostech.
Komabe sanachotse malo opembedzerapo mafano. Anthu anapitiriza kupereka nsembe ndi kufukiza lubani kumeneko.
5 I stalo se, když upevněno bylo království v ruce jeho, že pobil služebníky své, kteříž byli zabili krále otce jeho.
Atakhazikika mu ufumu wake, Amaziya anapha atumiki ake amene anapha abambo ake, mfumu ija.
6 Synů pak těch vražedlníků nepobil, jakož jest psáno v knize zákona Mojžíšova, kdež přikázal Hospodin, řka: Nebudouť na hrdle trestáni otcové za syny, aniž synové trestáni budou na hrdle za otce, ale jeden každý za svůj hřích umře.
Komatu iye sanaphe ana a anthu amene anapha abambo ake potsatira zomwe zinalembedwa mʼbuku la Malamulo a Mose. Mʼmenemo Yehova analamula kuti, “Makolo asaphedwe chifukwa cha ana awo, ndipo ana asaphedwe chifukwa cha makolo awo, koma aliyense ayenera kufa chifukwa cha zolakwa zake.”
7 On také porazil Idumejských v údolí solnatém deset tisíců, a dobyl Sela bojem. I nazval jméno jeho Jektehel až do tohoto dne.
Iye ndiye amene anapha Aedomu 10,000 mʼchigwa cha Mchere nalanda mzinda wa Sela pa nkhondo ndipo anawutcha Yokiteeli, dzina lake ndi lomwelo mpaka lero lino.
8 Tedy poslal Amaziáš posly k Joasovi synu Joachaza, syna Jéhu krále Izraelského, řka: Nuže, pohleďme sobě v oči.
Tsono Amaziya anatuma amithenga kwa Yehowasi mwana wa Yehowahazi, mwana wa Yehu mfumu ya Israeli ndi kumuopseza kuti, “Bwera tidzaonane maso ndi maso.”
9 Zase poslal Joas král Izraelský k Amaziášovi králi Judskému a řekl: Bodlák, kterýž byl na Libánu, poslal k cedru Libánskému, řka: Dej dceru svou synu mému za manželku. V tom šlo tudy zvíře polní, kteréž bylo na Libánu, a pošlapalo ten bodlák.
Koma Yehowasi mfumu ya Israeli anabweza mawu kwa Amaziya mfumu ya Yuda kuti, “Mtengo wa minga wa ku Lebanoni unatumiza uthenga kwa mkungudza wa ku Lebanoni. ‘Patse mwana wako wamkazi kuti ndimukwatire.’ Kenaka chirombo cha ku Lebanoni chinabwera ndi kupondaponda mtengo wa mingawo.
10 Že jsi mocně porazil Idumejské, protož pozdvihlo tě srdce tvé. Chlub se a seď v domě svém. I proč se máš plésti v neštěstí, abys padl ty i Juda s tebou?
Inde iwe wagonjetsa Edomu ndipo tsopano wayamba kudzikuza. Dzitamandire chifukwa cha kupambana kwako, koma khala kwanu konko! Nʼchifukwa chiyani ukuyamba dala mavuto amene adzakuwononga pamodzi ndi Yuda?”
11 Ale Amaziáš neuposlechl. Protož vytáhl Joas král Izraelský, a pohleděli sobě v oči, on s Amaziášem králem Judským u Betsemes Judova.
Koma Amaziya sanamvere zimenezi. Choncho Yehowasi mfumu ya Israeli anakamuthira nkhondo. Yehowasi ndi Amaziya anakumana maso ndi maso ku Beti-Semesi mʼdziko la Yuda.
12 I poražen jest Juda od Izraele, a utíkali jeden každý do příbytků svých.
Israeli anagonjetsa Yuda ndipo munthu aliyense anathawira kwawo.
13 Amaziáše pak krále Judského, syna Joasa syna Ochoziášova, jal Joas král Izraelský u Betsemes, a přitáh do Jeruzaléma, zbořil zed Jeruzalémskou, od brány Efraim až k bráně úhlu, na čtyři sta loktů.
Yehowasi mfumu ya Israeli anagwira Amaziya mfumu ya Yuda, mwana wa Yowasi, mwana wa Ahaziya ku Beti-Semesi. Ndipo anapita ku Yerusalemu nakagwetsa khoma la Yerusalemu kuyambira ku Chipata cha Efereimu mpaka ku Chipata Chapangodya, gawo lotalika mamita 180.
14 A pobral všecko zlato i stříbro, a všecky nádoby, kteréž se nalézaly v domě Hospodinově a v pokladích domu královského, také i mládence zastavené, a navrátil se do Samaří.
Iye anatenga golide ndi siliva yense pamodzi ndi ziwiya zonse zimene zinali mʼNyumba ya Yehova ndi zimene zinali mosungira chuma cha nyumba ya mfumu. Iye anagwiranso anthu nabwerera ku Samariya.
15 O jiných pak činech Joasa, kteréž činil, i síle jeho, a kterak bojoval proti Amaziášovi králi Judskému, psáno jest v knize o králích Izraelských.
Ntchito zina za Yehowasi ndi zonse zimene anachita, kuwonjezera za nkhondo yake ndi Amaziya mfumu ya Yuda, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
16 I usnul Joas s otci svými, a pochován jest v Samaří s králi Izraelskými, i kraloval Jeroboám syn jeho místo něho.
Yehowasi anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda mu Samariya pamodzi ndi mafumu a Israeli. Ndipo mwana wake Yeroboamu analowa ufumu mʼmalo mwake.
17 Živ pak byl Amaziáš syn Joasův, král Judský, po smrti Joasa syna Joachaza, krále Izraelského, patnácte let.
Amaziya mwana wa Yowasi mfumu ya Yuda anakhala zaka khumi ndi zisanu atamwalira Yehowasi mwana wa Yehowahazi mfumu ya Israeli.
18 O jiných pak věcech Amaziášových psáno jest v knize o králích Judských.
Ntchito zina za Amaziya, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
19 Potom spuntovali se proti němu v Jeruzalémě, a on utekl do Lachis. Protož poslali za ním do Lachis, a zamordovali ho tam.
Anthu anapangana zomuchita chiwembu mu Yerusalemu ndipo Amaziya anathawira ku Lakisi, koma anatumiza anthu ku Lakisiko nakamuphera komweko.
20 Odkudž odnesli jej na koních, a pochován jest v Jeruzalémě s otci svými v městě Davidově.
Anabwera naye ku pa kavalo ku Yerusalemu ndi kumuyika mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu Mzinda wa Davide.
21 Tedy všecken lid Judský vzali Azariáše, kterýž byl v šestnácti letech, a ustanovili ho za krále na místě otce jeho Amaziáše.
Ndipo anthu onse a ku Yuda anatenga Azariya, amene anali ndi zaka 16 namulonga ufumu mʼmalo mwa abambo ake Amaziya.
22 Onť jest vzdělal Elat a dobyl ho Judovi, když byl již usnul král s otci svými.
Azariya anamanga mzinda wa Elati ndi kuwubwezeretsa ku Yuda, Amaziya atamwalira.
23 Léta patnáctého Amaziáše syna Joasa, krále Judského, kraloval Jeroboám syn Joasa, krále Izraelského, v Samaří čtyřidceti a jedno léto.
Mʼchaka cha khumi ndi chisanu cha Amaziya mwana wa Yowasi mfumu ya Yuda, Yeroboamu mwana wa Yehowasi mfumu ya Israeli analowa ufumu ku Samariya ndipo analamulira za 41.
24 A činil to, což jest zlého před očima Hospodinovýma, neuchýliv se od žádných hříchů Jeroboáma syna Nebatova, kterýž k hřešení přivedl Izraele.
Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova ndipo sanasiye machimo a Yeroboamu mwana wa Nebati, amene anachimwitsa nawo Israeli.
25 On zase dobyl končin Izraelských od toho místa, kudy se jde do Emat, až k moři pustému, vedlé řeči Hospodina Boha Izraelského, kterouž byl mluvil skrze služebníka svého Jonáše syna Amaty proroka, kterýž byl z Gethefer.
Iye ndi amene anabwezeretsanso malire a Israeli kuyambira ku Lebo Hamati mpaka ku Nyanja ya Araba, molingana ndi zimene ananena Yehova Mulungu wa Israeli, kudzera mwa mtumiki wake Yona mwana wa Amitai, mneneri wochokera ku Gati-Heferi.
26 Nebo viděl Hospodin trápení Izraele těžké náramně, a že jakož zajatý, tak i zanechaný s nic býti nemůže, aniž jest, kdo by spomohl Izraelovi.
Pakuti Yehova anaona masautso a Israeli amene anali owawa kwambiri, panalibe kapolo kapena mfulu ngakhale wina aliyense amene akanathandiza Israeli.
27 A nemluvil Hospodin, že by chtěl zahladiti jméno Izraele, aby ho nebylo pod nebem; protož vysvobodil je skrze Jeroboáma syna Joasova.
Pakuti Yehova anali asananene zofafaniza ufumu wa Israeli pa dziko lapansi, Iye anawapulumutsa kudzera mʼdzanja la Yeroboamu mwana wa Yowasi.
28 O jiných pak věcech Jeroboámových, a cožkoli činil, i o síle jeho, a kterak bojoval, jak zase dobyl Damašku a Emat Judova Izraelovi, psáno jest v knize o králích Izraelských.
Ntchito zina za Yeroboamu ndi zonse zimene anachita, za kupambana kwake pa nkhondo, za mmene anagonjetsera Damasiko ndi Hamati, imene inali mizinda ya Yuda, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
29 I usnul Jeroboám s otci svými, s králi Izraelskými, a kraloval Zachariáš syn jeho místo něho.
Yeroboamu anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi mafumu a Israeli. Ndipo Zekariya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.