< 2 Kronická 35 >

1 Slavil také Joziáš v Jeruzalémě velikunoc Hospodinu, a zabili beránka velikonočního čtrnáctého dne měsíce prvního.
Yosiya anachita chikondwerero cha Paska wa Yehova mu Yerusalemu, ndipo mwana wankhosa wa Paska anaphedwa pa tsiku la khumi ndi chinayi la mwezi woyamba.
2 A postaviv kněží v strážech jejich, utvrdil je v přisluhování domu Hospodinova.
Iye anasankha ansembe pa maudindo awo ndipo anawalimbikitsa pa ntchito ya mʼnyumba ya Yehova.
3 I řekl Levítům, kteříž připravovali za všecken lid Izraelský věci svaté Hospodinu: Vneste truhlu svatosti do domu, kterýž ustavěl Šalomoun syn Davidův, král Izraelský. Nebudeť vám břemenem na ramenou. A tak nyní služte Hospodinu Bohu svému a lidu jeho Izraelskému.
Iye anati kwa Alevi amene amalangiza Aisraeli onse omwe anadzipatula kwa Yehova: Ikani bokosi lopatulika mʼNyumba ya Mulungu amene Solomoni mwana wa Davide mfumu ya Israeli anamanga. Lisamanyamulidwe pa mapewa anu. Tsopano tumikirani Yehova Mulungu wanu ndi anthu ake Aisraeli.
4 A připravte se po čeledech otců svých, po třídách svých, tak jakž nařídil David král Izraelský, a podlé nařízení Šalomouna syna jeho.
Mukhale mʼmagulu anu molingana ndi mabanja anu, molingana ndi momwe analembera Davide mfumu ya Israeli ndiponso mwana wake Solomoni.
5 A stůjte v svatyni podlé rozdílu čeledí otcovských, bratří národu svého, a podlé rozdělení každé čeledi otcovské Levítů.
“Muziyima ku malo opatulika pamodzi ndi gulu la Alevi oyimira gulu lililonse lalingʼono la mabanja a abale anu amene ndi anthu wamba.
6 A tak zabíte beránka, a posvěťte se, a připravte bratřím svým, chovajíce se vedlé slova Hospodinova vydaného skrze Mojžíše.
Muzipha ana ankhosa a Paska, muzidzipatula nokha ndi kuwakonzera abale anu ana ankhosa awo, kuchita zimene Yehova analamulira mwa Mose.”
7 Daroval pak Joziáš všemu množství z stáda beránků a kozelců, vše k obětem velikonočním, podlé toho všeho, jakž postačovalo, v počtu třidcet tisíců, a skotů tři tisíce, to vše z statku královského.
Yosiya anapereka kwa anthu wamba onse ana ankhosa ndi ana ambuzi okwanira 30,000 ndi ngʼombe zazimuna 3,000, zopereka za Paska zonse zochokera pa chuma chake cha mfumu.
8 Knížata jeho také k lidu, kněžím i Levítům štědře se ukázali: Helkiáš, Zachariáš a Jechiel, přední v domě Božím, dali kněžím k obětem velikonočním dva tisíce a šest set bravů a skotů tři sta.
Akuluakulu akenso anapereka mwaufulu kwa anthu ndi kwa ansembe ndi Alevi. Hilikiya, Zekariya ndi Yehieli oyangʼanira ntchito ya mʼNyumba ya Mulungu anapereka kwa ansembe zopereka za Paska 2,600 ndi ngʼombe 300.
9 Konaniáš pak s Semaiášem a Natanaelem bratřími svými, též Chasabiáš, Jehiel, Jozabad, přední z Levítů, darovali jiným Levítům k obětem velikonočním pět tisíc bravů a skotů pět set.
Konaniya nayenso pamodzi ndi Semaya ndi Netaneli, abale ake ndi Hasabiya, Yeiyeli ndi Yozabadi, atsogoleri a Alevi, anapereka nsembe za Paska 5,000 ndi ngʼombe 500 kwa Alevi.
10 A když připraveno bylo všecko k službě, stáli kněží na místě svém, a Levítové v třídách svých, podlé rozkazu královského.
Mwambo unakonzedwa ndipo ansembe anayima pamalo pawo pamodzi ndi Alevi mʼmagulu awo monga mfumu inalamulira.
11 I zabijeli beránky velikonoční, kněží pak kropili krví, berouce z rukou jejich, a Levítové vytahovali z koží.
Ana ankhosa a Paska anaphedwa ndipo ansembe anawaza magazi amene anaperekedwa kwa iwo pamene Alevi anali kusenda nyamazo.
12 Tedy oddělili zápal, aby dali lidu podlé rozdělení domů čeledí otcovských, tak aby obětováno bylo Hospodinu, jakž psáno jest v knize Mojžíšově. Tolikéž i s voly učinili.
Iwo anayika padera nsembe zopsereza kuti azipereke kwa magulu angʼonoangʼono a mabanja a anthu kuti apereke kwa Yehova monga zinalembedwa mʼbuku la Mose. Ndipo anachita chimodzimodzi ndi ngʼombe.
13 I pekli beránky velikonoční ohněm podlé obyčeje, ale jiné věci posvěcené vařili v hrncích, v kotlících a v pánvicích, a rozdávali rychle všemu lidu.
Anawotcha nyama za Paska monga momwe zinalembedwera ndi kuwiritsa zopereka zopatulika mʼmiphika, mʼmitsuko ndi mʼziwaya ndipo anazipereka mofulumira kwa anthu onse.
14 Potom pak připravili sobě a kněžím. Nebo kněží, synové Aronovi, zápaly a tuky až do noci obětovali, protož Levítové připravili sobě i kněžím, synům Aronovým.
Izi zitatha, anakonza zawo ndi za ansembe chifukwa ansembe, zidzukulu za Aaroni, anali otanganidwa kupereka nsembe zopsereza ndi mafuta a nyama mpaka madzulo. Choncho Alevi amakonza zawo ndi za ansembe, ana a Aaroni.
15 Též i zpěváci, synové Azafovi, stáli na místě svém podlé rozkázaní Davidova Azafovi, Hémanovi i Jedutunovi, proroku královskému, vydaného. Vrátní také při jedné každé bráně neměli odcházeti od své povinnosti, pročež bratří jejich Levítové jiní strojili jim.
Anthu oyimba nyimbo, zidzukulu za Asafu, anali pa malo awo potsata zomwe analemba Davide, Asafu, Hemani ndi Yedutuni mlosi wa mfumu. Alonda apazipata anali pa chipata chilichonse ndipo kunali kosafunika kuti achoke pa ntchito yawo, poti abale awo Alevi ankawakonzera zonse.
16 A tak nastrojena byla všecka služba Hospodinova v ten den, v slavení hodu beránka a obětování oběti zápalné na oltáři Hospodinovu, podlé rozkázaní krále Joziáše.
Kotero pa nthawi imeneyi ntchito yonse ya Yehova ya chikondwerero cha Paska ndi nsembe zopsereza pa guwa la Yehova inachitika monga analamulira mfumu Yosiya.
17 I slavili synové Izraelští, což se jich našlo, hod beránka v ten čas a slavnost přesnic za sedm dní.
Aisraeli amene analipo anachita chikondwerero cha Paska pa nthawi imeneyi ndi kuchita mwambo wa chikondwerero cha Buledi Wopanda Yisiti, kwa masiku asanu ndi awiri.
18 Nebyla pak slavena velikanoc té podobná v Izraeli ode dnů Samuele proroka, aniž který z králů Izraelských slavil hodu beránka podobného tomu, kterýž slavil Joziáš s kněžími a Levíty, i se vším lidem Judským a Izraelským, což se ho našlo, i s obyvateli Jeruzalémskými.
Paska yofanana ndi iyi sinachitikepo ku Israeli kuyambira nthawi ya Samueli ndipo palibe mmodzi mwa mafumu a Israeli anachitapo chikondwerero cha Paska ngati anachitira Yosiya pamodzi ndi ansembe, Alevi ndi Ayuda onse ndi Aisraeli amene anali pamodzi ndi anthu a mu Yerusalemu.
19 Osmnáctého léta kralování Joziášova slaven byl ten hod beránka.
Chikondwerero cha Paska ichi chinachitika mʼchaka cha 18 cha ulamuliro wa Yosiya.
20 Potom po všem, když již spravil Joziáš dům Boží, přitáhl Nécho král Egyptský, aby bojoval proti Charkemis podlé Eufraten, Joziáš pak vytáhl proti němu.
Zimenezi zitachitika, pamene Yosiya anakonzanso Nyumba ya Mulungu, Neko mfumu ya Igupto inapita kukachita nkhondo ku Karikemesi ku mtsinje wa Yufurate, ndipo Yosiya anapita kukamenyana naye.
21 Kterýž ač poslal k němu posly, řka: Já nic nemám s tebou činiti, králi Judský. Ne proti tobě, slyš ty, dnes táhnu, ale proti domu, kterýž se mnou bojuje, kamž mi rozkázal Bůh, abych pospíšil. Nebojuj s Bohem, kterýž se mnou jest, ať tě neshladí:
Koma Neko anatumiza amithenga kwa iye kunena kuti, “Kodi pali mkangano wanji pakati pa iwe ndi ine, iwe mfumu ya Yuda? Ine sindikuthira nkhondo iwe pa nthawi ino, koma nyumba imene ndili nayo pa nkhondo. Mulungu wandiwuza kuti ndifulumize choncho leka kutsutsana ndi Mulungu amene ali ndi ine, mwina adzakuwononga.”
22 Joziáš však neodvrátil tváři své od něho, ale aby bojoval s ním, změnil oděv svůj, aniž uposlechl slov Néchových, pošlých z úst Božích. A tak přitáhl, aby se s ním potýkal na poli Mageddo.
Komabe Yosiya sanatembenuke kumusiya iyeyo, koma anadzizimbayitsa ndi kukalowa mʼnkhondo. Iye sanamvere zimene Neko ananena molamulidwa ndi Mulungu koma anapita kukamenyana naye ku chigwa ku Megido.
23 I postřelili střelci krále Joziáše. Tedy řekl král služebníkům svým: Odvezte mne, neboť jsem velmi nemocen.
Anthu oponya mivi analasa mfumu Yosiya, ndipo iye anawuza akuluakulu ake, “Chotseni. Ndavulazidwa kwambiri.”
24 Takž přenesli jej služebníci jeho z toho vozu, a vložili ho na druhý vůz, kterýž měl, a dovezli jej do Jeruzaléma. I umřel a pochován jest v hrobích otců svých. I plakal všecken Juda a Jeruzalém nad Joziášem.
Choncho anamuchotsa iye mʼgaleta lake, ndipo anamuyika mʼgaleta lina limene anali nalo ndipo anabwera naye ku Yerusalemu kumene anamwalirira. Iye anayikidwa mʼmanda a makolo ake. Ndipo Ayuda ndi Yerusalemu yense anamulira.
25 Naříkal také i Jeremiáš nad Joziášem, a zpívávali všickni zpěváci a zpěvakyně v naříkáních svých o Joziášovi až do dnešního dne, kteráž uvedli v obyčej Izraeli. A ta jsou zapsána v pláči Jeremiášovu.
Yeremiya anapeka nyimbo za maliro chifukwa cha Yosiya, ndipo mpaka lero lino amuna ndi akazi onse oyimba amakumbukira Yosiya pa nyimbo zawo za maliro. Izi zinakhala mwambo mu Israeli ndipo zinalembedwa mʼNyimbo za Maliro.
26 Jiné pak věci Joziášovy, i pobožnost jeho, jakž napsáno jest v zákoně Hospodinově,
Zochitika zina za ulamuliro wa Yosiya ndi ntchito za kudzipereka kwake, monga zinalembedwa mʼMalamulo a Yehova,
27 I skutkové jeho první i poslední, to vše zapsáno jest v knize o králích Izraelských a Judských.
zochitika zonse, kuyambira pachiyambi mpaka pa mapeto, zalembedwa mʼbuku la mafumu a Israeli ndi Yuda.

< 2 Kronická 35 >