< 2 Kronická 17 >

1 I kraloval Jozafat syn jeho místo něho, a zmocnil se Izraele.
Yehosafati mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake ndipo anadzilimbitsa pofuna kulimbana ndi Israeli.
2 I osadil lidem válečným všecka města hrazená v Judstvu, a postavil stráž v zemi Judské a v městech Efraim, kteráž byl zdobýval Aza otec jeho.
Iye anayika magulu a asilikali mʼmizinda yonse yotetezedwa ya Yuda, ndipo anamanga maboma mu Yuda ndi mʼmizinda yonse ya Efereimu imene Asa abambo ake analanda.
3 A byl Hospodin s Jozafatem; nebo chodil po cestách Davida otce svého prvních, aniž hledal modl.
Yehova anali ndi Yehosafati chifukwa mʼzaka zoyambirira anatsatira makhalidwe a Davide abambo ake. Iye sanafunsire kwa Abaala.
4 Ale Boha otce svého hledal, a v přikázaních jeho chodil, aniž následoval skutků lidu Izraelského.
Koma anafunafuna Mulungu wa abambo ake ndipo anatsatira malamulo ake osati zochita za Israeli.
5 I utvrdil Hospodin království v ruce jeho, a dal všecken lid Judský dary Jozafatovi, tak že měl bohatství a slávy hojně.
Yehova anakhazikitsa kolimba ufumuwo mʼmanja mwake ndipo Ayuda onse anabweretsa mphatso kwa Yehosafati, kotero kuti anali ndi chuma ndi ulemu wambiri.
6 A nabyv udatného srdce k cestám Hospodinovým, zkazil přesto také i výsosti a háje v Judstvu.
Mtima wake anawupereka kutsatira Yehova, kuwonjezera apo, anachotsa malo onse achipembedzo ndi mafano a Asera mu Yuda.
7 Léta pak třetího království svého poslal knížata svá: Benchaile, Abdiáše, Zachariáše, Natanaele a Micheáše, aby učili v městech Judských.
Mʼchaka chachitatu cha ufumu wake, iye anatuma akuluakulu ake Beni-Haili, Obadiya, Zekariya, Netaneli ndi Mikaya kukaphunzitsa mʼmizinda ya Yuda.
8 A s nimi Levíty: Semaiáše, Netaniáše, Zebadiáše, Azaele, Semiramota, Jonatana, Adoniáše, Tobiáše a Tobadoniáše, Levíty, a s nimi Elisama a Jehorama, kněží,
Pamodzi ndi iwo panali Alevi ena: Semaya, Netaniya, Zebadiya, Asaheli, Semiramoti, Yonatani, Adoniya, Tobiya ndi Tobu-Adoniya ndiponso ansembe Elisama ndi Yehoramu.
9 Kteříž učili v Judstvu, majíce s sebou knihu zákona Hospodinova. Chodili pak vůkol po všech městech Judských, vyučujíce lid.
Iwo anaphunzitsa mu Yuda monse atatenga Buku la Malamulo a Yehova iwo anayenda mʼmizinda yonse ya ku Yuda ndipo anaphunzitsa anthu.
10 I byl strach Hospodinův na všech královstvích zemí, kteréž byly vůkol Judstva, tak že nebojovali proti Jozafatovi.
Kuopsa kwa Yehova kunali pa maufumu onse a mayiko oyandikana ndi Yuda, kotero kuti sanachite nkhondo ndi Yehosafati.
11 Nýbrž i Filistinští přinášeli Jozafatovi dary a berni uloženou. Arabští také přiháněli jemu dobytky, skopců po sedmi tisících a sedmi stech, též kozlů po sedmi tisících a sedmi stech.
Afilisti ena anabweretsa kwa Yehosafati mphatso ndi siliva ngati msonkho, ndipo Aarabu anabweretsa ziweto: nkhosa zazimuna 7,700 ndi mbuzi 7,700.
12 I prospíval Jozafat, a rostl až na nejvyšší, a vystavěl v Judstvu zámky a města k skladům.
Mphamvu za Yehosafati zinkakulirakulira. Iye anamanga malo otetezedwa ndi mizinda yosungiramo chuma mu Yuda
13 A práci mnohou vedl při městech Judských, muže pak válečné a slovoutné měl v Jeruzalémě.
ndipo anali ndi katundu wambiri mʼmizinda ya Yuda. Iye anayikanso asilikali odziwa bwino nkhondo mu Yerusalemu.
14 A tento jest počet jich po domích otců jejich: Z Judy knížata nad tisíci: Adna kníže, a s ním udatných rytířů třikrát sto tisíc.
Chiwerengero chawo potsata mabanja awo chinali chotere: kuchokera ku Yuda, atsogoleri a magulu 1,000; mtsogoleri Adina, anali ndi anthu 300,000 odziwa nkhondo;
15 A po něm Jochanan kníže, a s ním dvě stě a osmdesát tisíc.
otsatana naye, mtsogoleri Yehohanani, anali ndi anthu 280,000;
16 Po něm Amaziáš syn Zichrův, kterýž se dobrovolně byl oddal Hospodinu, a při něm dvakrát sto tisíc mužů udatných.
otsatana naye, Amasiya mwana wa Zikiri amene anadzipereka yekha kutumikira Yehova, anali ndi anthu 200,000.
17 Z Beniamina pak muž udatný Eliada, a s ním lidu zbrojného s lučišti a pavézami dvakrát sto tisíc.
Kuchokera ku Benjamini: Eliada, msilikali wolimba mtima, anali ndi anthu 200,000 amene anali ndi mauta ndi zishango;
18 A po něm Jozabad, a s ním sto a osmdesát tisíc způsobných k boji.
otsatana naye, Yehozabadi, anali ndi anthu 180,000 okonzekera nkhondo.
19 Ti sloužili králi, kromě těch, kteréž byl osadil král po městech hrazených po všem Judstvu.
Awa ndi anthu amene ankatumikira mfumu osawerengera amene anawayika mʼmizinda yotetezedwa mʼdziko lonse la Yuda.

< 2 Kronická 17 >