< 2 Kronická 16 >

1 Léta třidcátého šestého kralování Azova vytáhl Báza král Izraelský proti Judovi, a stavěl Ráma, aby nedal vyjíti ani jíti k Azovi králi Judskému.
Mʼchaka cha 36 cha ufumu wa Asa, Baasa mfumu ya Israeli inapita kukathira nkhondo dziko la Yuda. Anamangira mpanda mzinda wa Rama kuletsa aliyense kutuluka kapena kulowa mʼdziko la Asa mfumu ya Yuda.
2 Tedy vzav Aza stříbro i zlato z pokladů domu Hospodinova i domu královského, poslal k Benadadovi králi Syrskému, kterýž bydlil v Damašku, řka:
Ndipo Asa anatenga siliva ndi golide ku malo osungirako a mʼNyumba ya Mulungu ndi ku nyumba yake yaufumu ndi kuzitumiza kwa Beni-Hadadi mfumu ya Aramu imene inkakhala mu Damasiko.
3 Smlouva jest mezi mnou a mezi tebou, mezi otcem mým a mezi otcem tvým. Aj, posílámť teď stříbro a zlato, jdi, zruš smlouvu svou s Bázou králem Izraelským, ať odtrhne ode mne.
Iye anati, “Pakhale pangano pakati pa inu ndi ine, monga zinalili pakati pa abambo anu ndi abambo anga. Taonani, ine ndikutumiza kwa inu siliva ndi golide. Tsopano thetsani mgwirizano wanu ndi Baasa mfumu ya Israeli kuti achoke kwa ine.”
4 I uposlechl Benadad krále Azy, a poslal knížata s vojsky svými proti městům Izraelským. I dobyli Jon a Dan, též Abelmaim i všech měst Neftalímových, v nichž měli sklady.
Beni-Hadadi anagwirizana ndi mfumu Asa ndipo anatumiza olamulira nkhondo ake kukathira nkhondo mizinda ya Israeli. Iwo anagonjetsa Iyoni, Dani, Abeli-Maimu ndi mizinda yonse yosungira chuma ya Nafutali.
5 To když uslyšel Báza, přestal stavěti Ráma, a zanechal díla svého.
Baasa atamva izi, anasiya kumanga Rama ndipo anayimitsa ntchito yakeyo.
6 V tom Aza král pojal všecken lid Judský, a pobrali kamení z Ráma i dříví, z něhož stavěl Báza, a vystavěl z něho Gabaa a Masfa.
Ndipo mfumu Asa anabwera ndi Ayuda onse, ndipo anachotsa miyala ndi matabwa ku Rama amene Baasa amagwiritsa ntchito. Ndi zimenezi Asa ankamangira Geba ndi Mizipa.
7 V ten pak čas přišel Chanani prorok k Azovi králi Judskému, a řekl jemu: Že jsi zpolehl na krále Syrského, a nezpolehl jsi na Hospodina Boha svého, proto ušlo vojsko krále Syrského z ruky tvé.
Nthawi imeneyi mlosi Hanani anabwera kwa Asa mfumu ya Yuda ndipo anati kwa iye, “Chifukwa chakuti munadalira mfumu ya Aramu osati Yehova Mulungu wanu, gulu la ankhondo la mfumu ya ku Aramu lapulumuka mʼmanja mwanu.
8 Zdaliž jsou Chussimští a Lubimští neměli vojsk velmi velikých, s vozy a jezdci náramně mnohými? A když jsi zpolehl na Hospodina, vydal je v ruku tvou.
Kodi Akusi ndi Alibiya sanali gulu lankhondo lamphamvu lokhala ndi magaleta ochuluka ndi okwera magaleta ake? Koma pamene inu munadalira Yehova, Iye anawapereka mʼdzanja lanu.
9 Oči zajisté Hospodinovy spatřují všecku zemi, aby dokazoval síly své při těch, kteříž jsou k němu srdce upřímého. Bláznivě jsi učinil v té věci, protož od toho času budou proti tobě války.
Pakuti Yehova amayangʼana uku ndi uku pa dziko lonse lapansi kuti alimbikitse iwo amene mitima yawo ayipereka kwathunthu kwa Iye. Inu mwachita chinthu chopusa ndipo kuyambira lero mudzakhala pa nkhondo.”
10 Tedy rozhněvav se Aza na proroka, dal ho do vězení; nebo se byl rozhněval na něj pro tu věc. A utiskal Aza některé z lidu toho času.
Asa anamupsera mtima mlosi uja chifukwa cha izi mwakuti anakwiya kwambiri namuyika mʼndende. Pa nthawi yomweyonso Asa anazunza mwankhanza anthu ena.
11 O jiných pak věcech Azových, prvních i posledních, zapsáno jest v knize o králích Judských a Izraelských.
Ntchito zina za mfumu Asa, kuyambira pachiyambi mpaka kumapeto zalembedwa mʼbuku la mafumu a Yuda ndi Israeli.
12 Potom léta třidcátého devátého kralování svého nemocen byl Aza na nohy své těžkou nemocí, a však v nemoci své nehledal Boha, ale lékařů.
Mʼchaka cha 39 cha ufumu wake, Asa anayamba kudwala nthenda ya mapazi. Ngakhale nthendayo inali yaululu kwambiri, komabe iye sanafunefune Yehova, koma anafuna thandizo kwa asingʼanga.
13 A tak usnul Aza s otci svými, a umřel léta čtyřidcátého prvního kralování svého.
Ndipo mʼchaka cha 41 cha ufumu wake, Asa anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake.
14 A pochovali jej v hrobě jeho, kterýž byl vytesal sobě v městě Davidově, a položili ho na lůžku, kteréž byl naplnil vonnými věcmi a mastmi dílem apatykářským připravenými. I pálili to jemu ohněm velmi velikým.
Iye anayikidwa mʼmanda amene anadzisemera yekha mu Mzinda wa Davide. Anagoneka mtembo wake pa chithatha chimene anayikapo zonunkhira zamitundumitundu, ndipo anasonkha chimoto chachikulu pomuchitira ulemu.

< 2 Kronická 16 >