< 1 Janův 5 >
1 Každý, kdož věří, že Ježíš jest Kristus, z Boha se narodil; a každý, kdož miluje toho, kterýž zplodil, milujeť i toho, kterýž zplozen jest z něho.
Aliyense amene amakhulupirira kuti Yesu ndi Khristu, iyeyo ndi mwana wa Mulungu, ndipo aliyense amene amakonda Atate amakondanso Mwana wake.
2 Po tomť poznáváme, že milujeme syny Boží, když Boha milujeme, a přikázaní jeho ostříháme.
Chodziwira kuti timakonda ana a Mulungu nʼchakuti timakonda Mulungu ndi kusunga malamulo ake.
3 Nebo toť je láska Boží, abychom přikázaní jeho ostříhali; a přikázaní jeho nejsou těžká.
Pakuti kukonda Mulungu ndiye kusunga malamulo ake. Ndipo malamulo ake siwolemetsa,
4 Všecko zajisté, což se narodilo z Boha, přemáhá svět; a toť jest to vítězství, kteréž přemáhá svět, víra naše.
chifukwa aliyense amene ndi mwana wa Mulungu amagonjetsa dziko lapansi. Chikhulupiriro chathu ndicho timagonjetsera dziko lapansi.
5 Kdo jest, ješto přemáhá svět, jediné, kdož věří, že Ježíš jest Syn Boží?
Ndani amagonjetsa dziko lapansi? Yekhayo amene amakhulupirira kuti Yesu ndi Mwana wa Mulungu.
6 Toť jest ten, kterýž přišel skrze vodu a krev, Ježíš Kristus, ne u vodě toliko, ale u vodě a ve krvi. A Duch jest, kterýž svědectví vydává, že Duch jest pravda.
Uyu ndiye anabwera mwa madzi ndi magazi, ndiye Yesu Khristu. Sanabwere mwa madzi okha, koma mwa madzi ndi magazi. Ndipo ndi Mzimu Woyera amene akuchitira umboni, chifukwa Mzimu Woyera ndi choonadi.
7 Nebo tři jsou, kteříž svědectví vydávají na nebi: Otec, Slovo, a Duch svatý, a ti tři jedno jsou.
Pakuti pali atatu amene amachitira umboni.
8 A tři jsou, kteříž svědectví vydávají na zemi: Duch, a voda, a krev, a ti tři jedno jsou.
Mzimu Woyera, madzi ndi magazi; ndipo atatu amavomerezana.
9 Poněvadž svědectví lidské přijímáme, svědectvíť Boží větší jest. Nebo totoť svědectví jest Boží, kteréž vysvědčil o Synu svém.
Timalandira umboni wa anthu, koma umboni wa Mulungu ndi wopambana. Umboniwo ndi umene anachitira Mwana wake.
10 Kdož věří v Syna Božího, máť svědectví sám v sobě. Kdož nevěří Bohu, lhářem jej učinil; nebo neuvěřil tomu svědectví, kteréž vysvědčil Bůh o Synu svém.
Aliyense amene amakhulupirira Mwana wa Mulungu ali nawo umboniwu mu mtima mwake, koma aliyense amene sanakhulupirire Mulungu amayesa kuti Mulunguyo ndi wonama, chifukwa sanakhulupirire umboni umene Mulungu anachitira wa Mwana wake.
11 A totoť jest svědectví to, že život věčný dal nám Bůh, a ten život v Synu jeho jest. (aiōnios )
Ndipo umboniwo ndi uwu: Mulungu anatipatsa moyo wosatha, ndipo moyowu uli mwa Mwana wake. (aiōnios )
12 Kdožť má Syna, máť život; kdož nemá Syna Božího, života nemá.
Iye amene ali ndi Mwana ali ndi moyo, amene alibe Mwana wa Mulungu alibe moyo.
13 Tyto věci psal jsem vám věřícím ve jménu Syna Božího, abyste věděli, že máte věčný život, a abyste věřili ve jméno Syna Božího. (aiōnios )
Ine ndikulemba zimenezi kwa inu, amene mwakhulupirira dzina la Mwana wa Mulungu kuti mudziwe kuti muli ndi moyo wosatha. (aiōnios )
14 A totoť jest to smělé doufání, kteréž máme k němu, že zač bychom koli prosili podlé vůle jeho, slyší nás.
Ife timalimba mtima tikamafika pamaso pa Mulungu, popeza kuti ngati tipempha kanthu kalikonse monga mwa chifuniro chake, amatimvera.
15 Že pak víme, že nás slyší, prosili-li bychom zač, podlé toho víme, že máme prosby naplněné, kteréž jsme předkládali jemu.
Ndipo ngati tikudziwa kuti amatimvera, chilichonse chimene timapempha, tikudziwanso kuti tili nacho chimene tamupempha Iye.
16 Viděl-li by kdo bratra svého hřešícího hříchem ne k smrti, modliž se za něj, a dá jemu Bůh život, totiž hřešícím ne k smrti. Jestiť hřích k smrti; ne za ten, pravím, aby se modlil.
Ngati wina aona mʼbale wake akuchita tchimo losadzetsa imfa, apemphere ndipo Mulungu adzamupatsa moyo mʼbale wakeyo. Ndikunena za ochita tchimo losadzetsa imfa. Pali tchimo lodzetsa imfa. Ine sindikunena kuti apemphere ayi.
17 Každá nepravost jestiť hřích, ale jestiť hřích ne k smrti.
Chilichonse chosalungama ndi tchimo ndipo pali tchimo losadzetsa imfa.
18 Víme, že každý, kdož se narodil z Boha, nehřeší; ale ten, kdož narozen jest z Boha, ostříhá sebe samého, a ten zlostník se ho nedotýká.
Tikudziwa kuti aliyense amene ndi mwana wa Mulungu sachimwirachimwirabe. Yesu, Mwana wa Mulungu, amamusunga ndipo woyipa uja sangamukhudze.
19 Víme, že z Boha jsme, ale svět všecken ve zlém leží.
Tikudziwa kuti ndife ana a Mulungu ndi kuti dziko lonse lapansi lili pansi pa ulamuliro wa woyipayo.
20 A vímeť, že Syn Boží přišel a dal nám smysl, abychom poznali toho pravého, a jsmeť v tom pravém, i v Synu jeho Ježíši Kristu. Onť jest ten pravý Bůh a život věčný. (aiōnios )
Tikudziwa kuti Mwana wa Mulungu anafika ndipo anatipatsa nzeru, kuti timudziwe Iye amene ali woona. Ndipo ife tili mwa Iye amene ndi woona, Mwana wake, Yesu Khristu. Iye ndi Mulungu woona ndi moyo wosatha. (aiōnios )
21 Synáčkové, vystříhejte se modl. Amen.
Ana okondedwa, dzisungeni bwino, osapembedza mafano.