< Psalmi 81 >

1 Zborovođi. Po napjevu “Tijesci”. Asafov. Kliknite Bogu, našoj jakosti, kličite Bogu Jakovljevu!
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a gititi. Salimo la Asafu. Imbani mwachimwemwe kwa Mulungu mphamvu yathu; Fuwulani mokweza kwa Mulungu wa Yakobo!
2 Nek' zazvuče žice, nek' se čuje bubanj, svirajte u milozvučnu harfu s citarom!
Yambani nyimbo, imbani tambolini imbani pangwe wolira bwino ndi zeze.
3 Zatrubite u rog za mlađaka, za uštapa, na svetkovinu našu!
Imbani lipenga la nyanga ya nkhosa yayimuna pa mwezi watsopano, ndi pamene mwezi waoneka wonse, pa tsiku la phwando;
4 Jer to je propis Izraelu, zapovijed Boga Jakovljeva.
ili ndi lamulo kwa Israeli, langizo la Mulungu wa Yakobo.
5 Takav je zakon dao Josipu kad je izlazio iz zemlje Egipta.
Iye anapereka lamulolo kwa zidzukulu za Yosefe pamene anatuluka kulimbana ndi Igupto, kumene tinamva chiyankhulo chimene sitinachidziwe.
6 Šapat tajnovit čuh: “Oslobodih od tereta rame njegovo, ruke su mu slobodne od košare.
Iye akunena kuti, “Ine ndinachotsa zolemetsa pa mapewa awo; Manja awo anamasulidwa mʼdengu.
7 U tjeskobi si zavapio i ja te izbavih; iz gromovna oblaka odgovorih tebi, iskušah te kod voda meripskih.
Pa mavuto anu munayitana ndipo ndinakulanditsani, ndinakuyankhani kuchokera mʼmitambo ya mabingu; ndinakuyesani pa madzi a ku Meriba. (Sela)
8 Slušaj, puče moj, i ja ću te opomenuti: o, da me poslušaš, Izraele!
“Imvani anthu anga, ndipo ndidzakuchenjezani ngati mungathe kumvetsera, Inu Israeli!
9 Nek' ne bude u tebe drugog boga i ne klanjaj se bogu tuđem!
Musadzakhale ndi mulungu wachilendo pakati panu; musadzagwadire mulungu wina.
10 Ja sam Jahve, Bog tvoj koji te izvedoh iz Egipta: otvori svoja usta da ih napunim!”
Ine ndine Yehova Mulungu wanu, amene ndinakutulutsani mʼdziko la Igupto. Yasamani kukamwa kwanu ndipo ndidzakudyetsani.
11 “Ali moj narod ne slušaše glasa moga, Izrael me ne posluša.
“Koma anthu anga sanandimvere; Israeli sanandigonjere.
12 Zato ga pustih okorjelom srcu njegovu: neka hodi kako mu se hoće!
Kotero ndinawasiya ndi mitima yawo yosamverayo kuti atsate zimene ankafuna.
13 O, kad bi me narod moj slušao, kad bi Izrael putovima mojim hodio,
“Anthu anga akanangondimvera, Israeli akanatsatira njira zanga,
14 brzo bih pokorio dušmane njegove, ruku bih svoju okrenuo na protivnike njegove.
nʼkanafulumira motani kuti ndigonjetse adani awo ndi kutembenuza mkono wanga kulimbana ndi amaliwongo!
15 Oni što ga sada mrze dodvarali bi mu se i njihov bi udes bio zapečaćen zauvijek.
Iwo amene amadana ndi Yehova akanakhwinyata pamaso pake, ndipo chilango chawo chinakakhala mpaka kalekale.
16 A svoj narod hranio bih pšenicom najboljom i sitio ga medom iz pećine.
Koma inu mukanadyetsedwa tirigu wabwino kwambiri; ndikanakukhutitsani ndi uchi wochokera pa thanthwe.”

< Psalmi 81 >