< Psalmi 60 >
1 Zborovođi. Po napjevu “Ljiljan svjedočanstva”. Miktam. Davidov. Kad je David izišao protiv Aram Naharajima i protiv Aram Sobe i kad je Joab na povratku potukao dvanaest tisuća Edomaca Bože, ti nas ÓodbÄaci i bojne nam redove prÓobi, razjari se, a sad nas opet vrati!
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Kakombo wa Pangano.” Mikitamu ya Davide yophunzitsira. Pamene anamenyana ndi Mesopotamiya ndi Aramu-Zoba, ndi pamene Yowabu anabwerera ndi kukantha Aedomu 12,000 mʼChigwa cha Mchere. Inu Mulungu mwatikanatu ife, ndipo mwatiwonongera otiteteza. Inu mwatikwiyira, tsopano tibwezeretseni mwakale!
2 Potrese zemlju, rasječe je, zatvori joj usjeline jer se poljuljala.
Inu mwagwedeza dziko ndipo mwalingʼamba, konzani mingʼalu yake pakuti ikugwedezeka kwambiri.
3 Zlu si kob na svoj narod navalio, napio nas vinom omamnim.
Inu mwaonetsa anthu anu nthawi za mavuto; inu mwatipatsa vinyo amene watichititsa kudzandira.
4 Al' si i stijeg dao vjernicima svojim da umaknu luku dušmanskom.
Koma kwa iwo amene amaopa Inu, Inu mwakweza mbendera kuti tisonkhanireko pothawa uta.
5 Da ti se ljubimci izbave, desnicom pomozi, usliši nas!
Tipulumutseni ndi kutithandiza ndi dzanja lanu lamanja, kuti iwo amene mumawakonda apulumutsidwe.
6 Bog reče u svom Svetištu: “Šekem ću razdijelit' kličući, dolinu Sukot izmjeriti.
Mulungu wayankhula kuchokera ku malo ake opatulika: “Mwakupambana ndidzagawa Sekemu ndipo ndidzayeza malire a chigwa cha Sukoti.
7 Moj je Gilead, moj Manaše, Efrajim mi kaciga, Judeja žezlo moje!
Giliyadi ndi wanga, Manase ndi wanganso; Efereimu ndi chipewa changa chodzitetezera, Yuda ndi ndodo yanga yaufumu
8 Moab je sud iz kojeg se umivam, na Edom ću baciti obuću, nad Filistejcem slavit' pobjedu!”
Mowabu ndi mbale yanga yosambira, pa Edomu ndidzaponyapo nsapato yanga, pa Filisitiya ndidzafuwula mwakupambana.”
9 Tko će me dovesti do utvrđena grada, tko će me dovesti do Edoma?
Adzandifikitse ndani ku mzinda wotetezedwa? Ndani adzanditsogolera ku Edomu?
10 Zar nećeš ti, o Bože, što nas odbaci? Zar više nećeš, Bože, s četama našim?
Kodi si Inu Mulungu, Inu amene mwatikana ife ndipo simutuluka pamodzi ndi magulu athu ankhondo.
11 Pomozi nam protiv dušmana, jer ljudska je pomoć ništavna!
Tipatseni chithandizo kuti tilimbane ndi mdani wathu, pakuti thandizo lochokera kwa munthu ndi lopanda phindu.
12 S pomoću Božjom hrabro ćemo se boriti, a on će zgaziti naše dušmane.
Chifukwa cha Mulungu, ife tidzapeza chipambano ndipo tidzapondaponda adani athu.