< Psalmi 49 >
1 Zborovođi. Sinova Korahovih. Psalam. Poslušajte ovo, svi narodi, čujte, svi stanovnici zemlje,
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora. Imvani izi anthu a mitundu yonse; mvetserani, nonse amene mumakhala pa dziko lonse,
2 vi, djeco puka, i vi, odličnici, bogati i siromašni zajedno!
anthu wamba pamodzi ndi anthu odziwika, olemera pamodzinso ndi osauka:
3 Moja će usta zboriti mudrost, i moje srce misli razumne.
Pakamwa panga padzayankhula mawu anzeru; mawu ochokera mu mtima mwanga adzapereka nzeru.
4 K poučnoj izreci priklonit ću uho, uz harfu ću izložit' svoju zagonetku.
Ndidzatchera khutu langa ku mwambo, ndi pangwe ndidzafotokoza momveka mwambi wanga.
5 Što da se bojim u danima nesreće kad me opkoli zloba izdajica
Ine ndichitirenji mantha pamene masiku oyipa afika, pamene achinyengo oyipa andizungulira.
6 koji se u blago svoje uzdaju i silnim se hvale bogatstvom?
Iwo amene adalira kulemera kwawo ndi kutamandira kuchuluka kwa chuma chawo?
7 TÓa nitko sebe ne može otkupit' ni za se dati Bogu otkupninu:
Palibe munthu amene angawombole moyo wa mnzake kapena kuperekera mnzake dipo kwa Mulungu.
8 životu je cijena previsoka, i nikada je neće platiti
Dipo la moyo ndi la mtengowapatali, palibe malipiro amene angakwanire,
9 tko želi živjeti dovijeka i ne vidjeti jamu grobnu.
kuti iye akhale ndi moyo mpaka muyaya ndi kusapita ku manda.
10 Jer, i mudri umiru, pogiba i luđak i bezumnik: bogatstvo svoje ostavlja drugima.
Pakuti onse amaona kuti anthu anzeru amamwalira; opusa ndi opanda nzeru chimodzimodzinso amawonongeka ndipo amasiyira chuma chawo anthu ena.
11 Grobovi im kuće zasvagda, stanovi njihovi od koljena do koljena, sve ako se zemlje nazivale imenima njihovim.
Manda awo adzakhala nyumba zawo mpaka muyaya, malo awo okhalako kwa nthawi yonse ya mibado yawo, ngakhale anatchula malo mayina awo.
12 Čovjek koji nerazumno živi sličan je stoci koja ugiba.
Ngakhale munthu akhale wachuma chotani, adzafa ngati nyama.
13 Takav je put onih koji se ludo uzdaju, to je konac onih koji uživaju u sreći:
Izi ndi zimene zimachitikira iwo amene amadzidalira okha, ndi owatsatira awo amene amavomereza zimene amayankhula. (Sela)
14 Poput stada redaju se u Podzemlju, smrt im je pastir, a dobri njima vladaju. Njihova će lika brzo nestati, Podzemlje će im biti postojbina. (Sheol )
Monga nkhosa iwo ayenera kupita ku manda, ndipo imfa idzawadya. Olungama adzawalamulira mmawa; matupi awo adzavunda mʼmanda, kutali ndi nyumba zawo zaufumu. (Sheol )
15 A moju će dušu Bog ugrabiti Podzemlju iz pandža i milostivo me primiti. (Sheol )
Koma Mulungu adzawombola moyo wanga kuchoka ku manda; ndithu Iye adzanditengera kwa Iye mwini. (Sheol )
16 Ne boj se ako se tko obogati i ako se poveća blago doma njegova:
Usavutike mu mtima pamene munthu akulemera, pamene ulemerero wa nyumba yake ukuchulukirachulukira;
17 kad umre, ništa neće ponijeti sa sobom, i blago njegovo neće s njime sići.
Pakuti sadzatenga kanthu pamodzi naye pamene wamwalira, ulemerero wake sudzapita pamodzi naye.
18 Ako se u životu držao sretnim - “Govorit će se da ti je dobro bilo!” -
Ngakhale pamene munthuyo ali moyo amadziyesa wodala, ndipo ngakhale atamandidwe pamene zinthu zikumuyendera bwino,
19 i on će doći u skup otaca svojih, gdje svjetlosti više vidjeti neće.
iyeyo adzakakhala pamodzi ndi mʼbado wa makolo ake, amene sadzaonanso kuwala.
20 Čovjek koji nerazumno živi sličan je stoci koja ugiba.
Munthu amene ali ndi chuma koma wopanda nzeru adzafa ngati nyama yakuthengo.