< Psalmi 43 >
1 Dosudi mi pravo, Bože, i povedi parbu moju protiv čeljadi bezbožne, izbavi me od čovjeka zlobna i opaka!
Onetsani kusalakwa kwanga Inu Mulungu; ndipo mundinenere mlandu wanga kutsutsana ndi mtundu wosapembedza; mundilanditse mʼmanja mwa achinyengo ndi anthu oyipa.
2 Jer ti si, Bože, zaklon moj: zašto me odbacuješ? Zašto obilazim žalostan, pritisnut dušmanima?
Pajatu Inu Mulungu ndinu mphamvu zanga. Nʼchifukwa chiyani mwandikana ine? Nʼchifukwa chiyani ndiyenera kuyenda ndikulira, woponderezedwa ndi mdani?
3 Pošlji svjetlost svoju i vjernost: nek' me vode, nek' me dovedu na tvoju svetu goru, u šatore tvoje!
Tumizani kuwunika kwanu ndi choonadi chanu kuti zinditsogolere; mulole kuti zindifikitse ku phiri lanu loyera, kumalo kumene inu mumakhala.
4 I pristupit ću Božjem žrtveniku, Bogu, radosti svojoj. Harfom ću slaviti tebe, Bože, o Bože moj!
Ndipo ndidzapita ku guwa lansembe la Mulungu, kwa Mulungu, chimwemwe changa ndi chikondwerero changa. Ndidzakutamandani ndi zeze, Inu Mulungu wanga.
5 Što si mi, dušo, klonula i što jecaš u meni? U Boga se uzdaj, jer opet ću ga slaviti, spasenje svoje, Boga svog!
Nʼchifukwa chiyani uli ndi chisoni iwe moyo wanga? Nʼchifukwa chiyani wakhumudwa iwe mʼkati mwanga? Khulupirira Mulungu, pakuti ndidzamutamandabe Iye, Mpulumutsi wanga ndi Mulungu wanga.