< Psalmi 146 >

1 Aleluja! Hvali, dušo moja, Jahvu!
Tamandani Yehova. Tamanda Yehova, iwe moyo wanga.
2 Hvalit ću Jahvu sveg života svojeg. Dok me bude, Bogu svom ću pjevati.
Ndidzatamanda Yehova ndi moyo wanga wonse; ndidzayimba nyimbo zamatamando kwa Mulungu wanga nthawi yonse ya moyo wanga.
3 Ne uzdajte se u knezove, u čovjeka od kog nema spasenja!
Musamadalire mafumu, anthu osakhalitsa, amene sangathe kupulumutsa.
4 Iziđe li duh iz njega, u zemlju svoju on se vraća i propadaju sve misli njegove.
Pamene mizimu yawo yachoka, iwo amabwerera ku dothi; zimene ankafuna kuchita zimatha tsiku lomwelo.
5 Blago onom kome je pomoćnik Bog Jakovljev, kome je ufanje u Jahvi, Bogu njegovu,
Wodala ndi amene thandizo lake ndi Mulungu wa Yakobo.
6 koji stvori nebo i zemlju, more i sve što je u njima; koji ostaje vjeran dovijeka,
Wolenga kumwamba ndi dziko lapansi, nyanja ndi zonse zili mʼmenemo; Yehova, amene ndi wokhulupirika kwamuyaya.
7 potlačenima vraća pravicu, a gladnima kruh daje. Jahve oslobađa sužnje,
Iye amachitira chilungamo anthu oponderezedwa ndipo amapereka chakudya kwa anthu anjala. Yehova amamasula amʼndende,
8 Jahve slijepcima oči otvara. Jahve uspravlja prignute, Jahve ljubi pravedne.
Yehova amatsekula maso anthu osaona, Yehova amadzutsa onse amene awerama pansi, Yehova amakonda anthu olungama.
9 Jahve štiti tuđince, sirote i udovice podupire, a grešnicima mrsi putove.
Yehova amasamalira alendo ndipo amathandiza ana ndi akazi amasiye, koma amasokoneza njira za anthu oyipa.
10 Jahve će kraljevati dovijeka, tvoj Bog, Sione, od koljena do koljena. Aleluja!
Yehova ndiye Mfumu mpaka muyaya, Mulungu wako iwe Ziyoni, pa mibado yonse. Tamandani Yehova.

< Psalmi 146 >