< Psalmi 125 >
1 Hodočasnička pjesma. Tko se uzda u Jahvu, on je kao brdo Sion: ne pomiče se, ostaje dovijeka.
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Amene amadalira Yehova ali ngati phiri la Ziyoni, limene silingagwedezeke koma ndi lokhala mpaka muyaya.
2 Bregovi okružuju Jeruzalem: Jahve okružuje narod svoj odsada i dovijeka.
Monga mapiri azungulira Yerusalemu, momwemonso Yehova azungulira anthu ake kuyambira tsopano mpaka muyaya.
3 I neće vladati žezlo bezbožničko nad udesom pravednih, da ne bi pravedni ruke za bezakonjem pružili.
Ndodo yaufumu ya anthu oyipa sidzakhala pa dziko limene lapatsidwa kwa anthu olungama, kuti anthu olungamawo angachite nawonso zoyipa.
4 Učini, Jahve, dobro dobrima i čestitima u srcu.
Yehova chitirani zabwino amene ndi abwino, amene ndi olungama mtima
5 A koji na krive skreću putove nek' ih istrijebi Jahve sa zločincima! Mir nad Izraelom!
Koma amene amatembenukira ku njira zokhotakhota, Yehova adzawachotsa pamodzi ndi anthu ochita zoyipa. Mtendere ukhale pa Israeli.