< Psalmi 124 >

1 Hodočasnička pjesma. Davidova. Da nije Jahve za nas bio - neka slobodno rekne Izrael -
Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Akanapanda kukhala mbali yathu Yehova, anene tsono Israeli,
2 da nije Jahve za nas bio: kad se ljudi digoše proti nama,
akanapanda kukhala mbali yathu Yehova, potiwukira anthuwo,
3 žive bi nas progutali. Kad je uskipio bijes njihov na nas,
iwo atatipsera mtima, akanatimeza amoyo;
4 voda bi nas podavila; bujica bi nas odnijela,
chigumula chikanatimiza, mtsinje ukanatikokolola,
5 vode pobješnjele sve nas potopile.
madzi a mkokomo akanatikokolola.
6 Blagoslovljen Jahve koji nas ne dade za plijen zubima njihovim!
Atamandike Yehova, amene sanalole kuti tikhale chakudya cha mano awo.
7 Duša je naša poput ptice umakla iz zamke lovaca: raskinula se zamka, a mi umakosmo!
Moyo wathu wawonjoka ngati mbalame yokodwa mu msampha wa mlenje; msampha wathyoka, ndipo ife tapulumuka.
8 Pomoć je naša u imenu Jahve koji stvori nebo i zemlju.
Thandizo lathu lili mʼdzina la Yehova wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.

< Psalmi 124 >