< Psalmi 104 >
1 Blagoslivljaj Jahvu, dušo moja, Jahve, Bože moj, silno si velik! Odjeven veličanstvom i ljepotom,
Tamanda Yehova, iwe moyo wanga. Inu Yehova Mulungu wanga, ndinu wamkulu kwambiri; mwavala ulemerero ndi ufumu.
2 svjetlošću ogrnut kao plaštem! Nebo si razapeo kao šator,
Iye wadzifunditsa kuwala ngati chovala; watambasula miyamba ngati tenti
3 na vodama sagradio dvorove svoje. Od oblaka praviš kola svoja, na krilima vjetrova putuješ.
ndipo wayika pa madzi mitanda ya chipinda chake. Iye amasandutsa mitambo kukhala galeta lake, ndi kuwuluka pa mapiko a mphepo.
4 Vjetrove uzimaš za glasnike, a žarki oganj za slugu svojega.
Amapanga mphepo kukhala amithenga ake, malawi amoto kukhala atumiki ake.
5 Zemlju si stavio na stupove njene: neće se poljuljati u vijeke vjekova,
Anakhazikitsa dziko lapansi pa maziko ake; silingasunthike.
6 pokrio si je vodama bezdanim k'o haljinom, iznad bregova stajahu vode;
Munaliphimba ndi nyanja yozama ngati chovala; madzi anayimirira pamwamba pa mapiri.
7 na tvoju se prijetnju povukoše, od tvoje grmljavine zadrhtaše.
Koma pakudzudzula kwanu madzi anathawa, pa mkokomo wa bingu lanu iwo anamwazika;
8 Bregovi se digoše, doline spustiše na mjesto koje si im odredio.
Inu munamiza mapiri, iwo anatsikira ku zigwa kumalo kumene munawakonzera.
9 Odredio si granicu koju ne smiju prijeći, da opet ne pokriju zemlju.
Inu munayika malire ndipo sangathe kudutsa, iwo sadzamizanso dziko lapansi.
10 Izvore svraćaš u potoke što žubore među brdima.
Iye achititsa akasupe kutulutsa madzi kupita ku zigwa; madziwo amayenda pakati pa mapiri.
11 Oni poje sve živine poljske, divlji magarci žeđ gase u njima.
Iwo amapereka madzi kwa zirombo zonse zakuthengo; abulu akuthengo amapha ludzu lawo.
12 Uz njih se gnijezde ptice nebeske i pjevaju među granama.
Mbalame zamlengalenga zimayika zisa mʼmbali mwa madzi; zimayimba pakati pa thambo.
13 Ti natapaš bregove iz dvorova svojih, zemlja se nasićuje plodom tvojih ruku.
Iye amathirira mapiri kuchokera ku zipinda zake zapamwamba; dziko lapansi limakhutitsidwa ndi chipatso cha ntchito yake.
14 Ti daješ te niče trava za stoku i bilje na korist čovjeku da izvede kruh iz zemlje
Amameretsa udzu kuti ngʼombe zidye, ndi zomera, kuti munthu azilima kubweretsa chakudya kuchokera mʼdziko lapansi:
15 i vino što razvedruje srce čovječje; da uljem lice osvježi i da kruh okrijepi srce čovjeku.
vinyo amene amasangalatsa mtima wa munthu, mafuta amene amachititsa nkhope yake kuwala, ndi buledi amene amapereka mphamvu.
16 Stabla se Jahvina napajaju hranom, cedri libanonski koje on zasadi.
Mitengo ya Yehova ndi yothiriridwa bwino, mikungudza ya ku Lebanoni imene Iye anadzala.
17 Ondje se ptice gnijezde, u čempresu dom je rodin.
Mbalame zimamanga zisa zawo; kakowa ali ndi malo ake mʼmikungudzamo.
18 Visoki bregovi daju kozorogu a pećine jazavcu sklonište.
Mapiri ataliatali ndi a mbalale; mʼmingʼalu ya miyala ndi mobisalamo mbira.
19 Ti si stvorio mjesec da označuje vremena i sunce znade kada ima zaći.
Mwezi umasiyanitsa nyengo ndipo dzuwa limadziwa nthawi yake yolowera.
20 Kad razastreš tmine i noć se spusti, tad se šuljaju u njoj životinje šumske.
Inu mumabweretsa mdima nukhala usiku, ndipo zirombo zonse za ku nkhalango zimatuluka.
21 Lavići riču za plijenom i od Boga hranu traže.
Mikango imabangula kufuna nyama, ndi kufunafuna chakudya chawo kuchokera kwa Mulungu.
22 Kad sunce ograne, nestaju i liježu na ležaje.
Dzuwa limatuluka ndipo iyo imapita kukabisala; imabwerera kukagona pansi mʼmapanga awo.
23 Tad čovjek izlazi na dnevni posao i na rad do večeri.
Pamenepo munthu amapita ku ntchito yake, kukagwira ntchito yake mpaka madzulo.
24 Kako su brojna tvoja djela, o Jahve! Sve si to mudro učinio: puna je zemlja stvorenja tvojih.
Ntchito zanu ndi zochulukadi Inu Yehova! Munazipanga zonse mwanzeru, dziko lapansi ladzaza ndi zolengedwa zanu.
25 Eno mora, velika i široka, u njemu vrve gmazovi bez broja, životinje male i velike.
Kuli nyanja yayikulu ndi yotambalala, yodzaza ndi zolengedwa zosawerengeka, zamoyo zanu zazikulu ndi zazingʼono zomwe.
26 Onud prolaze nemani, Levijatan kojeg stvori da se igra u njemu.
Kumeneko sitima zapamadzi zimayenda uku ndi uku, ndiponso Leviyatani amene munamulenga kuti asewere kumeneko.
27 I sva ova bića željno čekaju da ih nahraniš na vrijeme.
Zonsezi zimayangʼana kwa Inu kuti muzipatse chakudya chawo pa nthawi yake yoyenera.
28 Daješ li im, tada sabiru: otvaraš li ruku, nasite se dobrima.
Mukazipatsa, zimachisonkhanitsa pamodzi; mukatsekula dzanja lanu, izo zimakhutitsidwa ndi zinthu zabwino.
29 Sakriješ li lice svoje, tad se rastuže; ako dah im oduzmeš, ugibaju i opet se u prah vraćaju.
Mukabisa nkhope yanu, izo zimachita mantha aakulu; mukachotsa mpweya wawo, zimafa ndi kubwerera ku fumbi.
30 Pošalješ li dah svoj, opet nastaju, i tako obnavljaš lice zemlje.
Mukatumiza mzimu wanu, izo zimalengedwa ndipo mumakozanso maonekedwe a dziko lapansi.
31 Neka dovijeka traje slava Jahvina: nek' se raduje Jahve u djelima svojim!
Ulemerero wa Yehova ukhalebe mpaka muyaya; Yehova akondwere ndi ntchito ya manja ake;
32 On pogleda zemlju i ona se potrese, dotakne bregove, oni se zadime.
Iye amene amayangʼana dziko lapansi ndipo limanjenjemera, amene amakhudza mapiri ndipo amatuluka utsi.
33 Pjevat ću Jahvi dokle god živim, svirat ću Bogu svome dokle god me bude.
Ine ndidzayimbira Yehova moyo wanga wonse; ndidzayimbira matamando Mulungu wanga nthawi yonse imene ndili ndi moyo.
34 Bilo mu milo pjevanje moje! Ja ću se radovati u Jahvi.
Zolingalira zanga zikhale zomukomera Iye, pamene ndikusangalala mwa Yehova.
35 Nek' zločinci sa zemlje nestanu i bezbožnika nek' više ne bude! Blagoslivljaj Jahvu, dušo moja! Aleluja!
Koma anthu ochimwa awonongeke pa dziko lapansi ndipo anthu oyipa asapezekenso. Tamanda Yehova, Iwe moyo wanga. Tamandani Yehova.