< Mudre Izreke 1 >
1 Mudre izreke Salomona, sina Davidova, kralja izraelskog:
Iyi ndi miyambi ya Solomoni mwana wa Davide, mfumu ya Israeli:
2 da se spozna mudrost i pouka, da se shvate razumne riječi;
Ndi yothandiza kuti munthu adziwe nzeru ndi malangizo; kuti amvetse mawu a matanthauzo ozama;
3 da se primi umna pouka, pravda i pravica i nepristranost;
kuti alandire malangizo othandiza kuti achite zinthu mwanzeru, akhale wangwiro, wachilungamo ndiponso wosakondera.
4 da se dade pamet neiskusnima, mladiću znanje i umijeće;
Ndi yothandiza munthu wamba kuti aphunzire nzeru za kuchenjera, achinyamata kudziwa zinthu bwino ndi kulingalira.
5 kad mudar čuje, da umnoži znanje, a razuman steče mudrije misli;
Munthu wanzeru amvetse bwino miyamboyi kuti awonjezere kuphunzira kwake, ndi munthu womvetsa zinthu bwino apatepo luso,
6 da razumije izreke i prispodobe, riječi mudraca i njihove zagonetke.
kuti azimvetsa miyambi ndi mafanizo, mawu a anthu anzeru ndi mikuluwiko.
7 Strah je Gospodnji početak spoznaje, ali ludi preziru mudrost i pouku.
Kuopa Yehova ndiye chiyambi cha nzeru. Zitsiru zimanyoza nzeru ndi malangizo.
8 Poslušaj, sine moj, pouku oca svoga i ne odbacuj naputka svoje majke!
Mwana wanga, mvera malangizo a abambo ako ndipo usakane mawu okuwongolera a amayi ako.
9 Jer će ti biti ljupki vijenac na glavi i ogrlica oko tvoga vrata.
Ali ngati sangamutu yokongola ya maluwa pamutu pako ndiponso ali ngati mkanda mʼkhosi mwako.
10 Sine moj, ako te grešnici mame, ne pristaj;
Mwana wanga, ngati anthu oyipa afuna kukukopa usamawamvere.
11 ako bi rekli: “Hodi s nama, da vrebamo krv, čekamo u zasjedi nevina ni za što;
Akadzati, “Tiye kuno; tikabisale kuti tiphe anthu, tikabisalire anthu osalakwa;
12 da ih progutamo žive kao carstvo smrti i cijele kao one koji silaze u grob; (Sheol )
tiwameze amoyo ngati manda, ndi athunthu ngati anthu otsikira mʼdzenje. (Sheol )
13 naplijenit ćemo svakojaka blaga, napuniti svoje kuće plijenom;
Motero tidzapeza zinthu zosiyanasiyana zamtengowapatali ndi kudzaza nyumba zathu ndi zolanda;
14 bacat ćeš s nama svoj ždrijeb, svi ćemo zajedno imati jednu kesu.”
Bwera, chita nafe maere, ndipo tidzagawana chuma chathu tonse.”
15 Sine moj, ne idi s njima na put, makni nogu od njihove staze.
Mwana wanga, usayende nawo pamodzi, usatsagane nawo mʼnjira zawozo.
16 Jer na zlo trče svojim nogama i hite prolijevati krv.
Iwowatu amangofuna zoyipa zokhazokha, amathamangira kukhetsa magazi.
17 Jer uzalud je razapinjati mrežu pred očima svima pticama.
Nʼkopanda phindu kutchera msampha mbalame zikuona!
18 A oni vrebaju vlastitu krv, postavljaju zasjedu svojemu životu.
Koma anthu amenewa amangobisalira miyoyo yawo yomwe; amangodzitchera okha msampha!
19 Takva je sudba svih lakomih na ružan dobitak: on ih života stane.
Awa ndiwo mathero a anthu opeza chuma mwankhanza; chumacho chimapha mwiniwake.
20 Mudrost glasno uzvikuje na ulici, na trgovima diže svoj glas;
Nzeru ikufuwula mu msewu, ikuyankhula mokweza mawu mʼmisika;
21 propovijeda po bučnim uglovima, na otvorenim gradskim vratima govori svoje riječi:
ikufuwula pa mphambano ya misewu, ikuyankhula pa zipata za mzinda kuti,
22 “Dokle ćete, vi glupi, ljubiti glupost i dokle će podsmjevačima biti milo podsmijevanje, i dokle će bezumnici mrziti znanje?
“Kodi inu anthu osachangamukanu, mudzakondwera ndi kusachangamuka mpaka liti? Nanga anthu onyogodola adzakondabe kunyogodola mpaka liti? Kapena opusa adzadana ndi nzeru mpaka liti?
23 Poslušajte moju opomenu! Gle, svoj duh pred vas izlijevam, hoću vas poučiti svojim riječima.
Tamverani mawu anga a chidzudzulo. Ine ndikukuwuzani maganizo anga ndi kukudziwitsani mawu anga.
24 Koliko sam vas zvala, a vi ste odbijali; pružala sam ruku, ali je nitko ne opazi.
Popeza ndinakuyitanani koma inu munakana kumvera. Ndinayesa kukuthandizani koma panalibe amene anasamala.
25 Nego ste odbacili svaki moj savjet i niste poslušali moje opomene;
Uphungu wanga munawunyoza. Kudzudzula kwanga simunakusamale.
26 zato ću se i ja smijati vašoj propasti, rugat ću se kad vas obuzme tjeskoba:
Ndiye inenso ndidzakusekani mukadzakhala mʼmavuto; ndidzakunyogodolani chikadzakugwerani chimene mumachiopacho.
27 kad navali na vas strah kao nevrijeme i zgrabi vas propast kao vihor, kad navali na vas nevolja i muka.
Chiwonongeko chikadzakugwerani ngati namondwe, tsoka likadzakufikirani ngati kamvuluvulu, mavuto ndi masautso akadzakugwerani.
28 Tada će me zvati, ali se ja neću odazvati; tražit će me, ali me neće naći.
“Tsono mudzandiyitana koma sindidzayankha; mudzandifunafuna, koma simudzandipeza.
29 Jer su mrzili spoznaju i nisu izabrali Gospodnjeg straha
Popeza iwo anadana ndi chidziwitso ndipo sanasankhe kuopa Yehova,
30 niti su poslušali moj savjet, nego su prezreli svaku moju opomenu.
popeza iwo sanasamale malangizo anga ndipo ananyoza chidzudzulo changa.
31 Zato će jesti plod svojeg vladanja i nasititi se vlastitih savjeta.
Tsono adzadya zipatso zoyenera mayendedwe awo ndi kukhuta ndi ntchito zimene anachita kwa ena.
32 Jer glupe će ubiti njihovo odbijanje, a nemar će upropastiti bezumne.
Pakuti anthu osachangamuka amaphedwa chifukwa cha kusochera kwawo, ndipo zitsiru zimadziwononga zokha chifukwa cha mphwayi zawo.
33 A tko sluša mene, bezbrižan ostaje i spokojno živi bez straha od zla.”
Koma aliyense wondimvera adzakhala mwa bata; adzakhala mosatekeseka posaopa chilichonse.”