< Mudre Izreke 14 >

1 Ženska mudrost sagradi kuću, a ludost je rukama razgrađuje.
Mkazi wanzeru amamanga banja lake, koma mkazi wopusa amalimasula ndi manja ake omwe.
2 Tko živi s poštenjem, boji se Jahve, a tko ide stranputicom, prezire ga.
Amene amayenda molungama amaopa Yehova, koma amene njira zake ndi zoyipa amanyoza Yehova.
3 U luđakovim je ustima šiba za oholost njegovu, a mudre štite vlastite usne.
Kuyankhula kwa chitsiru kumamuyitanira ndodo pa msana, koma milomo ya munthu wanzeru imamuteteza.
4 Gdje nema volova, prazne su jasle, a obilna je žetva od snage bikove.
Pakasowa ngʼombe zolima gome limakhala lopanda chakudya, koma pakakhala ngʼombe zamphamvu zakudya zimachulukanso.
5 Istinit svjedok ne laže, a krivi svjedok širi laž.
Mboni yokhulupirika sinama, koma mboni yonyenga imayankhula zabodza.
6 Podsmjevač traži mudrost i ne nalazi je, a razumni lako dolazi do znanja.
Wonyoza anzake amafunafuna nzeru koma osayipeza, koma munthu womvetsa bwino amadziwa zinthu msanga.
7 Idi od čovjeka bezumna jer nećeš upoznati usne što zbore znanje.
Khala kutali ndi munthu wopusa chifukwa sudzapeza mawu a nzeru.
8 Mudrost je pametna čovjeka u tom što pazi na svoj put, a bezumnička ludost prijevara je.
Nzeru za munthu wochenjera zagona pakuzindikira njira zake. Koma uchitsiru wa zitsiru umapusitsidwa ndi chinyengo chawo chomwe.
9 Luđacima je grijeh šala, a milost je Božja s poštenima.
Zitsiru zimanyoza za kulapa machimo, awo, koma kufuna kwabwino kumapezeka mwa anthu olungama.
10 Srce poznaje svoj jad, i veselje njegovo ne može dijeliti nitko drugi.
Mtima uliwonse umadziwa wokha zowawa zake, ndipo palibe wina aliyense angadziwe kukondwa kwake.
11 Dom opakih propast će, a šator će pravednika procvasti.
Nyumba ya munthu woyipa idzapasuka, koma tenti ya munthu wowongoka mtima idzakhazikika.
12 Neki se put učini čovjeku prav, a na koncu vodi k smrti.
Pali njira ina yooneka ngati yabwino kwa munthu, koma kumatsiriziro kwake ndi ku imfa.
13 I u smijehu srce osjeća bol, a poslije veselja dolazi tuga.
Ngakhale poseka mtima utha kumva kuwawa, ndipo mathero achimwemwe akhoza kukhala chisoni.
14 Otpadnik se siti svojim prestupcima, a dobar čovjek svojim radom.
Munthu wosakhulupirika adzalandira zogwirizana ndi ntchito yake, koma munthu wabwino adzalandira mphotho ya ntchito yake.
15 Glupan vjeruje svakoj riječi, a pametan pazi na korak svoj.
Munthu wopusa amakhulupirira chilichonse, koma munthu wochenjera amaganizira bwino mayendedwe ake.
16 Mudar se boji i oda zla se uklanja, a bezuman se raspaljuje i bez straha je.
Munthu wanzeru amaopa Mulungu ndipo amapewa zoyipa, koma munthu wopusa ndi wokula mtima amakhala wosasamala.
17 Nagao čovjek čini ludosti, a razborit ih podnosi.
Munthu wopsa mtima msanga amachita zinthu za uchitsiru, ndipo anthu amadana ndi munthu wachinyengo.
18 Glupaci baštine ludost, a mudre ovjenčava znanje.
Anthu opusa amalandira uchitsiru, koma anthu ochenjera amavekedwa chipewa cha ulemerero wa kudziwa zinthu.
19 Zli padaju ničice pred dobrima i opaki pred vratima pravednikovim.
Anthu oyipa adzagwada pamaso pa anthu abwino, ndipo anthu oyipa adzapempha thandizo kwa anthu olungama.
20 I svom prijatelju mrzak je siromah, a bogataš ima mnogo ljubitelja.
Munthu wosauka ngakhale anansi ake omwe amamuda, koma munthu wolemera ali ndi abwenzi ambiri.
21 Griješi tko prezire bližnjega svoga, a blago onomu tko je milostiv ubogima.
Wonyoza mnansi wake ndi wochimwa koma ndi wodala amene amachitira chifundo anthu osowa.
22 Koji snuju zlo, ne hode li stranputicom, a zar nisu dobrota i vjernost s onima koji snuju dobro?
Kodi amene amakonzekera zoyipa sasochera? Koma amene amakonzekera zabwino anthu amawaonetsa chikondi ndi kukhulupirika.
23 U svakom trudu ima probitka, a pusto brbljanje samo je na siromaštvo.
Ntchito iliyonse imakhala ndi phindu, koma kuyankhulayankhula kumabweretsa umphawi.
24 Mudrima je vijenac bogatstvo njihovo, a bezumnima kruna - njihova ludost.
Chipewa chaulemu cha anthu a nzeru ndi chuma chawo chomwe, koma malipiro a zitsiru ndi uchitsiru.
25 Istinit svjedok izbavlja duše, a tko laži širi, taj je varalica.
Mboni yokhulupirika imapulumutsa miyoyo, koma mboni yabodza imaphetsa.
26 U strahu je Gospodnjem veliko pouzdanje i njegovim je sinovima utočište.
Amene amaopa Yehova ali ndi chitetezo chokwanira ndipo iye adzakhala pothawira pa ana ake.
27 Strah Gospodnji izvor je života: on izbavlja od zamke smrti.
Kuopa Yehova ndiye kasupe wamoyo, kumathandiza munthu kuti apewe msampha wa imfa.
28 Mnoštvo je naroda ponos kralju, a bez puka knez propada.
Gulu lalikulu la anthu ndiye ulemerero wa mfumu, koma popanda anthu kalonga amawonongeka.
29 Tko se teško srdi, velike je razboritosti, a nabusit duhom pokazuje ludost.
Munthu wosapsa mtima msanga amamvetsa zinthu kwambiri, koma munthu wopsa mtima msanga amaonetsa uchitsiru wake.
30 Mirno je srce život tijelu, a ljubomor je gnjilež u kostima.
Mtima wodekha umapatsa thupi moyo, koma nsanje imawoletsa mafupa.
31 Tko tlači siromaha huli na stvoritelja, a časti ga tko je milostiv ubogomu.
Amene amapondereza mʼmphawi amanyoza mlengi wake, koma wochitira chifundo munthu wosowa amalemekeza Mulungu.
32 Opaki propada zbog vlastite pakosti, a pravednik i u samoj smrti nalazi utočište.
Anthu oyipa adzakanthidwa chifukwa cha ntchito zawo zomwe, koma olungama adzatetezedwa mwa imfa yawo.
33 U razumnu srcu mudrost počiva, a što je u bezumnome, to se i pokaže.
Nzeru zimakhala mu mtima mwa anthu omvetsa zinthu, koma nzeru sipezeka mu mtima mwa zitsiru.
34 Pravednost uzvisuje narod, a grijeh je sramota pucima.
Chilungamo chimakweza mtundu wa anthu, koma uchimo umachititsa manyazi mtundu uliwonse.
35 Kralju je mio razborit sluga, a na sramotna se srdi.
Mfumu imasangalatsidwa ndi wantchito wanzeru, koma imachitira ukali wantchito wochititsa manyazi.

< Mudre Izreke 14 >