< Brojevi 7 >
1 U onaj dan kad Mojsije završi podizanje Prebivališta i kad ga pomaza i posveti sa svim njegovim posuđem, a tako i žrtvenik sa svim njegovim priborom,
Mose atamaliza kuyimika chihema chija, anachidzoza mafuta ndi kuchipatula pamodzi ndi ziwiya zake zonse. Anadzozanso guwa lansembe ndi kulipatula pamodzi ndi ziwiya zake zonse.
2 pristupe glavari izraelski, starješine njihovih pradjedovskih domova, to jest knezovi plemenski koji su vodili popisivanje,
Kenaka atsogoleri a Aisraeli, akuluakulu a mabanja omwe ankayangʼanira mafuko a anthu omwe anawawerenga aja, anachita chopereka.
3 i dovedu svoje prinose pred Jahvu: šestora teretna kola i dvanaest volova - jedna kola za dvojicu glavara i vola za svakoga pojedinoga. Dovedu ih pred Prebivalište.
Anabweretsa zopereka zawo pamaso pa Yehova: ngolo zophimbidwa zisanu ndi imodzi ndiponso ngʼombe zothena khumi ndi ziwiri. Mtsogoleri mmodzi ngʼombe yothena imodzi ndipo atsogoleri awiri ngolo imodzi. Izi anazipereka ku chihema.
4 Tada Jahve progovori Mojsiju:
Yehova anawuza Mose kuti,
5 “Primi to od njih za upotrebu pri službi u Šatoru sastanka; onda to podaj svakome levitu prema njegovoj službi.”
“Ulandire zimenezi kwa iwo kuti zigwire ntchito ku tenti ya msonkhano. Uzipereke kwa Alevi, aliyense monga mwa ntchito yake.”
6 Mojsije uze kola i volove pa ih dade levitima.
Choncho Mose anatenga ngolo ndi ngʼombe zothenazo nazipereka kwa Alevi.
7 Dvoja kola i četiri vola dade Geršonovcima prema njihovoj službi,
Anapereka ngolo ziwiri ndi ngʼombe zothena zinayi kwa Ageresoni monga mwantchito yawo
8 a četvera kola i osam volova dade Merarijevcima prema njihovoj službi pod vodstvom Itamara, sina svećenika Arona.
ndiponso anapereka ngolo zinayi ndi ngʼombe zothena zisanu ndi zitatu kwa Amerari molingananso ndi ntchito yawo. Onsewa ankawayangʼanira anali Itamara mwana wa Aaroni wansembe.
9 Kehatovcima nije dao ništa, jer je njihova zadaća bila nositi posvećene predmete na ramenima.
Koma Mose sanapereke zimenezi kwa Akohati chifukwa zinthu zawo zopatulika zomwe ankayangʼanira zinali zoti azinyamula pa mapewa awo.
10 Tada glavari prinesu prinos za posvetu žrtvenika na dan njegova pomazanja. Dok su glavari prinosili svoje prinose pred žrtvenik,
Guwa la nsembe litadzozedwa, atsogoleri anabweretsa zopereka zawo zopatulira guwa nazipereka paguwapo.
11 Jahve progovori Mojsiju: “Svakoga dana neka po jedan glavar donese svoj prinos za posvetu žrtvenika!”
Pakuti Yehova anawuza Mose kuti, “Tsiku lililonse mtsogoleri mmodzi azibweretsa chopereka chake chopatulira guwa lansembe.”
12 Prvoga dana donese svoj prinos Nahšon, sin Aminadabov, od plemena Judina.
Amene anabweretsa chopereka chake tsiku loyamba anali Naasoni mwana wa Aminadabu wa fuko la Yuda.
13 Njegov je prinos bio: jedna srebrna zdjela teška sto trideset šekela i jedan srebrni kotlić od sedamdeset šekela, prema hramskom šekelu; jedno i drugo bijaše napunjeno najboljim brašnom, zamiješenim u ulju, za prinosnicu.
Chopereka chake chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi, ndi beseni lasiliva limodzi lowazira, lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo wopatulika ndipo zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta ngati chopereka chachakudya;
14 Onda jedna zlatna posudica od deset šekela puna tamjana;
mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
15 jedan junac, jedan ovan, jedno janje od godinu dana za paljenicu;
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa wamwamuna mmodzi wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza;
16 jedan jarac za žrtvu okajnicu,
mbuzi yayimuna imodzi, nsembe ya machimo;
17 a za žrtvu pričesnicu: dva vola, pet ovnova, pet kozlića i pet jednogodišnjih janjaca. To je bio prinos Nahšona, Aminadabova sina.
ndi ngʼombe zothena ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa asanu a chaka chimodzi kuti zikhale za nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Naasoni mwana wa Aminadabu.
18 Drugoga dana donese svoj prinos Netanel, sin Suarov, glavar Jisakarovaca.
Pa tsiku lachiwiri, Natanieli mwana wa Zuwara, mtsogoleri wa Isakara, anabweretsa chopereka chake.
19 Za svoj prinos donio je: jednu srebrnu zdjelu tešku sto trideset šekela, jedan srebrni kotlić od sedamdeset šekela, prema hramskom šekelu; oboje puno najboljeg brašna, zamiješena u ulju, za prinosnicu;
Chopereka chomwe anabwera nacho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, molingana ndi muyeso wa ku malo opatulika. Mbale zonse zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka cha chakudya.
20 onda jednu zlatnu posudicu od deset šekela punu tamjana;
Mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110 yodzaza ndi lubani;
21 jednog junca, jednoga ovna, jedno janje od godinu dana za paljenicu;
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza:
22 jednog jarca za okajnicu,
mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yotetezera machimo;
23 a za pričesnicu: dva vola, pet ovnova, pet kozlića i pet jednogodišnjih janjaca. To je bio prinos Netanela, Suarova sina.
ndi ngʼombe ziwiri, nkhosa zazimuna ziwiri, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa asanu a chaka chimodzi, nsembe ya chiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Netanieli mwana wa Zuwara.
24 Trećega dana donese svoj prinos glavar Zebulunovaca, Eliab, sin Helonov.
Pa tsiku lachitatu, Eliabu mwana wa Heloni, mtsogoleri wa Azebuloni, anabweretsa chopereka chake.
25 Njegov je prinos bio: jedna srebrna zdjela teška sto trideset šekela i jedan srebrni kotlić od sedamdeset šekela, prema hramskom šekelu; oboje puno najboljeg brašna, zamiješena u ulju, za prinosnicu;
Chopereka chake chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, ndi beseni limodzi lasiliva lowazira lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika, mbale zonse zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, chopereka cha chakudya;
26 jedna zlatna posudica puna tamjana;
mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
27 jedan junac, jedan ovan, jedno janje od godinu dana za paljenicu;
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa wamwamuna mmodzi wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza;
28 jedan jarac za okajnicu,
mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
29 a za pričesnicu: dva vola, pet ovnova, pet kozlića i pet jednogodišnjih janjaca. To je bio prinos Eliaba, Helonova sina.
ndi ngʼombe ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Eliabu mwana wa Heloni.
30 Četvrtog dana donese svoj prinos glavar Rubenovaca, Elisur, sin Šedeurov.
Tsiku lachinayi linali la Elizuri mwana wa Sedeuri, mtsogoleri wa fuko la Rubeni, anabweretsa chopereka chake.
31 Njegov je prinos bio: jedna srebrna zdjela teška sto trideset šekela, jedan srebrni kotlić od sedamdeset šekela, prema hramskom šekelu; oboje puno najboljeg brašna, zamiješena u ulju, za prinosnicu;
Chopereka chake chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, chopereka chachakudya.
32 onda jedna zlatna posudica od deset šekela puna tamjana;
Mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
33 jedan junac, jedan ovan, jedno janje od godinu dana za paljenicu;
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza;
34 jedan jarac za okajnicu,
mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
35 a za pričesnicu: dva vola, pet ovnova, pet kozlića i pet jednogodišnjih janjaca. To je bio prinos Elisura, Šedeurova sina.
ndi ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna ziwiri, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Elizuri mwana wa Sedeuri.
36 Petoga dana donese svoj prinos glavar Šimunovaca, Šelumiel, sim Surišadajev.
Pa tsiku lachisanu Selumieli mwana wa Zurisadai, mtsogoleri wa fuko la Simeoni, anabweretsa chopereka chake.
37 Njegov je prinos bio: jedna srebrna zdjela teška sto trideset šekela, jedan srebrni kotlić od sedamdeset šekela, prema hramskom šekelu; oboje napunjeno najboljim brašnom, zamiješenim u ulju, za prinosnicu;
Chopereka chake chinali mbale yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka ndi beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika. Zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
38 onda jedna zlatna posudica od deset šekela puna tamjana;
mbale yagolide imodzi yolemera 110, yodzaza ndi lubani;
39 jedan junac, jedan ovan, jedno janje od godinu dana za paljenicu;
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi ndi mwana wankhosa mmodzi wamwamuna wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza;
40 jedan jarac za okajnicu,
mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
41 a za pričesnicu: dva vola, pet ovnova, pet kozlića i pet jednogodišnjih janjaca. To je bio prinos Šelumiela, Surišadajeva sina.
ngʼombe ziwiri, nkhosa zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Selumieli mwana wa Zurisadai.
42 Šestoga dana donese svoj prinos glavar Gadovaca, Elijasaf, sin Deuelov.
Pa tsiku lachisanu ndi chimodzi, Eliyasafu mwana wa Deuweli, mtsogoleri wa fuko la Gadi, anabweretsa chopereka chake.
43 Njegov je prinos bio: jedna srebrna zdjela teška sto trideset šekela, jedan srebrni kotlić od sedamdeset šekela, prema hramskom šekelu; oboje napunjeno najboljim brašnom, zamiješenim u ulju, za prinosnicu;
Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
44 onda jedna zlatna posudica od deset šekela puna tamjana;
mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
45 jedan junac, jedan ovan, jedno janje od godinu dana za paljenicu;
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa wamwamuna mmodzi wa chaka chimodzi, chopereka cha nsembe yopsereza:
46 jedan jarac za okajnicu,
mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
47 a za pričesnicu: dva vola, pet ovnova, pet kozlića i pet jednogodišnjih janjaca. To je bio prinos Elijasafa, Deuelova sina.
ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Eliyasafu mwana wa Deuweli.
48 Sedmoga dana donese svoj prinos glavar Efrajimovaca, Elišama, sin Amihudov.
Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri Elisama mwana wa Amihudi, mtsogoleri wa fuko la Efereimu, anabweretsa chopereka chake.
49 Njegov je prinos bio: jedna srebrna zdjela teška sto trideset šekela i jedan srebrni kotlić od sedamdeset šekela, prema hramskom šekelu; oboje puno najboljeg brašna, zamiješena u ulju, za prinosnicu;
Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, ndi beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonsezi monga mwa muyeso wa ku malo opatulika, zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
50 onda jedna zlatna posudica od deset šekela puna tamjana;
mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
51 jedan junac, jedan ovan, jedno janje od godinu dana za paljenicu,
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa wamwamuna mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza;
52 jedan jarac za okajnicu,
mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
53 a za pričesnicu: dva vola, pet ovnova, pet kozlića i pet jednogodišnjih janjaca. To je bio prinos Elišama, Amihudova sina.
ngʼombe ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Elisama mwana wa Amihudi.
54 Osmoga dana donese svoj prinos glavar Manašeovaca, Gamliel, sin Pedahsurov.
Pa tsiku lachisanu ndi chitatu Gamalieli mwana wa Pedazuri, mtsogoleri wa fuko Manase, anabweretsa chopereka chake.
55 Njegov je prinos bio: jedna srebrna zdjela teška sto trideset šekela i jedan srebrni kotlić od sedamdeset šekela, prema hramskom šekelu; oboje napunjeno najboljim brašnom, zamiješenim u ulju, za prinosnicu;
Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, ndi beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
56 onda jedna zlatna posudica od deset šekela puna tamjana;
mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani,
57 jedan junac, jedan ovan, jedno janje od godinu dana za paljenicu;
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza;
58 jedan jarac za okajnicu,
mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
59 a za pričesnicu: dva vola, pet ovnova, pet kozlića i pet jednogodišnjih janjaca. To je bio prinos Gamliela, Pedahsurova sina.
ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Gamalieli mwana wa Pedazuri.
60 Devetoga dana donese svoj prinos glavar Benjaminovaca, Abidan, sin Gidonijev.
Pa tsiku lachisanu ndi chinayi Abidani mwana wa Gideoni mtsogoleri wa fuko la Benjamini, anabweretsa chopereka chake.
61 Njegov je prinos bio: jedna srebrna zdjela teška sto trideset šekela i jedan srebrni kotlić od sedamdeset šekela, prema hramskom šekelu; oboje napunjeno najboljim brašnom, zamiješenim u ulju, za prinosnicu;
Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka ndi beseni limodzi lowazira lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka cha zakudya;
62 onda jedna zlatna posudica od deset šekela puna tamjana,
mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
63 jedan junac, jedan ovan, jedno janje od godinu dana za paljenicu;
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza;
64 jedan jarac za okajnicu,
mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
65 a za pričesnicu: dva vola, pet ovnova, pet kozlića i pet jednogodišnjih janjaca. To je bio prinos Abidana, Gidonijeva sina.
ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu, ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Abidani mwana wa Gideoni.
66 Desetoga dana donese svoj prinos glavar Danovaca, Ahiezer, sin Amišadajev.
Pa tsiku lakhumi Ahiyezeri mwana wa Amisadai, mtsogoleri wa fuko la Dani anabweretsa chopereka chake.
67 Njegov je prinos bio: jedna srebrna zdjela teška sto trideset šekela i jedan srebrni kotlić od sedamdeset šekela, prema hramskom šekelu; oboje napunjeno najboljim brašnom, zamiješenim u ulju, za prikaznicu;
Chopereka chake chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika, zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
68 onda jedna zlatna posudica od deset šekela puna tamjana;
mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
69 jedan junac, jedan ovan, jedno janje od godinu dana za paljenicu;
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza;
70 jedan jarac za okajnicu,
mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
71 a za pričesnicu: dva vola, pet ovnova, pet kozlića i pet jednogodišnjih janjaca. To je bio prinos Ahiezera, Amišadajeva sina.
ndi ngʼombe ziwiri zazimuna, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu, ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Ahiyezeri mwana wa Amisadai.
72 Jedanaestoga dana donese svoj prinos glavar Ašerovaca, Pagiel, sin Okranov.
Pa tsiku la khumi ndi chimodzi, Pagieli mwana wa Okirani, mtsogoleri wa fuko la Aseri, anabweretsa chopereka chake.
73 Njegov je prinos bio: jedna srebrna zdjela teška sto trideset šekela i jedan srebrni kotlić od sedamdeset šekela, prema hramskom šekelu; oboje napunjeno najboljim brašnom, zamiješenim u ulju, za prinosnicu;
Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
74 onda jedna zlatna posudica od deset šekela puna tamjana;
mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
75 jedan junac, jedan ovan, jedno janje od godinu dana za paljenicu;
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza;
76 jedan jarac za okajnicu,
mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo;
77 a za pričesnicu: dva vola, pet ovnova, pet kozlića i pet jednogodišnjih janjaca. To je bio prinos Pagiela, Okranova sina.
ngʼombe ziwiri zazimuna, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu, ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Pagieli mwana wa Okirani.
78 Dvanaestoga dana donese svoj prinos glavar Naftalijevaca, Ahira, sin Enanov.
Pa tsiku la khumi ndi chimodzi Ahira mwana wa Enani, mtsogoleri wa fuko la Nafutali, anabweretsa chopereka chake.
79 Njegov je prinos bio: jedna srebrna zdjela teška sto trideset šekela i jedan srebrni kotlić od sedamdeset šekela, prema hramskom šekelu; oboje napunjeno najboljim brašnom, zamiješenim u ulju, za prinosnicu;
Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lowazira lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika, zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
80 onda jedna zlatna posudica od deset šekela puna tamjana;
mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
81 jedan junac, jedan ovan, jedno janje od godinu dana za paljenicu;
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza;
82 jedan jarac za okajnicu,
mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
83 a za pričesnicu: dva vola, pet ovnova, pet kozlića i pet jednogodišnjih janjaca. To je bio prinos Ahire, Enanova sina.
ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu, ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Ahira mwana wa Enani.
84 To su bili prinosi glavara izraelskih za posvetu žrtvenika na dan kad bijaše pomazan: dvanaest srebrnih zdjela, dvanaest srebrnih kotlića i dvanaest zlatnih posudica.
Zopereka za atsogoleri a Israeli zopatulira guwa lansembe pamene linadzozedwa zinali izi: mbale khumi ndi ziwiri zasiliva, mabeseni owazira asiliva khumi ndi awiri ndi mbale zagolide khumi ndi ziwiri.
85 Svaka srebrna zdjela težila je sto trideset šekela; svaki kotlić sedamdeset šekela. Svega srebra u posuđu bilo je dvije tisuće i četiri stotine hramskih šekela.
Mbale iliyonse yasiliva inkalemera kilogalamu imodzi ndi theka, ndipo beseni lililonse lowazira linkalemera magalamu 800. Pamodzi, mbale zonse zasiliva zinkalemera makilogalamu 27 monga mwa muyeso wa ku malo opatulika.
86 Zlatnih posudica punih tamjana bilo je dvanaest, svaka posudica težila je deset hramskih šekela. Sve zlato u posudicama težilo je sto dvadeset šekela.
Mbale khumi ndi ziwiri zagolide zodzaza ndi lubanizo zinkalemera magalamu 110 iliyonse, monga mwa muyeso wa ku malo opatulika. Pamodzi, mbale zagolide zinkalemera kilogalamu imodzi ndi theka.
87 Sve stoke za paljenicu: dvanaest junaca, dvanaest ovnova, dvanaest jednogodišnjih janjaca s njihovim prinosima. Za okajnicu dvanaest jaraca.
Chiwerengero cha nyama zonse za nsembe yopsereza chinali motere: ngʼombe zazimuna khumi ndi ziwiri, nkhosa zazimuna khumi ndi ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi awiri a chaka chimodzi pamodzi ndi chopereka chachakudya. Mbuzi zazimuna khumi ndi ziwiri zinali za nsembe yopepesera machimo.
88 Sve stoke za pričesnicu: dvadeset i četiri vola, šezdeset ovnova, šezdeset kozlića i šezdeset janjaca od godine dana. To je bio prinos za posvetu žrtvenika pošto bijaše pomazan.
Chiwerengero cha nyama zonse za nsembe yachiyanjano chinali motere: ngʼombe zothena 24, nkhosa zazimuna 60, mbuzi zazimuna 60 ndi ana ankhosa aamuna a chaka chimodzi 60. Zimenezi ndi zimene zinali zopereka zopatulira guwa lansembe litadzozedwa.
89 Kad bi Mojsije ulazio u Šator sastanka da razgovara s Njim, slušao bi glas kako mu govori ozgo s Pomirilišta što je bilo na Kovčegu svjedočanstva, među dva kerubina. Tada bi mu govorio.
Mose atalowa mu tenti ya msonkhano kukayankhula ndi Yehova, anamva mawu kuchokera pakati pa Akerubi awiri amene anali pamwamba pa chivundikiro cha bokosi la umboni. Ndipo anayankhula naye.