< Brojevi 4 >
1 Jahve reče Mojsiju i Aronu:
Yehova anati kwa Mose ndi Aaroni:
2 “Izdvojite između sinova Levijevih glavare Kehatovih sinova po rodovima i porodicama njihovim:
“Werengani Akohati omwe ndi gawo limodzi la Alevi monga mwa mafuko awo ndi mabanja awo.
3 od trideset godina naviše, sve do pedeset godina - sve koji mogu ući u red da vrše službe u Šatoru sastanka.
Werengani amuna onse amene ali ndi zaka makumi atatu mpaka zaka makumi asanu amene amabwera kudzagwira ntchito mu tenti ya msonkhano.
4 A služba je Kehatovih sinova u Šatoru sastanka: briga za svetinje nad svetinjama.
“Ntchito ya Akohati mu tenti ya msonkhano ndi iyi: kusamalira zinthu zopatulika kwambiri.
5 Kad se tabor diže na put, neka uđu Aron i njegovi sinovi te skinu zaštitnu zavjesu i njom pokriju Kovčeg svjedočanstva.
Pamene anthu akusamuka pa msasa, Aaroni ndi ana ake aamuna azilowa mu tenti ndi kuchotsa chinsalu chotchingira ndi kuphimba nacho bokosi la umboni.
6 Neka onda na nj stave pokrivalo od fine kože, a po njemu neka razastru platno, potpuno ljubičasto. Potom neka Kovčegu namjeste motke.
Ndipo azikuta bokosilo ndi zikopa za akatumbu ndi kuyala pamwamba pake nsalu ya mtundu wa thambo ndi kuyika mitengo yonyamulira mʼmalo mwake.
7 Po stolu prinošenja neka prostru ljubičasto platno. Onda neka na nj stave zdjele, žlice, krčage i vrčeve za ljevanice. Kruh neprekidnog prinošenja neka također bude na njemu.
“Pa tebulo pamene pamakhala buledi wa ansembe aziyalapo nsalu ya mtundu wa thambo, ndipo aziyikapo mbale, mabeseni, zipande ndi mitsuko yoperekera nsembe yachakumwa. Aziyikaponso buledi wokhala pamenepo nthawi zonse.
8 To neka prekriju tamnocrvenim platnom, a preko njega neka prebace pokrivalo od fine kože. Potom neka stolu namjeste motke.
Tsono pamwamba pa izi aziyalapo nsalu yofiira, ndi kuzikuta mʼzikopa za akatumbu ndi kuyika mitengo yonyamulira mʼmalo mwake.
9 Neka zatim uzmu ljubičasto platno i pokriju svijećnjak za svjetlo i njegove svjetiljke, njegove usekače, njegove lugare i sve posude za ulje kojima se ono poslužuje.
“Azitenga nsalu ya mtundu wa thambo ndi kukutira choyikapo nyale, pamodzi ndi nyale zake, zopanira zake, zotengera zake ndi mitsuko yonse yosungiramo mafuta.
10 Neka ga stave sa svim njegovim priborom na pokrivalo od fine kože pa polože na nosiljku.
Kenaka achikulunge pamodzi ndi zipangizo zake zonse mʼzikopa za akatumbu ndi kuchiyika pa chonyamulira chake.
11 Po zlatnom žrtveniku neka razastru ljubičasto platno i prekriju ga pokrivalom od fine kože. Potom neka mu namjeste motke.
“Pamwamba pa guwa la golide aziyalapo nsalu ya mtundu wa thambo ndi kukutira ndi zikopa za akatumbu ndi kuyika mʼmalo mwake mitengo yonyamulira.
12 Neka sad uzmu sav pribor što se upotrebljava za službu u Svetištu pa ga stave na ljubičasto platno i onda prekriju pokrivačem od fine kože. Zatim neka sve to polože na nosiljku.
“Azitenga zipangizo zonse zogwiritsira ntchito ku malo wopatulika, azizikulunga mʼnsalu ya mtundu wa thambo, azizikuta ndi zikopa za akatumbu ndi kuziyika pa zonyamulira zake.
13 Neka pometu pepeo sa žrtvenika i po njemu razastru crveno platno.
“Azichotsa phulusa la pa guwa lansembe lamkuwa ndi kuyalapo nsalu yapepo pamwamba pake.
14 Na nj neka postave sav pribor što se upotrebljava za službu: kadionike, viljuške, lopatice i zdjele - sve posuđe za žrtvenik. Po njemu onda neka razastru pokrivalo od fine kože. Zatim neka namjeste motke.
Kenaka aziyikapo zipangizo zonse zogwiritsira ntchito potumikira pa guwa, kuphatikizapo miphika yowotchera nyama, mafoloko otengera nyama, zowolera phulusa ndi mbale zowazira magazi pa guwa lansembe ndipo pamwamba pake aziyalapo zikopa za akatumbu ndi kuziyika mʼzonyamulira zake.
15 Pošto Aron i njegovi sinovi završe pokrivanje Svetišta i svega svetog posuđa, u času kad imadne tabor krenuti na put, neka dođu potomci Kehatovi da to ponesu. No svetih se predmeta ne smiju doticati da ne poginu. To je dužnost Kehatovih potomaka u Šatoru sastanka.
“Aaroni ndi ana ake aamuna akamaliza kukutira ziwiya za ku malo wopatulika ndi zipangizo zopatulika zonse, ndipo akakonzeka kusamuka pamalopo, Akohati abwere kudzazinyamula koma asagwire zinthu zopatulikazo. Akatero adzafa. Izi ndizo zinthu zimene Akohati ayenera kunyamula mu tenti ya msonkhano.
16 A Eleazar, sin svećenika Arona, neka se brine za ulje svijećnjaka, za mirisni kad, za trajnu prinosnicu i za ulje pomazanja; neka se brine za sve Prebivalište, za sve što je u njemu - za Svetište i njegovo posuđe.”
“Eliezara mwana wa Aaroni, wansembe, aziyangʼanira mafuta a nyale, ndi lubani wa nsembe zofukiza, nsembe yaufa yoperekedwa nthawi zonse ndi mafuta odzozera. Aziyangʼaniranso chihema ndi zonse zili mʼmenemo, kuphatikizapo zida ndi ziwiya zonse zopatulika.”
17 Jahve reče Mojsiju i Aronu:
Yehova anawuzanso Mose ndi Aaroni kuti,
18 “Ne dopustite da nestane pleme rodova Kehatovih između levita.
“Onetsetsani kuti mabanja a fuko la Kohati asachotsedwe kwa Alevi.
19 Ovako postupajte s njima, da žive i ne izginu primičući se najvećim svetinjama: neka dođu Aron i njegovi sinovi da postave svakoga od njih na njegovu službu i uz njegovu dužnost.
Koma muziwachitira izi kuti asafe, akhalebe ndi moyo pamene ayandikira zinthu za ku malo wopatulika kwambiri: Aaroni ndi ana ake aamuna azipita ku malo wopatulika ndi kumamupatsa munthu aliyense ntchito yake ndi zimene ayenera kunyamula.
20 Oni neka ne ulaze ni da začas pogledaju Svetište da ne bi poginuli.”
Koma Akohati asalowe kukaona zinthu zopatulika, ngakhale kanthawi pangʼono, chifukwa akatero adzafa.”
Yehova anawuza Mose kuti,
22 “Popiši i Geršonove sinove po njihovim porodicama i njihovim rodovima, od trideset godina naviše, sve do pedesete godine;
“Werenganso Ageresoni monga mwa mabanja ndi mafuko awo.
23 popiši ih sve koji mogu ići u red da vrše službu u Šatoru sastanka.
Uwerenge amuna onse a zaka makumi atatu mpaka a zaka makumi asanu zakubadwa amene amabwera kudzatumikira ku tenti ya msonkhano.
24 A ovo je služba rodova Geršonovaca pri radu i prenošenju:
“Ntchito ya mafuko a Ageresoni pamene akugwira ntchito ndi kunyamula katundu ndi iyi:
25 neka nose zavjese Prebivališta, Šator sastanka s njegovim krovom, pokrivalo od fine kože što je povrh njega, i zavjesu na ulazu u Šator sastanka;
Azinyamula makatani a ku chihema, tenti ya msonkhano, zokutira zake ndi zokutira kunja za zikopa za akatumbu, makatani a pa khomo la ku tenti ya msonkhano,
26 onda, dvorišne zavjese, zavjesu s vrata na ulazu u predvorje što opkoljuje Prebivalište i žrtvenik, konopce i sav pribor za njihovu službu; što god treba oko tih stvari raditi, neka učine.
makatani wotchingira bwalo lozungulira chihema ndi guwa, katani ya pa khomo, zingwe ndi zida zonse zimene zimagwiritsidwa ntchito mʼchihema. Ageresoni azichita zonse zofunika kuchitika ndi zinthu zimenezi.
27 Neka Geršonovci obavljaju sve svoje dužnosti - sve što imaju nositi i sve što imaju raditi - po nalogu Arona i njegovih sinova. Njihovoj brizi povjerite sve što treba da nose.
Ntchito yawo yonse, kaya kunyamula kapena kugwira ntchito zina, achite Ageresoni motsogozedwa ndi Aaroni ndi ana ake aamuna. Uwagawire ntchito zonse zimene akuyenera kugwira.
28 To je služba rodova Geršonovaca u Šatoru sastanka. Njihova služba neka bude pod vodstvom Itamara, sina svećenika Arona.”
Iyi ndiye ntchito ya fuko la Ageresoni ku tenti ya msonkhano. Ntchito zawo zichitike motsogozedwa ndi Itamara mwana wa wansembe Aaroni.
29 “Sinove Merarijeve popiši po rodovima i porodicama njihovim.
“Werenga Amerari monga mwa mafuko awo ndi mabanja awo.
30 Popiši ih od trideset godina naviše, sve do pedeset godina, koji mogu ući u red da vrše službu u Šatoru sastanka.
Werenga amuna onse a zaka makumi atatu mpaka zaka makumi asanu zakubadwa amene akatumikire mu tenti ya msonkhano.
31 Za sve njihove službe u Šatoru sastanka dužnost im je da nose trenice za Prebivalište, njegove priječnice, njegove stupce i njegova podnožja;
Ntchito yawo pamene azikatumikira mu tenti ya msonkhano ndi iyi: kunyamula matabwa a chihema, mitanda, mizati ndi matsinde,
32 stupce što okružuju predvorje, njihova podnožja, njihove kočiće, njihove konopce, sa svim priborom za njihovu službu. Poimenično popišite predmete što su im povjereni da ih nose.
ndiponso mizati yozungulira bwalo ndi matsinde ake, zikhomo za chihema, zingwe ndi zipangizo zake zonse ndiponso zonse zokhudzana ndi ntchito yake. Uwuze munthu aliyense chomwe ayenera kuchita.
33 To je služba rodova Merarijevaca u svemu što imaju činiti u Šatoru sastanka pod vodstvom Itamara, sina svećenika Arona.”
Iyi ndiyo ntchito ya mafuko a Amerari pamene akugwira ntchito ku tenti ya msonkhano motsogozedwa ndi Itamara mwana wa wansembe Aaroni.”
34 Mojsije, Aron i glavari zajednice popisali su Kehatove sinove po njihovim rodovima i porodicama -
Mose, Aaroni ndi atsogoleri a magulu a anthu anawerenga Akohati monga mwa mafuko ndi mabanja awo.
35 sve koji mogu ući u red da vrše službu u Šatoru sastanka, od trideset godina naviše, sve do pedeset godina.
Aamuna onse a zaka makumi atatu mpaka makumi asanu amene anabwera kudzagwira ntchito ku tenti ya msonkhano,
36 I popisanih po njihovim rodovima bijaše dvije tisuće sedam stotina i pedeset.
atawawerenga mwa mafuko awo, anali 2,750.
37 To je popis rodova Kehatovaca, svih koji su služili u Šatoru sastanka, a koje popisa Mojsije i Aron na zapovijed što je Jahve dade Mojsiju.
Ichi chinali chiwerengero cha mafuko a Akohati onse omwe ankatumikira mu tenti ya msonkhano. Mose ndi Aaroni anawawerenga monga mwa lamulo la Yehova.
38 Popisanih sinova Geršonovih po njihovim rodovima i porodicama,
Ageresoni anawerengedwanso monga mwa mafuko ndi mabanja awo.
39 od trideset godina naviše, sve do pedeset godina, svih koji mogu ući u red da vrše službu u Šatoru sastanka -
Amuna onse a zaka makumi atatu mpaka makumi asanu amene anabwera kudzagwira ntchito ku tenti ya msonkhano,
40 popisanih, dakle, po njihovim rodovima i porodicama bijaše dvije tisuće šest stotina i pedeset.
atawawerenga mwa mafuko ndi mabanja awo, anali 2,630.
41 To je popis rodova Geršonovaca, svih koji su služili u Šatoru sastanka, a koje popisa Mojsije i Aron na Jahvinu zapovijed.
Ichi chinali chiwerengero cha Ageresoni mwa mabanja awo amene ankatumikira ku tenti ya msonkhano. Mose ndi Aaroni anawawerenga monga mwa lamulo la Yehova.
42 Popis rodova Merarijevih sinova po njihovim rodovima i porodicama,
Amerari anawawerenga monga mwa mafuko ndi mabanja awo.
43 od trideset godina naviše, sve do pedeset godina, svih koji mogu ući u red da vrše službu u Šatoru sastanka -
Amuna onse kuyambira zaka makumi atatu mpaka makumi asanu amene anabwera kudzatumikira ntchito mu tenti ya msonkhano,
44 popisanih, dakle, po njihovim rodovima bijaše tri tisuće dvjesta.
atawawerenga mwa mafuko ndi mabanja awo, anali 3,200.
45 To je popis Merarijevaca što su ga sastavili Mojsije i Aron na zapovijed koju je Jahve dao Mojsiju.
Ichi ndicho chinali chiwerengero cha mabanja a Amerari. Mose ndi Aaroni anawawerenga monga momwe Yehova anawalamulira kudzera mwa Mose.
46 Svih, dakle, popisanih levita koje su popisali Mojsije, Aron i glavari izraelski po njihovim rodovima i porodicama, od trideset godina naviše do pedeset godina -
Kotero Mose, Aaroni ndi atsogoleri a Israeli anawerenga Alevi onse monga mwa mafuko ndi mabanja awo.
47 svih koji su ušli u službu posluživanja i službu prenošenja u Šatoru sastanka -
Aamuna onse a zaka makumi atatu mpaka zaka makumi asanu omwe anabwera kudzagwira ntchito yonyamula zinthu ku tenti ya msonkhano
48 bilo je osam tisuća pet stotina i osamdeset.
analipo 8,580.
49 Na zapovijed koju je Jahve dao Mojsiju svakoga su unijeli u popis prema onom u čemu je služio i što je prenosio. Popisali su ih kako je Jahve zapovjedio Mojsiju.
Aliyense anamupatsa ntchito ndi kumuwuza choti anyamule monga mwa lamulo la Yehova kudzera mwa Mose. Anawawerenga chomwechi potsata zimene Yehova analamula Mose.