< Brojevi 30 >

1 Zatim reče Mojsije glavarima plemena Izraelovih: “Ovo je Jahve naredio.
Mose anawuza Aisraeli onse zonse zimene Yehova anamulamula. Iye anati, “Zimene Yehova walamula ndi izi:
2 Ako koji čovjek učini zavjet ili se uz zakletvu obveže da će se nečega odreći, neka ne krši svoje riječi; neka izvrši sve što iz njegovih usta izađe!
Munthu wamwamuna ngati walonjeza kwa Yehova kapena kulumbira kuti adzachita zimene walumbirazo, asaphwanye mawuwo koma ayenera kuchita chilichonse chimene wanena.
3 Ako koja žena učini Jahvi zavjet ili se obveže da će se nečega odreći dok je još mlada, u očevu domu,
“Pamene munthu wamkazi amene akukhalabe mʼnyumba ya abambo ake alumbira kwa Yehova kuti adzachita zimene walonjeza pa ubwana wake,
4 a otac joj sazna za zavjet i obećanje kojim se obvezala pa joj ništa ne rekne, tada su valjani svi njezini zavjeti i valjano je svako obećanje kojim se obvezala.
abambo ake namva kulumbira kwakeko kapena kulonjeza kwake kuti adzachitadi, ndipo abambo akewo wosayankhula kanthu, mkaziyo achitedi zomwe analumbirazo. Ayenera kudzachita zonse zimene walonjeza zija.
5 Ali ako joj se otac usprotivi kad sazna, nikakav njezin zavjet ni njezino obećanje kojim se vezala ne vrijedi. Jahve će joj oprostiti jer joj se otac usprotivio.
Koma ngati abambo akewo amva kulumbira kwake ndi kumukaniza, palibe lamulo lomukakamiza mkaziyo kuchita zimene walonjeza. Yehova adzamukhululukira chifukwa abambo ake anamukaniza.
6 Ako se uda dok je pod svojim zavjetima ili pod obećanjem koje je nepromišljeno izišlo iz njezinih usta,
“Ngati akwatiwa atalumbira kale kapena ngati alonjeza mofulumira ndi pakamwa pake,
7 pa njezin muž sazna i pošto je saznao ništa joj ne rekne, tada vrijede njezini zavjeti i vrijede obećanja kojima se obvezala.
mwamuna wake ndi kumva kulumbira kwakeko koma wosanenapo kanthu, mkaziyo achitedi zomwe walumbirazo. Achite ndithu zomwe walonjeza zija.
8 No ako se njezin muž usprotivi kad o tom sazna, ukida se time njezin zavjet i obećanje što je nepromišljeno izišlo iz njezinih usta. I Jahve će joj oprostiti.
Koma ngati mwamuna wake amuletsa atamva kulumbira kwakeko, pamenepo amumasula mayiyo ku zimene analumbira komanso ku zimene analonjeza mosaganiza bwinozo ndipo Yehova adzamukhululukira.
9 A zavjet udovice ili žene otpuštene i sve obveze koje je na se preuzela vrijede za nju.
“Mayi wamasiye kapena wosiyidwa ukwati akalumbira kapena kulonjeza kuti adzachita kanthu kalikonse, ayenera kukachitadi.
10 Ako se zavjetuje ili se obveže zakletvom na obećanje dok je u kući svoga muža,
“Koma ngati mayi wokwatiwa alumbira nalonjeza kuti adzachitadi zimene walonjeza,
11 pa njezin muž sazna i ništa joj ne rekne, ne usprotivi joj se, svaki je njezin zavjet valjan i valjano je svako obećanje kojim se obvezala.
mwamuna wake ndi kumva kulumbira kwakeko koma osayankhulapo kanthu, osamuletsa, ayenera kuchitadi zonse zimene walumbira ndi zonse zimene walonjeza.
12 Ali ako ih njezin muž proglasi ništetnim kad o njima sazna, tada ništa što je izišlo iz njezinih usta, njezini zavjeti ili preuzete obveze neće vrijediti. Muž ih je njezin poništio, i Jahve će joj oprostiti.
Koma ngati mwamuna wake amva ndi kumuletsa kuti asachite zomwe walumbirazo, palibe lamulo lomukakamiza mayiyo kuchita zomwe walumbirazo kapenanso zimene walonjeza. Popeza mwamuna wake wamuletsa, Yehova adzamukhululukira mayiyo.
13 Svaki zavjet i svaku zakletvu koja obvezuje ženu na neko mrtvenje njezin muž može uzdržati na snazi ili poništiti.
Mwamuna wake ali ndi mphamvu zovomereza kapena kukana zimene mayiyo walumbira kapena zimene walonjeza zokhudza kudzilanga yekha.
14 Ako joj muž od dana do dana ništa ne rekne, time potvrđuje sve njezine zavjete i sva njezina obećanja kojima se obvezala; on ih je učinio valjanima ako ništa nije rekao kad je o njima čuo.
Ndipo ngati mmawa mwake ndi masiku otsatira mwamuna wake sanenapo kanthu atamva zimenezi, mayiyo achitedi zimene walumbira kapena zimene walonjeza. Mwamunayo wavomereza zimenezo, chifukwa sanamuwuze kanthu mayiyo pa tsiku limene anamva akulonjeza kapena kulumbira.
15 Ali ako ih poništi kasnije, pošto je o njima već čuo, neka snosi njezinu krivnju.”
Koma ngati mwamunayo amukaniza patapita kanthawi atazimva kale, iyeyo ndiye wochimwa mʼmalo mwa mayiyo.”
16 To su uredbe koje je Jahve Mojsiju izdao za muža i njegovu ženu i za oca i njegovu kćer, koja, još mlada, živi u kući očevoj.
Awa ndiwo malamulo amene Yehova analamula Mose za mwamuna ndi mkazi wake, ndiponso abambo ndi mwana wawo wamkazi amene akanali mtsikana wokhalabe mʼnyumba ya abambo akewo.

< Brojevi 30 >