< Brojevi 13 >
Yehova anawuza Mose kuti,
2 “Pošalji ljude, po jednoga čovjeka iz pojedinog pradjedovskog plemena, da izvide kanaansku zemlju, koju dajem Izraelcima. Pošaljite sve njihove glavare!”
“Tuma anthu kuti akazonde dziko la Kanaani limene ndikupereka kwa Aisraeli. Kuchokera pa fuko lililonse utume munthu mmodzi amene ndi mtsogoleri wawo.”
3 Na Jahvinu zapovijed Mojsije ih posla iz pustinje Parana. Svi ti ljudi bijahu glavari Izraelaca.
Monga mwa mawu a Yehova, Mose anawatuma kuchokera ku chipululu cha Parani. Onsewo anali atsogoleri a Aisraeli.
4 A ovo su njihova imena: Šamua, sin Zakurov, od plemena Rubenova;
Mayina awo ndi awa: kuchokera ku fuko la Rubeni, Samuwa mwana wa Zakuri;
5 Šafat, sin Horijev, od plemena Šimunova;
kuchokera ku fuko la Simeoni, Safati mwana wa Hori;
6 Kaleb, sin Jefuneov, od plemena Judina;
kuchokera ku fuko la Yuda, Kalebe mwana wa Yefune;
7 Jigal, sin Josipov, od plemena Jisakarova;
kuchokera ku fuko la Isakara, Igala mwana wa Yosefe;
8 Hošea, sin Nunov, od plemena Efrajimova;
kuchokera ku fuko la Efereimu, Hoseya mwana wa Nuni;
9 Palti, sin Rafuov, od plemena Benjaminova;
kuchokera ku fuko la Benjamini, Paliti mwana wa Rafu;
10 Gadiel, sin Sodijev, od plemena Zebulunova;
kuchokera ku fuko la Zebuloni, Gadieli mwana wa Sodi;
11 Gadi, sin Susijev, od plemena Josipova, od plemena Manašeova;
kuchokera ku fuko la Manase (fuko la Yosefe), Gadi mwana wa Susi;
12 Amiel, sin Gemalijev, od plemena Danova;
kuchokera ku fuko la Dani, Amieli mwana wa Gemali;
13 Setur, sin Mikaelov, od plemena Ašerova;
kuchokera ku fuko la Aseri, Seturi mwana wa Mikayeli;
14 Nahbi, sin Vofsijev, od plemena Naftalijeva;
kuchokera ku fuko la Nafutali, Naabi mwana wa Vofisi;
15 Geuel, sin Makijev, od plemena Gadova.
kuchokera ku fuko la Gadi, Geuweli mwana wa Maki.
16 To su imena ljudi koje je Mojsije poslao da izvide zemlju. A Hošeu, sina Nunova, Mojsije prozva Jošuom.
Amenewa ndiwo mayina a anthu amene Mose anawatuma kukazonda dzikolo. (Hoseya mwana wa Nuni, Mose anamupatsa dzina loti Yoswa).
17 Posla ih Mojsije da izvide kanaansku zemlju pa im reče: “Idite gore u Negeb, onda se popnite na brdo.
Mose atawatuma kuti akazonde Kanaani anati, “Mupite kudzera ku Negevi, mukapitirire mpaka ku dziko la mapiri.
18 Razgledajte zemlju kakva je. Je li narod koji u njoj živi jak ili slab, malobrojan ili mnogobrojan?
Mukaone dzikolo kuti ndi lotani ndi anthu okhala mʼmenemo ngati ndi amphamvu kapena ofowoka, ochepa kapena ambiri.
19 Kakva je zemlja u kojoj živi: dobra ili rđava? Kakvi su gradovi u kojima borave: otvoreni ili utvrđeni?
Nanga dziko limene akukhalako ndi lotani? Ndi labwino kapena loyipa? Mizinda imene akukhalamo ndi yotani? Kodi ilibe malinga kapena ndi ya malinga?
20 Kakvo je tlo: plodno ili mršavo? Ima li po njemu drveća ili nema? Odvažni budite i ponesite plodova te zemlje.” Bilo je upravo vrijeme ranog grožđa.
Nthaka yake ndi yotani? Yachonde kapena yopanda chonde? Kodi dzikolo lili ndi mitengo kapena lilibe mitengo? Mukayesetse kubweretsako zipatso za mʼdzikomo.” (Inali nthawi yamphesa zoyamba kupsa).
21 Odu oni gore da izvide zemlju od pustinje Sina do Rehoba, koji je na ulazu u Hamat.
Choncho anapita kukazonda dzikolo kuchokera ku chipululu cha Zini mpaka ku Rehobu, mopenyana ndi Lebo Hamati.
22 Popnu se u Negeb i dođu do Hebrona, gdje su se nalazili Ahiman, Šešaj i Talmaj, Anakovi potomci. - Hebron je osnovan sedam godina prije nego Soan u Egiptu. -
Anapita kudzera ku Negevi ndi kukafika ku Hebroni, kumene Ahimani, Sesai ndi Talimai, ana a Anaki ankakhala. (Anamanga Hebroni zaka zisanu ndi ziwiri asanamange Zowani ku Igupto).
23 Kada stigoše u Dolinu Eškol, odrezaše ondje lozu s grozdom i ponesoše ga, udvoje, na motki; ponesoše i mogranja i smokava.
Atafika ku chigwa cha Esikolo, anadulako nthambi ya mpesa ya phava limodzi la mphesa ndipo anthu awiri ananyamulizana, natenganso makangadza ndi nkhuyu.
24 Ono se mjesto prozva Dolina Eškol zbog grozda koji su ondje Izraelci odrezali.
Malo amenewo anawatcha chigwa cha Esikolo chifukwa cha phava la mphesa limene Aisraeli anadula kumeneko.
25 Nakon četrdeset dana vrate se iz zemlje koju su izviđali.
Patapita masiku makumi anayi, anthu aja anabwerako kokazonda dziko lija.
26 Odu k Mojsiju i Aronu i svoj izraelskoj zajednici u Kadeš, u Paranskoj pustinji. Podnesu njima i svoj zajednici izvještaj, a onda im pokažu plodove zemlje.
Ndipo atabwerako anapita kwa Mose ndi Aaroni ndi kwa Aisraeli onse ku Kadesi mʼchipululu cha Parani. Kumeneko anafotokozera anthu onse nawaonetsanso zipatso za mʼdzikolo.
27 Izvijeste ga oni: “Išli smo u zemlju u koju si nas poslao. Zaista njome teče med i mlijeko. Evo njezinih plodova.
Anthuwo anafotokozera Mose kuti, “Tinapita ku dziko komwe munatituma. Dzikolo ndi loyenda mkaka ndi uchi ndipo zipatso zake ndi izi.
28 Ali je jak narod koji u onoj zemlji živi, gradovi su utvrđeni i vrlo veliki. A vidjesmo ondje i potomke Anakove.
Koma anthu amene amakhala mʼdzikomo ndi amphamvu, mizinda yawo ndi ya malinga aakulu kwambiri. Tinaonanso Aanaki kumeneko.
29 Amalečani borave u negepskom kraju: Hetiti, Jebusejci i Amorejci žive u brdu; a Kanaanci se nalaze uz more i duž Jordana.”
Aamaleki amakhala ku Negevi, Ahiti, Ayebusi ndi Aamori amakhala mʼdziko la mapiri ndipo Akanaani amakhala pafupi ndi nyanja, mʼmbali mwa Yorodani.”
30 Kaleb ušutka narod oko Mojsija i progovori: “Krenimo ne oklijevajući i zauzmimo je, jer je možemo nadvladati!”
Koma Kalebe anawakhalitsa chete anthuwo pamaso pa Mose, ndipo anati, “Tiyeni tipite ndithu ndi kutenga dzikolo, pakuti tingathe kulitenga.”
31 Ali ljudi što su s njim išli odvratiše: “Ne možemo ići na onaj narod jer je jači od nas.”
Koma anthu aja amene anapita naye anati, “Sitingathe kulimbana ndi anthuwo popeza ndi amphamvu kuposa ifeyo.”
32 I počnu ozloglašivati Izraelcima zemlju koju su izviđali: “Zemlja kroz koju smo prošli da je izvidimo zemlja je što proždire svoje stanovništvo. Sav narod što ga u njoj vidjesmo ljudi su krupna stasa.
Choncho anthuwo anafalitsa pakati pa Aisraeli mbiri yoyipa ya dziko lomwe anakalionalo. Iwo anati, “Dziko limene tinapita kukalizonda limawononga anthu okhala mʼmenemo. Ndipo anthu onse amene tinakawaona kumeneko ndi ataliatali.
33 Vidjesmo ondje i divove - Anakovo potomstvo od divova. Činilo nam se da smo prema njima kao skakavci. Takvi bijasmo i njima.”
Kumeneko tinaona Anefili (ana a Aanaki ochokera kwa Nefili). Ifeyo timangodziona ngati ziwala mʼmaso mwawo, ndipo kwa iwo timaonekadi motero ndithu.”