< Mihej 2 >
1 Teško onima koji smišljaju nedjelo i snuju zlo na posteljama svojim! Kad svane dan, oni ga izvrše, jer je sila u njihovoj ruci.
Tsoka kwa amene amakonzekera chiwembu, kwa amene amakonzekera kuchita zoyipa usiku pa mabedi awo! Kukacha mmawa amakachitadi chifukwa ali ndi mphamvu zochitira zimenezo.
2 Zažele li polja, otimaju ih, i kuće, uzimaju ih; čine nasilje čovjeku i kući njegovoj, vlasniku i posjedu njegovu.
Amasirira minda ndi kuyilanda, amasirira nyumba ndi kuzilanda. Amatenga nyumba ya munthu mwachinyengo, munthu mnzawo kumulanda cholowa chake.
3 Zato ovako govori Jahve: “Evo tome rodu smišljam zlo iz kojega nećete izvući vratova, niti ćete hoditi ponosito, jer će biti zlo vrijeme.
Nʼchifukwa chake Yehova akuti, “Ine ndikukonzekera kubweretsa tsoka pa anthu awa, tsoka limene simudzatha kudzipulumutsa nokha. Inu simudzayendanso monyada, pakuti idzakhala nthawi ya masautso.
4 U onaj će vam se dan složiti rugalica, zapjevati tužaljka i reći: 'Propalo je! Posve smo opustošeni, baština je naroda moga otuđena i nitko da mu je vrati, naša polja podijeljena su odmetniku.'
Tsiku limenelo anthu adzakuchitani chipongwe; adzakunyogodolani ndi nyimbo iyi yamaliro: ‘Tawonongeka kotheratu; dziko la anthu anga lagawidwa. Iye wandilanda! Wapereka minda yathu kwa anthu otiwukira.’”
5 Zato neće biti nikoga tko bi bacio kocku za dio tvoj u zboru Jahvinu.”
Nʼchifukwa chake simudzakhala ndi munthu mu msonkhano wa Yehova kuti agawe dziko pochita maere.
6 “Ne balite!” - bale oni - “Tako se ne bali! Sramota na nas neće pasti!
Aneneri awo amanena kuti, “Usanenere! Usanenere ndi pangʼono pomwe zimenezi; ife sitidzachititsidwa manyazi.”
7 Zar će biti proklet dom Jakovljev? Zar je Jahve izgubio strpljivost? Zar on tako postupa? Nisu li riječi njegove ugodne Izraelu, narodu njegovu?”
Inu nyumba ya Yakobo, monga zimenezi ndi zoyenera kuzinena: “Kodi Mzimu wa Yehova wakwiya? Kodi Iye amachita zinthu zotere?” “Kodi mawu ake sabweretsa zabwino kwa amene amayenda molungama?
8 Vi se sami dižete kao neprijatelji narodu mojemu. Čovjeku nezazornu vi otimate kabanicu, onome koji bez straha putuje ratne strahote dosuđujete.
Posachedwapa anthu anga andiwukira ngati mdani. Mumawavula mkanjo wamtengowapatali anthu amene amadutsa mosaopa kanthu, monga anthu amene akubwera ku nkhondo.
9 Vi izgonite žene moga naroda iz njihovih milih domova; djeci njihovoj zauvijek oduzimate slavu koju sam im dao:
Mumatulutsa akazi a anthu anga mʼnyumba zawo zabwino. Mumalanda ana awo madalitso anga kosatha.
10 “Ustanite, idite! Ovo nije počivalište! Zbog nečistoće teško vas uže svezalo.”
Nyamukani, chokani! Pakuti ano si malo anu opumulirapo, chifukwa ayipitsidwa, awonongedwa, sangatheke kuwakonzanso.
11 Kad bi mogao biti nadahnut čovjek koji izmišlja ovu opsjenu: “Prorokujem ti vino i piće”, on bi bio prorok narodu ovome.
Ngati munthu wabodza ndi wachinyengo abwera nʼkunena kuti, ‘Ine ndidzanenera ndipo mudzakhala ndi vinyo ndi mowa wambiri, woteroyo adzakhala mneneri amene anthu awa angamukonde!’
12 Svega ću te sabrati, Jakove, sakupit ću Ostatak Izraelov! Smjestit ću ih zajedno kao ovce u toru, kao stado na paši - neće se bojati nikoga.
“Inu banja la Yakobo, ndidzakusonkhanitsani nonse; ndidzawasonkhanitsa pamodzi otsala a ku Israeli. Ndidzawabweretsa pamodzi ngati nkhosa mʼkhola, ngati ziweto pa msipu wake; malowo adzadzaza ndi chinamtindi cha anthu.
13 Pred njima stupa rušilac: oni će se porušiti i ući, kroz vrata će proći i izaći; pred njima će ići njihov kralj, Jahve će biti na čelu.
Amene adzawapulumutse adzayenda patsogolo pawo; iwo adzathyola chipata ndipo adzatuluka. Mfumu yawo idzawatsogolera, Yehova adzakhala patsogolo pawo.”