< Levitski zakonik 5 >

1 “Zgriješi li tko tako što čuje riječi proklinjanja a odbije da svjedoči iako je mogao biti svjedokom jer je ili sam vidio ili doznao pa tako nosi krivnju na sebi;
“‘Ngati munthu anayitanidwa ku bwalo kuti akachitire umboni pa zimene anaziona kapena kuzimva koma iye nʼkukana kuchitira umboni, munthu ameneyo wachimwa ndipo ayenera kulangidwa.
2 ili ako tko dirne kakav nečist predmet, strv nečiste zvijeri, strv nečista živinčeta ili strv nečista puzavca - i u neznanju postane nečist i odgovoran;
“‘Munthu akakhudza chinthu chilichonse chodetsedwa, monga nyama yakufa ya mʼthengo, kapena chiweto chakufa kapenanso chokwawa chakufa, ngakhale iyeyo wachikhudza mosadziwa, wasanduka wodetsedwa ndipo wachimwa.
3 ili kad se tko dotakne nečistoće čovječje, bilo to što mu drago od čega se nečistim postaje i toga ne bude svjestan, kad dozna, biva odgovoran;
“‘Munthu akakhudza choyipitsa munthu cha mtundu uliwonse, ndipo pochikhudzapo ndi kuyipitsidwa nacho mosadziwa, munthuyo adzakhala wopalamula akangodziwa chimene wachitacho.
4 nadalje, kad tko nepromišljeno izusti zakletvu na dobro ili zlo - na što se već čovjek nepromišljeno zaklinje - i toga ne bude svjestan, onda, kad dozna, biva odgovoran;
“‘Munthu akalumbira mofulumira kapena mosasamala kuti adzachita chinthu, choyipa kapena chabwino, ngakhale kuti wachita izi mosadziwa kuti nʼkulakwa, pamene wazindira kulakwa kwake, iye adzakhalabe wopalamula akangodziwa chimene wachitacho.
5 ako, dakle, tko postane odgovoran u bilo čemu od toga, neka prizna počinjeni grijeh.
“‘Pamene munthu wazindikira kuti wachimwa motere, awulule tchimo limene wachitalo.
6 I neka prinese Jahvi kao žrtvu naknadnicu za počinjeni grijeh jednu ženku od sitne stoke, janje ili kozle, kao žrtvu okajnicu. Neka svećenik izvrši nad njim obred pomirenja koji će ga osloboditi od njegova grijeha.”
Pambuyo pake, munthuyo abwere kwa Yehova ndi mwana wankhosa wamkazi kapena mbuzi kuti ikhale chopereka chopepesera tchimo ndipo wansembe achite mwambo wopepesera tchimo lomwe wachitalo. Tsono wansembe achite mwambo wopepesera tchimo la munthuyo.
7 “Ako mu sredstva ne dopuštaju da pribavi glavu sitne stoke, neka Jahvi, kao naknadnicu za počinjeni grijeh, prinese dvije grlice ili dva golubića; jedno kao žrtvu okajnicu, a drugo kao žrtvu paljenicu.
“‘Ngati munthuyo alibe mwana wankhosa, abweretse njiwa ziwiri kapena nkhunda ziwiri kwa Yehova ngati chopereka chopepesera tchimo lake. Imodzi ikhale nsembe yopepesera tchimo, ndipo inayo ikhale nsembe yopsereza.
8 Neka ih donese svećeniku, a on neka najprije prinese ono što je određeno kao žrtva okajnica. Stisnuvši ga za vrat, neka mu slomi šiju, ali neka glave ne otkida.
Tsono abwere nazo kwa wansembe, ndipo wansembeyo ayambe wapereka mbalame imodzi ngati yopepesera tchimo. Apotole khosi koma osayidula mutu,
9 Neka krvlju žrtve poškropi žrtvenik sa strane, a ostatak krvi neka se iscijedi podno žrtvenika. To je žrtva okajnica.
kenaka awaze magazi a chopereka chopepesera tchimocho mʼmbali mwa guwa. Magazi ena onse awathire pa tsinde la guwa. Imeneyi ndi nsembe yopepesera tchimo.
10 Onda neka drugo prinese kao žrtvu paljenicu prema propisu. Neka tako svećenik nad tim čovjekom izvrši obred pomirenja za grijeh koji je počinio, i bit će mu oprošteno.
Pambuyo pake wansembe apereke mbalame inayo kuti ikhale chopereka chopsereza potsata mwambo wake. Wansembe atatha kupereka nsembe yopepesera tchimo limene munthu uja wachita, wochimwayo adzakhululukidwa.
11 Ako mu sredstva ne dopuštaju da pribavi dvije grlice ili dva golubića, neka Jahvi, u zadovoljštinu za počinjeni grijeh, prinese jednu desetinu efe njaboljeg brašna. Ulja u nj neka ne ulijeva niti na nj tamjana stavlja jer je žrtva okajnica.
“‘Koma ngati munthuyo alibe njiwa ziwiri kapena nkhunda ziwiri, abweretse ufa wosalala wokwanira kilogalamu imodzi kuti ukhale chopereka chopepesera tchimo limene wachita. Asathiremo mafuta kapena lubani chifukwa ndi chopereka chopepesera tchimo.
12 Kada to donese svećeniku, neka svećenik zagrabi punu pregršt kao spomen-žrtvu i na žrtveniku sažeže u čast Jahvi povrh paljenih žrtava. To je žrtva okajnica.
Abweretse ufawo kwa wansembe ndipo wansembeyo atapeko dzanja limodzi kuti ukhale ufa wachikumbutso ndi kuwutentha pa guwa pamodzi ndi chopereka chopsereza kwa Yehova. Imeneyi ndi nsembe yopepesera tchimo.
13 Neka tako svećenik izvrši nad tim čovjekom obred pomirenja za grijeh koji je počinio u bilo kojem od tih slučajeva, pa će mu biti oprošteno. Ono ostalo neka pripadne svećeniku kao i od žrtve prinosnice.”
Umu ndi mmene wansembe adzachitire mwambo wopepesera machimo ena aliwonse amene munthu wachita, ndipo munthuyo adzakhululukidwa. Zopereka zonse zotsala zidzakhala za wansembeyo monga momwe amachitira ndi chopereka chachakudya.’”
14 Još reče Jahve Mojsiju:
Yehova anawuza Mose kuti,
15 “Ako tko počini pronevjerenje ogriješivši se nehotično o svete stvari Jahvine, neka za naknadu, kao žrtvu naknadnicu, prinese Jahvi, iz svoga stada, ovna bez mane, vrijedna - po tvojoj procjeni - najmanje dva šekela srebra - prema cijeni hramskog šekela.
“Munthu akachita zinthu mosakhulupirika, nachimwa mosadziwa posapereka zinthu zopatulika zofunika kwa Yehova, munthuyo apereke kwa Yehova nsembe yopepesera machimo ake. Nsembeyo ikhale nkhosa yayimuna yopanda chilema ndipo mtengo wake ukhale wokwana masekeli oyenera a siliva pakawerengedwe ka ku Nyumba ya Mulungu. Imeneyi ndi nsembe yopepesera kupalamula.
16 Neka nadoknadi koliko se ogriješio o svete stvari i tome doda još petinu i neka dadne svećeniku. Neka svećenik nad njim izvrši obred pomirenja ovnom žrtve naknadnice, i bit će mu oprošteno.
Munthuyo ayenera kubweza zinthu zopatulika zimene sanaperekezo. Awonjezepo chimodzi mwa zigawo zisanu zilizonse ndi kuzipereka zonsezo kwa wansembe amene adzachita mwambo wopepesera machimo a munthuyo, popereka nkhosa yayimuna ija ngati nsembe yopepesera ndipo wochimwayo adzakhululukidwa.
17 Ako tko i ne znajući pogriješi i učini štogod što je Jahve zabranio, kriv je, pa neka snosi posljedice svoje krivnje.
“Ngati munthu wachimwa mosadziwa pochita chilichonse chimene Yehova salola, munthuyo ndi wopalamula ndithu, ndipo ayenera kulangidwa.
18 Neka svećeniku dovede za naknadnicu iz svoga stada ovna bez mane, prema tvojoj procjeni. Neka svećenik nad tim čovjekom izvrši obred pomirenja za pogrešku što je počinio u neznanju, i bit će mu oprošteno.
Abwere kwa wansembe ndi chopereka chopepesera kupalamula kwake. Chopereka chikhale nkhosa yayimuna yopanda chilema ndipo mtengo wake ukhale woyenera nsembe yopepesera kupalamula kumene anachimwa mosadziwako, ndipo munthuyo adzakhululukidwa.
19 To je žrtva naknadnica; on je doista bio odgovoran Jahvi.”
Imeneyi ndi nsembe yopepesera kupalamula popeza munthuyo wapezeka wolakwa pamaso pa Yehova.”

< Levitski zakonik 5 >