< Levitski zakonik 10 >

1 A sinovi Aronovi Nadab i Abihu uzmu svaki svoj kadionik; stave u nj vatre i na nju metnu tamjana da prinesu pred Jahvom neposvećenu vatru, koju im on ne bijaše propisao.
Ana a Aaroni, Nadabu ndi Abihu, aliyense anatenga chofukizira lubani chake nayikamo makala a moto ndi kuthiramo lubani. Iwo anapereka pamaso pa Yehova moto wachilendo, moto umene Yehova sanawalamule.
2 Ali izbije plamen ispred Jahve te ih proguta - poginuše oni pred Jahvom.
Choncho moto unatuluka pamaso pa Yehova ndi kuwapsereza, ndipo anafa pamaso pa Yehova.
3 Nato će Mojsije Aronu: “To je ono što je Jahve navijestio: Po onima koji su mi blizu svetim ću se pokazati; pred svim ću se pukom proslaviti.” Aron je šutio.
Pamenepo Mose anawuza Aaroni kuti, “Pajatu Yehova ananena kuti, “‘Kwa iwo amene amandiyandikira ndidzaonetsa ulemerero wanga; pamaso pa anthu onse ndidzalemekezedwa.’” Aaroni anakhala chete wosayankhula.
4 Mojsije zovnu Mišaela i Elsafana, sinove Aronova strica Uziela, pa im reče: “Dođite i odnesite svoju braću ispred Svetišta u polje izvan tabora!”
Mose anayitana Misaeli ndi Elizafani, ana a Uzieli, abambo angʼono a Aaroni, ndipo anawawuza kuti, “Bwerani kuno mudzachotse abale anuwa pa malo wopatulika ndi kuwatulutsira kunja kwa msasa.”
5 Oni dođu i odnesu ih u njihovim košuljama u polje izvan tabora, kako je Mojsije rekao.
Choncho anabwera atavala minjiro yawo ndipo anawatenga ndi kuwatulutsa kunja kwa msasawo monga momwe Mose analamulira.
6 Poslije toga Mojsije reče Aronu i njegovim sinovima, Eleazaru i Itamaru: “Ne raščupavajte svoje kose niti razdirite svojih haljina da ne poginete i da se On ne razljuti na svekoliku zajednicu. Vaša braća i sav dom Izraelov neka oplakuje one koje je vatra Jahvina sažegla.
Ndipo Mose anawuza Aaroni ndi ana ake Eliezara ndi Itamara kuti, “Musalileke tsitsi lanu nyankhalala ndipo musangʼambe zovala zanu kuti mungafe, ndi mkwiyo wa Yehova ungagwere anthu onsewa. Koma abale anu okha, kutanthauza fuko lonse la Israeli ndiwo ayenera kulira omwalira aja amene Yehova wawapsereza ndi moto.
7 Ne smijete odlaziti s ulaza u Šator sastanka da ne pomrete, jer na vama je Jahvino ulje pomazanja.” Oni učine po riječi Mojsijevoj.
Musatuluke kunja kwa tenti ya msonkhano, mungafe, chifukwa munadzozedwa ndi mafuta a Yehova kukhala ansembe.” Choncho iwo anachita monga Mose ananenera.
8 Jahve reče Aronu:
Pambuyo pake Yehova anayankhula ndi Aaroni nati,
9 “Kad ulazite u Šator sastanka, nemojte piti vina niti opojnoga pića, ni ti ni tvoji sinovi s tobom! Tako nećete poginuti. To je trajan zakon za vaše naraštaje;
“Iwe ndi ana ako musamamwe vinyo kapena chakumwa chilichonse choledzeretsa pamene mukulowa mu tenti ya msonkhano kuti mungafe. Ili ndi lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse.
10 da možete lučiti posvećeno od običnoga, čisto od nečistoga;
Muzisiyanitsa pakati pa zinthu zopatulika ndi zinthu wamba, pakati pa zinthu zodetsedwa ndi zinthu zoyeretsedwa,
11 da možete učiti Izraelce svim zakonima što ih je Jahve predao preko Mojsija.”
ndipo muyenera kuphunzitsa Aisraeli onse malamulo amene Yehova wakupatsani kudzera mwa Mose.”
12 Onda Mojsije rekne Aronu i njegovim preživjelim sinovima, Eleazaru i Itamaru: “Uzimajte od žrtve prinosnice što preostaje nakon prinesene žrtve u čast Jahvi paljene i beskvasnu je uza žrtvenik jedite jer je vrlo sveta.
Mose anawuza Aaroni ndi ana ake otsalawo, Eliezara ndi Itamara kuti, “Tengani zopereka zachakudya zopanda yisiti zimene zatsala pa nsembe zopsereza za kwa Yehova ndipo muzidye pafupi ndi guwa pakuti ndi zopatulika kwambiri.
13 Blagujte je u svetom mjestu, jer to je - tako je meni naređeno - pristojbina tvoja i pristojbina tvojih sinova od žrtava paljenih u čast Jahvi.
Muzidye pa malo wopatulika chifukwa zimenezi ndi gawo lako ndi la ana ako pa zopereka zopsereza kwa Yehova. Izitu ndi zimene Yehova anandilamulira.
14 A grudi žrtve prikaznice i pleće žrtve podizanice ti i tvoji sinovi i tvoje kćeri s tobom jedite na bilo kojem čistom mjestu. Jer to je dodijeljeno za pristojbinu tebi i tvojim sinovima od izraelskih žrtava pričesnica.
Koma iwe pamodzi ndi ana ako aamuna ndi aakazi muzidya chidale chimene chinaweyulidwa ndi ntchafu zimene zinaperekedwa nsembe. Muzidye pamalo woyeretsedwa. Zimenezi zaperekedwa kwa iwe ndi ana ako monga gawo lanu pa zopereka zachiyanjano zimene apereka Aisraeli.
15 Pleće žrtve podizanice i grudi žrtve prikaznice što se donose zajedno s lojem, na vatri paljenim - pošto budu prineseni za žrtvu prikaznicu pred Jahvom - neka pripadnu tebi i tvojim sinovima s tobom. To je, kako je Jahve naredio, trajan zakon.”
Ntchafu imene inaperekedwayo ndi chidale chomwe chinaweyulidwacho abwere nazo pamodzi ndi nsembe ya mafuta ya Yehova yotentha pa moto, ndipo uziweyule kuti zikhale zopereka zoweyula pamaso pa Yehova. Zimenezi zizikhala zako ndi ana ako nthawi zonse monga walamulira Yehova.”
16 Potom se Mojsije potanje raspita o jarcu žrtve okajnice. Već je bio spaljen. On se razljuti na Eleazara i Itamara, Aronove preživjele sinove, pa rekne:
Pambuyo pake Mose anafunafuna mbuzi ya nsembe yopepesera machimo koma anapeza kuti anayitentha kale. Apa Mose anakalipira Eliezara ndi Itamara, ana a Aaroni otsala aja nati,
17 “Zašto ste jeli žrtvu okajnicu na svetome mjestu? Vrlo ja sveta! To vam je dao Jahve da uklanjate krivnju sa zajednice vršeći nad njom obred pomirenja pred Jahvom.
“Chifukwa chiyani simunadyere pamalo wopatulika nsembe yopepesera machimo ija? Kodi imene ija siyopatulika? Kodi Yehova sanapereke nyamayo kwa inu kuti muchotse machimo a mpingo wonse powachitira mwambo wa nsembe yopepesera machimo pamaso pa Yehova?
18 Budući da krv žrtve nije bila unesena unutar Svetišta, morali ste je blagovati u Svetištu, kako mi je bilo zapovjeđeno.”
Pakuti magazi ake sanalowe nawo ku Malo Wopatulika, mukanadya nyama ya mbuziyo pa malo wopatulikawo monga Yehova analamulira.”
19 Nato će Aron Mojsiju: “Danas su, eto, prinijeli svoju žrtvu okajnicu i svoju žrtvu paljenicu pred Jahvom! Što bi se meni dogodilo da sam ja danas jeo od žrtve okajnice? Bi li to bilo milo Jahvi?”
Aaroni anamuyankha Mose kuti, “Lero anthu apereka nsembe yawo yopepesera machimo ndiponso nsembe yawo yopsereza pamaso pa Yehova komabe zinthu zoterezi zandichitikira. Kodi Yehova akanakondwa ndikanadya nsembe yopepesera machimo lero?”
20 Kad Mojsije to ču, odobri.
Pamene Mose anamva zimenezi, anakhutira.

< Levitski zakonik 10 >