< Jošua 1 >
1 Poslije smrti Mojsija, sluge Jahvina, reče Jahve Jošui, sinu Nunovu, pomoćniku Mojsijevu:
Atamwalira Mose mtumiki wa Mulungu, Yehova anati kwa Yoswa mwana wa Nuni mthandizi wa Mose:
2 “Moj je sluga Mojsije umro; zato sada ustani, prijeđi preko toga Jordana, ti i sav taj narod, u zemlju koju dajem sinovima Izraelovim.
“Mose mtumiki wanga wamwalira. Ndipo iwe ndi anthu onsewa, tsopano konzekani kuwoloka mtsinje wa Yorodani kupita ku dziko limene ndiwapatse Aisraeli onse.
3 Svako mjesto na koje stupi vaša noga dajem vam, kao što obećah Mojsiju.
Paliponse pamene phazi lanu liponde, ndikupatsani monga momwe ndinalonjezera Mose.
4 Od pustinje i od Libanona pa do Velike rijeke, rijeke Eufrata, i sve do Velikog mora na sunčanom zapadu - sve će to biti vaše područje.
Dziko lanu lidzayambira ku chipululu kummwera mpaka ku mapiri a Lebanoni kumpoto, kuchokeranso ku mtsinje waukulu wa Yufurate kummawa, mpaka dziko lonse la Ahiti, kukafika ku Nyanja Yayikulu ya kumadzulo.
5 Nitko neće odoljeti pred tobom u sve dane tvog života; ja ću biti s tobom, kao što sam bio s Mojsijem, i nikada te neću napustiti niti ću te ostaviti.
Palibe munthu amene adzatha kukugonjetsa masiku onse a moyo wako. Monga Ine ndinakhalira ndi Mose, chomwechonso ndidzakhala nawe. Sindidzakusiya kapena kukataya.
6 Budi odvažan i hrabar jer ćeš ti uvesti narod ovaj da primi u baštinu zemlju za koju se zakleh ocima njihovim da ću im je dati.
“Ukhale wamphamvu ndi wolimba mtima, chifukwa iwe udzatsogolera anthu awa kukalandira dziko limene Ine ndinalonjeza makolo awo kuti ndidzawapatsa.
7 Samo budi odvažan i hrabar da sve učiniš vjerno prema naredbama koje ti je dao Mojsije, sluga moj. Ne skreći od toga ni desno ni lijevo da bi ti bilo sretno sve što poduzmeš.
Ukhale wamphamvu ndi wolimba mtima kwambiri. Usamale ndithu kuti umvere malamulo onse amene mtumiki wanga Mose anakupatsa. Usachoke pa malamulo anga ndipo kulikonse kumene udzapite udzapambana.
8 Neka knjiga Zakona bude na ustima tvojim: razmišljaj o njoj danju i noću, kako bi vjerno držao sve što je u njoj napisano: samo ćeš tada biti sretan i uspjet ćeš u pothvatima. Nisam li ti zapovjedio:
Uziwerenga Buku la Malamuloli, uzilingalira zolembedwa mʼmenemo usana ndi usiku, kuti uchite zonse zimene zinalembedwamo. Ukamatero udzapeza bwino ndi kupambana.
9 odvaži se i budi hrabar? Ne boj se i ne strahuj, jer kuda god pođeš, s tobom je Jahve, Bog tvoj.”
Paja ndinakulamula kuti ukhale wamphamvu ndi wolimba mtima. Choncho usamachite mantha kapena kutaya mtima popeza Ine Yehova Mulungu wako ndidzakhala nawe kulikonse kumene udzapite.”
10 Tada zapovijedi Jošua glavarima narodnim:
Tsono Yoswa analamula atsogoleri a Aisraeli nawawuza kuti,
11 “Prođite kroz tabor i proglasite puku ovu zapovijed: 'Spremite sebi brašnenice jer ćete za tri dana prijeći preko Jordana da biste primili u posjed zemlju koju vam Jahve, Bog vaš, daje u baštinu.'”
“Pitani ku misasa yonse ndipo muwuze anthu kuti, ‘Konzekani, mangani katundu wanu, popeza pakapita masiku atatu kuyambira lero mudzawoloka Yorodani kupita kukatenga dziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani.’”
12 Zatim reče Jošua plemenu Rubenovu i Gadovu i polovini plemena Manašeova:
Koma Yoswa anawuza fuko la Rubeni, fuko la Gadi ndi theka la fuko la Manase kuti,
13 “Sjetite se onoga što vam je zapovjedio Mojsije, sluga Jahvin, kada vam je rekao: 'Jahve, Bog vaš, hoće da počinete i daje vam ovu zemlju.
“Kumbukirani zimene Mose mtumiki wa Yehova anakulamulani kuti, ‘Yehova Mulungu wanu akukupatsani mpumulo, ndi dziko ili kuti likhale lanu.’
14 Vaše žene, djeca i stada mogu ostati u zemlji koju vam je dao Mojsije s onu stranu Jordana. Vi pak ratnici, za boj spremni, morate naoružani poći pred svojom braćom da im pomognete,
Tsono akazi anu, ana anu ndi ziweto zanu zitsale mʼdziko lino limene Mose anakupatsani kummawa kwa Yorodani. Koma ankhondo anu okha ndiwo awoloke atatenga zida zawo ndi kupita patsogolo pa abale anu kukawathandiza.
15 sve dok Jahve ne dade da počinu i vaša braća, kao i vi, i dok ne zaposjednu zemlju koju im daje Jahve, Bog vaš. Tada se možete vratiti u zemlju koja vam pripada i koju vam je dao Jahvin sluga Mojsije, na drugoj strani Jordana, prema istoku sunca.'”
Abale anuwo akadzalandira dziko limene Yehova Mulungu wanu akuwapatsa monga inu mwachitira, inu mudzabwerera kudzakhazikika mʼdziko lanu limene Mose mtumiki wa Yehova anakupatsani tsidya la kummawa kwa Yorodani.”
16 Oni odgovore Jošui: “Sve što nam zapovjediš, učinit ćemo, i kuda nas god pošalješ, poći ćemo.
Kenaka iwo anayankha Yoswa kuti, “Ife tidzachita chilichonse chimene mwatilamula, ndipo kulikonse kumene mudzatitume tidzapita.
17 Kao što smo slušali Mojsija, tako ćemo se pokoravati i tebi. Samo neka Jahve, Bog tvoj, bude s tobom kao što bijaše s Mojsijem!
Monga momwe tinamvera Mose kwathunthu, chomwechonso tidzakumvera iwe. Yehova Mulungu wanu akhale nanu monga momwe anachitira ndi Mose.
18 Tko se god usprotivi tvome glasu i ne posluša tvojih riječi u svemu što mu zapovjediš neka bude pogubljen. Samo ti budi odvažan i hrabar!”
Aliyense wotsutsana ndi inu kapena wosamvera zimene mutilamula adzaphedwa. Inu mukhale wamphamvu ndi wolimba mtima!”