< Jošua 3 >
1 Urani Jošua i sa svim sinovima Izraelovim krene od Šitima. I stignu do Jordana pa ondje prije prelaza prenoće.
Yoswa ndi Aisraeli onse anadzuka mmamawa nanyamuka ku Sitimu kupita ku Yorodani. Iwo anagona kumeneko asanawoloke mtsinje wa Yorodaniwo.
2 Poslije tri dana prođu starješine kroz tabor i zapovjede puku:
Patatha masiku atatu, atsogoleri anayendera misasa yonse,
3 “Čim ugledate Kovčeg saveza Jahve, Boga vašega, i svećenike levite koji ga nose, krenite svi sa svoga mjesta i pođite za njim.
kulangiza anthu kuti, “Mukaona ansembe a Chilevi atanyamula Bokosi la Chipangano la Yehova Mulungu wanu, inu munyamuke pa malo ano ndi kumalitsatira.
4 Tako ćete znati put kojim vam je ići, jer tim putem još nikada niste išli. Ali između vas i Kovčega neka bude razmak do dvije tisuće lakata. I da mu se niste približili.”
Potero mudzadziwa njira yoti mudzere, popeza simunayendepo njira ino nʼkale lomwe. Koma musaliyandikire. Pakati pa inu ndi bokosilo pakhale mtunda pafupifupi kilomita imodzi.”
5 A Jošua zapovjedi narodu: “Posvetite se za sutra, jer će sutra Jahve učiniti čudesa među vama.”
Yoswa anawuza anthu kuti, “Dzipatuleni tsono pakuti mawa Yehova adzachita zodabwitsa pakati panu.”
6 A svećenicima Jošua zapovjedi: “Dignite Kovčeg saveza i nosite ga pred narodom.” I digoše Kovčeg saveza i poniješe ga pred narodom.
Mmawa mwake Yoswa ananena kwa ansembe kuti, “Nyamulani Bokosi la Chipangano muwoloke ndipo mukhale patsogolo pa anthu.” Motero iwo analinyamula ndi kupita patsogolo pawo.
7 Jahve reče Jošui: “Danas te počinjem uzvisivati pred očima svega Izraela, neka znaju da sam s tobom kao što bijah s Mojsijem.
Ndipo Yehova anati kwa Yoswa, “Lero Ine ndidzayamba kukukweza pamaso pa Aisraeli onse kuti adziwe kuti ndili nawe monga ndinalili ndi Mose.
8 Ti pak zapovjedi svećenicima koji nose Kovčeg saveza:' Kada stignete do voda jordanskih, u Jordanu se samom zaustavite.'”
Ansembe amene akunyamula Bokosi la Chipangano uwalamule kuti, ‘Mukafika ku mtsinje wa Yorodani mulowe mu mtsinjemo ndi kuyima mʼmphepete.’”
9 Tada reče Jošua Izraelcima: “Priđite i čujte riječi Jahve, Boga svojega.”
Yoswa anati kwa Aisraeli, “Bwerani pano mudzamve mawu a Yehova Mulungu wanu.
10 I reče Jošua: “Po ovomu ćete spoznati da je među vama Bog živi: on će goniti ispred vas Kanaance, Hetite, Hivijce, Perižane, Girgašane, Amorejce i Jebusejce.
Umu ndi mmene mudzadziwira kuti Mulungu wamoyo ali pakati panu. Inu mukamadzapita patsogolo Iye adzathamangitsa Akanaani, Ahiti, Ahivi, Aperezi, Agirigasi, Aamori ndi Ayebusi.
11 Evo, Kovčeg saveza Gospodara sve zemlje proći će pred vama preko Jordana.
Pamenepo, Bokosi la Chipangano la Mbuye wa dziko lonse lapansi lidzawoloka mu Yorodani patsogolo panu.
12 Izaberite odmah dvanaest ljudi iz plemena Izraelovih, po jednoga iz svakoga plemena.
Musankhe amuna khumi ndi awiri kuchokera ku fuko lililonse la Israeli.
13 Čim stopala svećenika koji nose Kovčeg Jahve, Gospodara sve zemlje, stupe u Jordan, razdijelit će se voda Jordana, i ona što teče odozgo ustavit će se kao nasip.'”
Mapazi a ansembe onyamula Bokosi la Yehova, Mbuye wa dziko lapansi, akadzangoponda mu Yorodani, madzi ake onse ochokera ku mtunda adzaleka kuyenda ndipo adzayima ngati chipupa.”
14 Kad je narod krenuo iz svojih šatora da prijeđe preko Jordana, ponesu svećenici Kovčeg saveza pred njim.
Tsono Aisraeli anachoka ku misasa yawo kukawoloka mtsinje wa Yorodani. Ansembe onyamula Bokosi la Chipangano ndiwo anatsogolera anthuwo.
15 A kad su nosači Kovčega stigli do Jordana i kada su svećenici koji su nosili Kovčeg zagazili u vodu na obali - a bilo je vrijeme žetve kad se Jordan prelijeva preko svojih obala -
Nyengo imeneyi inali yokolola ndipo mtsinje wa Yorodani umakhala wodzaza. Komabe, ansembe onyamula Bokosi la Chipangano anafika ku Yorodani, ndipo atangoponda mʼmadzimo,
16 voda što je tekla odozgo daleko se, poput nasipa, ustavila kod grada Adame, koji se nalazi kraj Sartana; a voda što je otjecala dolje u Arabsko ili Slano more sasvim je otekla i narod je prelazio prema Jerihonu.
madzi ochokera ku mtunda anasiya kuyenda. Madzi a Yorodani ochokera ku mtunda anawunjikana pamodzi ngati khoma lalitali pa mtunda wautali ndithu ndi mzinda wa Adama chapafupi ndi mzinda wa Zaretani. Madzi othamangira ku nyanja ya Araba, ngakhalenso amene amachokera kuti Nyanja ya Mchere amathera pamenepo. Choncho anthu anawoloka tsidya lina moyangʼanana ndi Yeriko.
17 Svećenici koji su nosili Kovčeg saveza Jahvina stajahu na suhu usred Jordana i prelažaše Izrael po suhu sve dok sav narod ne prijeđe preko rijeke.
Ansembe onyamula Bokosi la Chipangano la Yehova anali chiyimire powuma, pakati pa Yorodani pamene Aisraeli amawoloka mpaka gulu lonse linamaliza kuwoloka powuma.