< Jošua 18 >
1 Sabrala se zajednica sinova Izraelovih u Šilo, i ondje razapeše Šator sastanka. Sva im se zemlja pokorila.
Atagonjetsa dziko lonse Aisraeli anasonkhana ku Silo ndipo anayimikako tenti ya msonkhano.
2 Ali ostade među sinovima Izraelovim još sedam plemena koja nisu primila svoje baštine.
Koma pa nthawiyo nʼkuti mafuko asanu ndi awiri a Aisraeli asanalandire cholowa chawo.
3 Tada im reče Jošua: “Dokle ćete oklijevati da pođete i zaposjednete zemlju koju vam je dao Jahve, Bog vaših otaca?
Ndipo Yoswa anati kwa Aisraeli, “Kodi mudikira mpaka liti kuti mulowe ndi kulanda dziko limene Yehova Mulungu wa makolo anu wakupatsani?
4 Izaberite po tri čovjeka iz svakoga plemena, a ja ću ih poslati da popišu svu zemlju za diobu. Kad se vrate k meni,
Sankhani amuna atatu kuchokera ku fuko lililonse ndipo ine ndidzawatuma kuti akayendere dzikolo ndi kukalilembera bwino kuti ndiligawe kukhala lawo. Akatero, abwererenso kwa ine.
5 razdijelit ću zemlju na sedam dijelova. Neka Juda ostane na svome području na jugu, a Josipov dom neka ostane u svome kraju na sjeveru.
Aligawe dzikolo mʼzigawo zisanu ndi ziwiri; fuko la Yuda lidzakhale ndi dziko lake la kummwera ndi nyumba ya Yosefe ikhalebe mʼdziko lawo la kumpoto.
6 A vi raspišite zemlju na sedam dijelova i donesite mi amo da bacim ždrijeb za vas ovdje pred Jahvom, Bogom našim.
Mudzalembe mawu ofotokoza za zigawo zisanu ndi ziwiri za dzikolo, ndi kubwera nawo kwa ine. Tsono ineyo ndidzakuchitirani maere pamaso pa Yehova Mulungu wanu.
7 Leviti neće imati dijela među vama jer je svećeništvo Jahvino njihova baština; a Gad, Ruben i polovina plemena Manašeova primili su svoju baštinu na istočnoj strani Jordana - onu koju im je dao Mojsije, sluga Jahvin.”
Alevi asakhale ndi dziko pakati panu, chifukwa gawo lawo ndi kutumikira Yehova pa ntchito ya unsembe. Ndipo Gadi, Rubeni ndi theka la fuko la Manase analandira kale cholowa chawo kummawa kwa Yorodani. Mose mtumiki wa Yehova ndiye anawapatsa.”
8 Spreme se ti ljudi na put, a Jošua zapovjedi onima koji su pošli popisati zemlju: “Idite i obiđite svu zemlju i opišite je, pa se onda vratite k meni da bacim ždrijeb ovdje pred Jahvom u Šilu.”
Anthuwo akupita kukalembera dzikolo, Yoswa anawalangiza kuti, “Pitani mukayendere ndi kulembera dzikolo. Kenaka mukabwere kwa ine, ndidzakuchitirani maere kuno ku Silo pamaso pa Yehova.”
9 Odoše oni ljudi, prođoše zemljom i u knjigu popisaše sve gradove u sedam dijelova, pa se vratiše k Jošui u tabor u Šilu.
Ndipo anthu anachoka ndi kukayendera dziko lonse. Iwo analemba bwinobwino mʼbuku za dzikolo, mzinda ndi mzinda. Analigawa magawo asanu ndi awiri, ndipo anabwerera kwa Yoswa ku misasa ya ku Silo.
10 A Jošua baci za njih ždrijeb u Šilu pred Jahvom i ondje razdijeli Jošua zemlju sinovima Izraelovim po njihovim dijelovima plemenskim.
Pambuyo pake Yoswa anawachitira maere ku Silo pamaso pa Yehova, ndipo fuko lililonse la Israeli analigawira dziko lake.
11 I pade ždrijeb na pleme sinova Benjaminovih po njihovim porodicama: utvrdi se da je njihov dio između dijela sinova Judinih i sinova Josipovih.
Maere anagwera mabanja a fuko la Benjamini. Dziko limene anapatsidwa linali pakati pa fuko la Yuda ndi fuko la Yosefe:
12 Sjeverna im se međa protezala od Jordana te išla uza sjeverni obronak Jerihona, uspinjala se sa zapada na goru i završavala se u pustinji Bet-Avenu.
Mbali ya kumpoto malire awo anayambira ku Yorodani nalowera chakumpoto kwa matsitso a ku Yeriko kulowera cha kumadzulo kwa dziko la ku mapiri ndi kukafika ku chipululu cha Beti-Aveni.
13 Odatle je išla k Luzu, k južnom obronku Luza, to jest Betela; spuštala se zatim u Atrot-Adar, kraj brda koje je južno od Donjeg Bet-Horona.
Kuchokera kumeneko malirewo analoza ku Luzi nadutsa mʼmbali mwa mapiri kummwera kwa Luzi (ndiye Beteli) ndipo anatsika mpaka ku Ataroti Adari, ku mapiri a kummwera kwa Beti-Horoni wa Kumunsi.
14 Međa se dalje savijala i okretala sa zapada prema jugu, od gore koja se diže nasuprot Bet-Horonu s juga, i svršavala se kod Kirjat Baala, danas Kirjat Jearima, grada sinova Judinih. To je zapadna strana.
Ndipo malirewo analowanso kwina, analunjika kummwera kuchokera kumadzulo kwake kwa phiri loyangʼanana ndi Beti-Horoni, mpaka ku mzinda wa Kiriyati Baala (ndiye Kiriati Yearimu), mzinda wa anthu a fuko la Yuda. Amenewa ndiye anali malire a mbali ya kumadzulo.
15 Južna se strana počinjala od granice Kirjat Jearima, pa se pružala na zapad k vrelu Neftoahu;
Malire a kummwera anayambira mʼmphepete mwenimweni mwa Kiriati Yearimu napita kumadzulo mpaka kukafika ku akasupe a Nefitowa.
16 potom se spuštala međa do kraja gore koja je prema dolini Ben-Hinomu, na sjeveru refaimske nizine, silazila zatim u dolinu Hinom uz Jebusejski obronak i dosegla do izvora Rogela.
Malire anatsikira mʼmphepete mwa phiri loyangʼanana ndi chigwa cha Beni Hinomu, kumpoto kwa chigwa cha Refaimu. Anapitirira kutsikira ku chigwa cha Hinomu kummwera kwa chitunda cha Ayebusi mpaka ku Eni Rogeli.
17 Zatim se savijala od sjevera te izlazila na En-Šemeš i doticala Gelilot, koji se diže prema Adumimskom usponu, i silazila na Kamen Bohana, sina Rubenova.
Kenaka anakhotera kumpoto kupita ku Eni-Semesi, kupitirira mpaka ku Geliloti amene amayangʼanana ndi pokwera pa Adumimu. Kenaka malire anatsikira ku Mwala wa Bohani, mwana wa Rubeni.
18 Prolazila je zatim obronkom sa sjeverne strane prema Bet-Haarabi i silazila do Arabe.
Anabzola cha kumpoto kwa chitunda cha Beti Araba ndi kutsikabe mpaka ku chigwa cha Yorodani.
19 Dalje je tekla međa uz obronak Bet-Hogle prema sjeveru i svršavala se na sjevernom Jeziku Slanog mora, do južnog kraja Jordana. To je južna međa.
Anabzolanso cha kumpoto kwa chitunda cha Beti-Hogila kukafika cha kumpoto ku gombe la Nyanja ya Mchere kumene mtsinje wa Yorodani umathirirako, cha kummwera kwenikweni. Awa anali malire a kummwera.
20 Jordan je pak bio međa s istočne strane. To je baština sinova Benjaminovih, s njihovim međama unaokolo po porodicama njihovim.
Yorodani ndiye anali malire a mbali ya kummawa. Awa anali malire a dziko limene mabanja a fuko la Benjamini analandira.
21 Gradovi plemena sinova Benjaminovih po porodicama njihovim jesu: Jerihon, Bet-Hogla, Emek Kesis;
Mabanja a fuko la Benjamini anali ndi mizinda iyi; Yeriko, Beti-Hogila, Emeki Kezizi,
22 Bet-Haaraba, Samarajim, Betel;
Beti-Araba, Zemaraimu, Beteli
24 Kefar Haamona, Ofni i Gaba: dvanaest gradova s njihovim selima.
Kefari-Amoni, Ofini ndi Geba, mizinda khumi ndi awiri ndi midzi yake
Panalinso Gibiyoni, Rama, Beeroti,
27 Rekem, Jirpeel, Tarala;
Rekemu, Iripeeli, Tarala,
28 Sela Haelef, Jebus (to je Jeruzalem), Gibat i Kirjat: četrnaest gradova s njihovim selima. To je baština sinova Benjaminovih po porodicama njihovim.
Zera Haelefu, mzinda wa Ayebusi (ndiye kuti Yerusalemu) Gibeya ndi Kiriati, mizinda 14 ndi midzi yake. Limeneli ndilo dziko limene mabanja a fuko la Benjamini analandira kuti likhale lawo.