< Job 7 >
1 Nije l' vojska život čovjekov na zemlji? Ne provodi l' dane poput najamnika?
“Kodi munthu sakhala ndi ntchito yowawa pa dziko lapansi? Kodi masiku ake sali ngati munthu waganyu?
2 Kao što trudan rob za hladom žudi, poput nadničara štono plaću čeka,
Monga ngati kapolo wolakalaka mthunzi wa nthawi yamadzulo, kapena ngati munthu waganyu woyembekezera malipiro ake,
3 mjeseci jada tako me zapadoše i noći su mučne meni dosuđene.
choncho ine ndapatsidwa nthawi yongovutika pachabe, ndiponso usiku wamasautso wapatsidwa kwa ine.
4 Liježuć' mislim svagda: 'Kada ću ustati?' A dižuć se: 'Kada večer dočekati!' I tako se kinjim sve dok se ne smrkne.
Ndikamagona ndimaganiza kuti, ‘Kodi kucha liti?’ Usikuwo umatalika ndipo sindigona tulo mpaka mmawa.
5 PÓut moju crvi i blato odjenuše, koža na meni puca i raščinja se.
Thupi langa ladzala mphutsi ndi zipsera, khungu langa langʼambika ndipo likutuluka mafinya.
6 Dani moji brže od čunka prođoše, promakoše hitro bez ikakve nade.
“Masiku anga ndi othamanga kupambana makina wolukira nsalu, ndipo amatha wopanda chiyembekezo.
7 Spomeni se: život moj je samo lahor i oči mi neće više vidjet' sreće!
Inu Mulungu kumbukirani kuti moyo wanga uli ngati mpweya; sindidzaonanso masiku achisangalalo.
8 Prijateljsko oko neće me gledati; pogled svoj u mene upro si te sahnem.
Amene akundiona tsopano akundiona; mudzandifunafuna koma sindidzapezekanso.
9 Kao što se oblak gubi i raspline, tko u Šeol siđe, više ne izlazi. (Sheol )
Monga mtambo umazimirira ndi kukanganuka, momwemonso munthu amene walowa mʼmanda sabwerera. (Sheol )
10 Domu svome natrag ne vraća se nikad, njegovo ga mjesto više ne poznaje.
Iye sadzabweranso ku nyumba kwake ndipo onse omudziwa adzamuyiwala.
11 Ustima ja svojim stoga branit' neću, u tjeskobi duha govorit ću sada, u gorčini duše ja ću zajecati.
“Nʼchifukwa chake ine sindidzakhala chete; ndidzayankhula mopsinjika mtima, ndidzadandaula mowawidwa mtima.
12 Zar sam more ili neman morska, pa si stražu nada mnom stavio?
Kodi ine ndine nyanja kapena chirombo chamʼnyanja kuti inu mundiyikire alonda?
13 Kažem li: 'Na logu ću se smirit', ležaj će mi olakšati muke',
Pamene ndikuganiza kuti ndidzapeza chitonthozo pa bedi panga ndipo pogona panga padzachepetsa madandawulo anga,
14 snovima me prestravljuješ tada, prepadaš me viđenjima mučnim.
ngakhale nthawi imeneyo mumandiopseza ndi maloto ndi kundichititsa mantha ndi masomphenya,
15 Kamo sreće da mi se zadavit'! Smrt mi je od patnja mojih draža.
kotero kuti ndimalakalaka kudzikhweza kapena kufa, kupambana kupirira zowawa zimene ndikuzimva mʼthupi mwanga.
16 Ja ginem i vječno živjet neću; pusti me, tek dah su dani moji!
Ine ndatopa nawo moyo wanga; sindingakonde kukhala moyo nthawi zonse. Ndisiyeni ndekha pakuti moyo wanga ulibe tanthauzo.
17 Što je čovjek da ga toliko ti cijeniš, da je srcu tvojem tako prirastao
“Kodi munthu nʼchiyani kuti muzimuganizira chotere, kuti muzisamala zochita zake,
18 i svakoga jutra da njega pohodiš i svakoga trena da ga iskušavaš?
kuti muzimusanthula mmawa uliwonse ndi kumamuyesa nthawi yonse?
19 Kada ćeš svoj pogled skinuti sa mene i dati mi barem pljuvačku progutat'?
Kodi simudzaleka kumandizonda kuti ndipezeko mpata wopumula?
20 Ako sam zgriješio, što učinih tebi, o ti koji pomno nadzireš čovjeka? Zašto si k'o metu mene ti uzeo, zbog čega sam tebi na teret postao?
Ngati ine ndachimwa, ndachita chiyani kwa Inu, Inu wopenyetsetsa anthu? Chifukwa chiyani mwachititsa kuti ndikhale ngati choponyera chandamale chanu? Kodi ndasanduka katundu wolemera kwa Inu?
21 Zar prijestupa moga ne možeš podnijeti i ne možeš prijeći preko krivnje moje? Jer, malo će proći i u prah ću leći, ti ćeš me tražiti, al' me biti neće.”
Chifukwa chiyani simukundikhululukira zolakwa zanga ndi kundichotsera machimo anga? Pakuti posachedwa ndilowa mʼmanda; mudzandifunafuna ine koma simudzandionanso.”