< Job 42 >
1 A Job ovako odgovori Jahvi:
Pamenepo Yobu anayankha Yehova kuti,
2 “Ja znadem, moć je tvoja bezgranična: što god naumiš, to izvesti možeš.
“Ndikudziwa kuti Inu mungathe kuchita zinthu zonse; chimene mufuna kuchita wina sangaletse konse.
3 Tko je taj koji riječima bezumnim zamračuje božanski promisao? Govorah stoga, ali ne razumjeh, o čudesima meni neshvatljivim.
Munandifunsa kuti, ‘Kodi ndiwe yani amene ukufuna kusokoneza uphungu wanga ndi mawu opanda nzeru? Zoonadi ndinayankhula zimene sindinazimvetse, zinthu zodabwitsa kwambiri kwa ine zimene sindinazidziwe.
4 O, poslušaj me, pusti me da zborim: ja ću te pitat', a ti me pouči.
“Inu munandiwuza kuti, ‘Mvetsetsa tsopano ndipo ndidzayankhula; ndidzakufunsa ndipo iwe udzandiyankhe.’
5 Po čuvenju tek poznavah te dosad, ali sada te oči moje vidješe.
Ndinkangomva za Inu ndi makutu anga, koma tsopanonso ndakuonani ndi maso anga.
6 Sve riječi svoje zato ja poričem i kajem se u prahu i pepelu.”
Nʼchifukwa chake ndi kuchita manyazi, ndikulapa podzithira fumbi ndi phulusa.”
7 Kada Jahve izgovori Jobu ove riječi, reče on Elifazu Temancu: “Ti i tvoja dva prijatelja raspalili ste gnjev moj jer niste o meni onako pravo govorili kao moj sluga Job.
Yehova atayankhula ndi Yobu mawu amenewa anawuza Elifazi wa ku Temani kuti, “Ine ndakukwiyira pamodzi ndi abwenzi ako awiri, chifukwa simunayankhule zabwino za Ine, monga mmene wayankhulira mtumiki wanga Yobu.
8 Zato uzmite sada sedam junaca i sedam ovnova i pođite k mome sluzi Jobu, pa prinesite za sebe paljenicu, a sluga moj Job molit će se za vas. Imat ću obzira prema njemu i neću vam učiniti ništa nažao zato što niste o meni onako pravo govorili kao moj sluga Job.”
Kotero tsopano mutenge ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri ndi nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri ndi kupita nazo kwa mtumiki wanga Yobu kuti mukapereke nsembe zopsereza. Mtumiki wanga Yobu adzakupemphererani, ndipo Ine ndidzalandira pemphero lake. Sindidzakuchitirani kanthu molingana ndi uchitsiru wanu. Inu simunayankhule zabwino za Ine, monga anayankhulira Yobu mtumiki wanga.”
9 Tada odoše Elifaz iz Temana, Bildad iz Šuaha i Sofar iz Naamata i učiniše kako im je Jahve zapovjedio. I Jahve se obazre na Joba.
Motero Elifazi wa ku Temani, Bilidadi wa ku Suki ndi Zofari wa ku Naama anachita zimene Yehova anawawuza ndipo Yehova anamvera pemphero la Yobu.
10 I Jahve vrati Joba u prijašnje stanje jer se založio za svoje prijatelje, pa mu još udvostruči ono što je posjedovao.
Yobu atawapempherera abwenzi ake aja, Yehova anamubwezera chuma chake ndipo anamupatsa mowirikiza kuposa zomwe anali nazo kale.
11 Tad se vratiše Jobu sva njegova braća, i sve njegove sestre, i svi prijašnji znanci te su jeli s njim kruh u njegovoj kući, žaleći ga i tješeći zbog svih nevolja što ih Jahve bijaše na nj poslao. Svaki mu darova po jedan srebrnik i po jedan zlatan prsten.
Abale ake ndi alongo ake onse, kuphatikizapo onse amene ankamudziwa kale, amabwera kwa iye nʼkudzadya naye chakudya mʼnyumba mwake. Iwo anamutonthoza ndi kumupepesa chifukwa cha mavuto onse amene Yehova analola kuti amugwere. Aliyense wa iwowa anamupatsa ndalama ndi mphete yagolide.
12 Jahve blagoslovi novo Jobovo stanje još više negoli prijašnje. Blago mu je brojilo četrnaest tisuća ovaca, šest tisuća deva, tisuću jarmova volova i tisuću magarica.
Yehova anadalitsa Yobu pa masiku ake otsirizawa kupambana poyamba paja. Iye anali ndi nkhosa 14,000, ngamira 6,000, ngʼombe zantchito 2,000 ndi abulu aakazi 1,000.
13 Imao je sedam sinova i tri kćeri.
Anaberekanso ana aamuna asanu ndi awiri ndi ana aakazi atatu.
14 Prvoj nadjenu ime Jemima, drugoj Kasija, a trećoj Keren-Hapuk.
Mwana wake wamkazi woyamba anamutcha Yemima, wachiwiri anamutcha Keziya, wachitatu anamutcha Kereni Hapuki.
15 U svem onom kraju ne bijaše žena tako lijepih kao Jobove kćeri. I otac im dade jednaku baštinu kao i njihovoj braći.
Mʼdziko monsemo munalibe akazi okongola ngati ana a Yobu, ndipo abambo awo anawapatsa cholowa pamodzi ndi alongo awo.
16 Poslije toga Job doživje dob od sto četrdeset godina i vidje djecu svoju i djecu svoje djece do četvrtog koljena.
Zitachitika zimenezi, Yobu anakhala ndi moyo zaka 140. Iye anaona zidzukulu zake mpaka mʼbado wachinayi.
17 Potom umrije Job, star, nauživši se života.
Potsiriza, Yobu anamwalira ali nkhalamba ya zaka zochuluka kwambiri.