< Job 39 >
1 Znaš li kako se legu divokoze? Vidje li kako se mlade košute?
“Kodi iwe umadziwa nthawi imene mbalale yayikazi imaswera? Kodi umaonerera pamene nswala ikubala?
2 Izbroji li koliko nose mjeseci, znaš li u koje doba se omlade?
Kodi umawerenga miyezi imene zimakhala ndi bere? Kodi nthawi imene zimaswana iwe umayidziwa?
3 Sagnuvši se, polegu lanad svoju i breme usred pustinje odlažu,
Zimakhala tsonga ndi kuswa ana awo; pamenepo ululu wobereka nʼkutha.
4 a kad im porod ojača, poraste, ostave ga i ne vraćaju mu se.
Ana a nyamazi amakhala ndi mphamvu ndipo amakulira mʼthengo; kenaka amachoka ndipo sabwereranso.
5 Tko dade divljem magarcu slobodu i tko to oglav skinu njemu s glave?
“Kodi bulu wakuthengo amamupatsa ndani ufulu wongodziyendera? Ndani amamasula zingwe zake?
6 U zavičaj mu dadoh ja pustinju i polja slana da ondje živuje.
Ine ndinamupatsa chipululu kuti chikhale mudzi wake, nthaka ya mchere kuti ikhale malo ake okhalamo
7 Buci gradova on se podruguje i ne sluša goničevih povika.
Iye amakhala kutali ndi phokoso la mu mzinda; ndipo samva kufuwula kwa oyendetsa nyama zakatundu.
8 Luta brdima, svojim pašnjacima, u potrazi za zeleni svakakvom.
Amayendayenda mʼmapiri kudya msipu ndipo amafunafuna msipu uliwonse wobiriwira.
9 Možeš li slugom učinit' bivola, zadržat' ga noć jednu za jaslama?
“Kodi njati ingavomere kukutumikira? Kodi ingagone mu gome lako usiku?
10 Možeš li njega za brazdu prikovat' da ralo vuče po docima tvojim?
Kodi ungathe kuyimanga ndi zingwe kuti izilima? Kodi ingasalaze nthumbira mʼmunda mwako?
11 Možeš li se osloniti na njega jer je njegova snaga prevelika i prepustit' mu težak svoj posao?
Kodi ungadalire njatiyo chifukwa champhamvu zake? Kodi ungayilekere kuti igwire ntchito zako zolemetsa?
12 Misliš li tebi da će se vratiti i na gumno ti dotjerati žito?
Kodi ungadalire kuti idzakubweretsera tirigu wako ndi kumuyika ku malo opunthira?
13 Krilima svojim noj trepće radosno, iako krila oskudnih i perja.
“Nthiwatiwa imakupiza mapiko ake monyadira, koma mapikowo sangafanane ndi mapiko ndi nthenga za kakowa.
14 On svoja jaja na zemlji ostavlja, povjerava ih pijesku da ih grije,
Nthiwatiwa imakwirira mazira ake pansi ndipo amafundidwa ndi nthaka,
15 ne mareć' što ih zgazit' može noga ili nekakva divlja zvijer zgnječiti.
nthiwatiwayo sidera nkhawa kuti mazira ake angathe kuswanyidwa, ndi kuti nyama zakuthengo zitha kuwaponda.
16 S nojićima k'o s tuđima postupa; što mu je trud zaludu, on ne mari.
Nthiwatiwa imachitira nkhanza ana ake ngati anawo si ake; Imayiwala zoti inavutika powabala.
17 Jer Bog je njega lišio pameti, nije mu dao nikakva razbora.
Chifukwa Mulungu anayimana nzeru, simvetsa kanthu kalikonse.
18 Ali kada na let krila raširi, tada se ruga konju i konjaniku.
Komatu nthiwatiwa ikadzambatuka ndi kuyamba kuthamanga, imamusiya kutali kavalo ndi wokwerapo wake.
19 Zar si ti konja obdario snagom zar si mu ti vrat grivom ukrasio?
“Kodi ndiwe amene umamupatsa mphamvu kavalo kapena kumuveka chenjerere mʼkhosi mwake?
20 Zar ti činiš da skače k'o skakavac, da u strah svakog nagoni hrzanjem?
Kodi ndiwe amene umalipatsa dzombe ulemerero wolumphira, ukali wake nʼkumachititsa mantha?
21 Kopitom zemlju veselo raskapa, neustrašivo srlja na oružje.
Iye amalumphalumpha moopseza, kukondwerera mphamvu zake, ndipo amapita ku nkhondo ndi mphamvu zake zonse.
22 Strahu se ruga, ničeg se ne boji, ni pred mačem uzmaknuti neće.
Iye sachita mantha, saopa chilichonse; sabwerera mʼmbuyo akaona lupanga.
23 Na sapima mu zvekeće tobolac, koplje sijeva i ubojna sulica.
Zida zankhondo zimachita kwichikwichi mʼchimake pambali pake pamodzi ndi mkondo wonyezimira ndi nthungo.
24 Bijesan i nestrpljiv guta prostore; kad rog zasvira, tko će ga zadržat':
Kavaloyo amanjenjemera ndi ukali ndi kulumphalumpha; satha kungoyima pamene wamva kulira kwa lipenga.
25 na svaki zvuk roga on zarže: Ha! Izdaleka on ljuti boj već njuši, viku bojnu i poklič vojskovođa.
Lipenga likalira amati, ‘Twee!’ Amamva fungo la nkhondo ali patali, kufuwula kwa anthu olamulira nkhondo ndi mfuwu wankhondo.
26 Zar po promislu tvojem lijeće soko i prema jugu krila svoja širi?
“Kodi kabawi amawuluka ndi nzeru zako, ndi kutambasula mapiko ake kupita kummwera?
27 Zar se na nalog tvoj diže orao i vrh timora gnijezdo sebi vije?
Kodi umalamulira chiwombankhanga ndiwe kuti chiziwuluka ndi kumanga chisa chake pamwamba penipeni?
28 Na litici on stanuje i noćÄi, na grebenima vrleti visokih.
Chimakhala pa phiri ndipo chimakhala pamenepo usiku; chimakhala pa msonga penipeni pa mwala.
29 Odatle na plijen netremice vreba, oči njegove vide nadaleko.
Chili pamenepo chimayangʼanayangʼana choti chigwire kuti chidye; maso ake amachionera patali chinthucho.
30 Krvlju se hrane njegovi orlići; gdje je ubijenih, tamo je i on.”
Ana ake amayamwa magazi, ndipo kumene kuli mitembo ndiko chimapezeka.”